Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Beginning

Read the Bible from start to finish, from Genesis to Revelation.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Yesaya 5-8

Nyimbo ya Munda Wamphesa

Ndidzamuyimbira bwenzi langa
    nyimbo yokamba za munda wake wa mpesa:
Wokondedwa wanga anali ndi munda wamphesa
    pa phiri la nthaka yachonde.
Anatipula nachotsa miyala yonse
    ndipo anawokamo mipesa yabwino kwambiri.
Anamanga nsanja yolondera pakati pa mundawo
    ndipo anasemanso mopsinyira mphesa mʼmundamo.
Ndipo iye anayembekezera kuti mundawo udzabala mphesa zabwino,
    koma ayi, unabala mphesa zosadya.

“Tsopano, inu amene mumakhala mu Yerusalemu ndi inu anthu a ku Yuda,
    weruzani pakati pa ine ndi munda wanga wa mpesawu.
Kodi nʼchiyaninso china chimene ndikanachitira munda wanga wa mpesa
    kupambana chomwe ndawuchitira kale?
Pamene ndinkayembekezera kuti udzabala mphesa zabwino,
    bwanji unabala mphesa zosadya?
Tsopano ndikuwuzani
    chimene ndidzawuchitire munda wanga wa mpesa:
ndidzachotsa mpanda wake,
    ndipo mundawo udzawonongeka;
ndidzagwetsa khoma lake,
    ndipo nyama zidzapondapondamo.
Ndidzawusandutsa tsala,
    udzakhala wosatengulira ndi wosalimira
    ndipo mudzamera mkandankhuku ndi minga ina.
Ndidzalamula mitambo
    kuti isagwetse mvula pa mundapo.”

Munda wamphesa wa Yehova Wamphamvuzonse
    ndi Aisraeli,
ndipo anthu a ku Yuda ndiwo
    minda yake yomukondweretsa.
Ndipo Iye ankayembekezera chiweruzo cholungama, mʼmalo mwake anaona kuphana;
    mʼmalo mwa chilungamo Iye anamva kulira kwa anthu ozunzika.

Tsoka ndi Chiweruzo

Tsoka kwa inu amene mumangokhalira kulumikiza nyumba,
    ndipo mumangokhalira kuwonjezera minda,
mpaka mutalanda malo onse
    kuti muzikhalamo nokha mʼdzikomo.

Yehova Wamphamvuzonse wayankhula ine ndikumva kuti,

“Ndithudi nyumba zambirizo zidzasanduka mabwinja,
    nyumba zazikulu zokongolazo zidzakhala zopanda anthu.
10 Munda wamphesa wa maekala khumi udzatulutsa vinyo wodzaza mbiya imodzi,
    kufesa madengu khumi a mbewu, zokolola zake zidzangodzaza dengu limodzi.”

11 Tsoka kwa iwo amene amadzuka mmamawa
    nathamangira chakumwa choledzeretsa,
amene amamwa mpaka usiku
    kufikira ataledzera kotheratu.
12 Pa maphwando awo pamakhala azeze, apangwe,
    matambolini, zitoliro ndi vinyo,
ndipo sasamala ntchito za Yehova,
    salemekeza ntchito za manja ake.
13 Motero anthu anga adzatengedwa ukapolo
    chifukwa cha kusamvetsa zinthu;
atsogoleri awo olemekezeka adzafa ndi njala,
    ndipo anthu wamba ochuluka adzafa ndi ludzu.
14 Nʼchifukwa chake ku manda sikukhuta
    ndipo kwayasama kwambiri kukamwa kwake;
mʼmandamo mudzagweranso anthu otchuka a mu Yerusalemu pamodzi ndi anthu wamba ochuluka;
    adzagweramo ali wowowo, nʼkuledzera kwawoko.
15 Ndipo munthu aliyense adzatsitsidwa,
    anthu onse adzachepetsedwa,
    anthu odzikuza adzachita manyazi.
16 Koma Yehova Wamphamvuzonse adzalemekezedwa chifukwa cha chiweruzo chake cholungama.
    Ndipo Mulungu woyera adzadzionetsa kuti ndi woyera pochita chilungamo chake.
17 Tsono nkhosa zidzadya pamenepo ngati pabusa pawo;
    ana ankhosa adzadya mʼmabwinja a anthu olemera.

18 Tsoka kwa amene amadzikokera tchimo ndi zingwe zachinyengo,
    ndipo amadzikokera zoyipa ndi zingwe zokokera ngolo,
19 amene amanena kuti, “Yehova afulumire,
    agwire ntchito yake mwamsanga
    kuti ntchitoyo tiyione.
Ntchito zionekere,
    zimene Woyerayo wa Israeli akufuna kuchita,
    zichitike kuti tizione.”

20 Tsoka kwa amene zoyipa amaziyesa zabwino
    ndipo zabwino amaziyesa zoyipa,
amene mdima amawuyesa kuwala
    ndipo kuwala amakuyesa mdima,
amene zowawasa amaziyesa zotsekemera
    ndipo zotsekemera amaziyesa zowawasa.

21 Tsoka kwa amene amadziona ngati anzeru
    ndipo amadziyesa ochenjera.

22 Tsoka kwa zidakwa zimene zimayika mtima pa vinyo
    ndipo ndi akatswiri posakaniza zakumwa,
23 amene amamasula olakwa chifukwa cha chiphuphu
    koma amayipitsa mlandu wa munthu wosalakwa.
24 Nʼchifukwa chake monga momwe moto umawonongera chiputu
    ndipo monga momwe udzu wowuma umapsera mʼmalawi a moto,
momwemonso mizu yawo idzawola
    ndipo maluwa awo adzafota ndi kuwuluka ngati fumbi;
chifukwa akana malamulo a Yehova Wamphamvuzonse,
    ndipo anyoza mawu a Woyerayo wa Israeli.
25 Nʼchifukwa chake mkwiyo wa Yehova wayakira anthu ake;
    watambasula dzanja lake pa anthuwo ndipo akuwakantha
Mapiri akugwedezeka,
    ndipo mitembo ya anthu yangoti mbwee mʼmisewu ngati zinyalala.

Komabe ngakhale watero, mkwiyo wake sunaleke,
    dzanja lake likanali chitambasulire;

26 Yehova wakweza mbendera kuyitana mtundu wa anthu akutali,
    akuyitana anthuwo ndi likhweru kuti abwere kuchokera ku mathero a dziko lapansi.
Awo akubwera,
    akubweradi mofulumira kwambiri!
27 Palibe ndi mmodzi yemwe amene akutopa kapena kupunthwa,
    palibe amene akusinza kapena kugona;
palibe lamba wa mʼchiwuno amene akumasuka,
    palibe chingwe cha nsapato chimene chaduka.
28 Mivi yawo ndi yakuthwa,
    mauta awo onse ndi okoka,
ziboda za akavalo awo nʼzolimba ngati mwala wansagalabwi,
    magaleta awo ndi aliwiro ngati kamvuluvulu.
29 Kufuwula kwawo kuli ngati kubangula kwa mkango,
    amabangula ngati misona ya mkango;
imadzuma pamene ikugwira nyama
    ndipo imapita nayo popanda ndi mmodzi yemwe woyipulumutsa.
30 Tsiku limenelo mitundu ya anthu idzabangula
    ngati mkokomo wa madzi a mʼnyanja.
Ndipo wina akakayangʼana dzikolo
    adzangoona mdima ndi zovuta;
    ngakhale kuwala kudzasanduka mdima chifukwa cha mitambo.

Masomphenya a Yesaya

Chaka chimene mfumu Uziya anamwalira, ndinaona Ambuye atakhala pa mpando waufumu, wautali ndi wokwezedwa, ndipo mkanjo wawo unali wautali; kotero kuti unadzaza mʼNyumba ya Yehova. Pamwamba pawo panayimirira Aserafi, aliyense anali ndi mapiko asanu ndi limodzi: awiri anaphimba nkhope zawo, awiri anaphimba mapazi awo, ndipo awiri ankawulukira. Ndipo Aserafiwo amafuwulirana kuti

“Woyera, woyera, woyera Yehova Wamphamvuzonse.
    Dziko lonse lapansi ladzaza ndi ulemerero wake.”

Chifukwa cha kufuwulako maziko a zitseko ndi ziwundo anagwedezeka ndipo mʼNyumba ya Yehova munadzaza utsi.

Tsono ine ndinafuwula kuti, “Tsoka langa ine! Ndatayika! Pakuti ndine munthu wapakamwa poyipa, ndipo ndimakhala pakati pa anthu a pakamwa poyipa, ndipo ndi maso anga ndaona mfumu Yehova Wamphamvuzonse.”

Pomwepo mmodzi mwa Aserafi aja anawulukira kwa ine ali ndi khala lamoto mʼdzanja lake, khala limene analichotsa ndi mbaniro pa guwa lansembe. Ndipo anandikhudza pakamwa panga ndi khala lamotolo nati, “Taona ndakhudza pa milomo yako ndi khalali; kulakwa kwako kwachotsedwa, machimo ako akhululukidwa.”

Kenaka ndinamva mawu a Ambuye akuti, “Kodi ndidzatuma yani? Ndipo ndani adzapite mʼmalo mwathu?”

Ndipo ine ndinati, “Ndilipo. Tumeni!”

Yehova anati, “Pita ndipo ukawawuze anthu awa:

“ ‘Kumva muzimva, koma osamvetsetsa;
    kupenya muzipenya koma osaona kanthu.’
10 Tsono anthu amenewa uwaphe mtima;
    uwagonthetse makutu,
    ndipo uwatseke mʼmaso.
Mwina angaone ndi maso awo,
    angamve ndi makutu awo,
    angamvetse ndi mitima yawo,
kenaka ndi kutembenuka mtima ndi kuchiritsidwa.”

11 Pamenepo ine ndinati, “Zimenezo ndi mpaka liti Inu Ambuye?”

Ndipo Iyeyo anandiyankha kuti,

“Mpaka mizinda itasanduka mabwinja
    nʼkusowa wokhalamo,
mpaka nyumba zitasowa anthu okhalamo,
    mpaka dziko litasanduka chipululu ndithu,
12 mpaka Yehova atasamutsira aliyense kutali,
    dziko nʼkusiyidwa kwathunthu.
13 Ndipo ngakhale chigawo chakhumi cha anthu chitatsala mʼdziko,
    nachonso chidzawonongedwa.
Koma monga momwe mitengo ya muwanga ndi thundu
    imasiyira chitsa pamene ayidula,
    chonchonso mbewu yoyera idzatsalira ngati chitsa chotsala mʼdziko.”

Yesaya Achenjeza Ahazi

Pamene Ahazi mwana wa Yotamu, mdzukulu wa Uziya anali mfumu ya Yuda, Rezini mfumu ya Siriya ndi Peka mwana wa Remaliya, mfumu ya Israeli anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu, koma sanathe kuwugonjetsa.

Tsono nyumba ya Davide inawuzidwa kuti, “Dziko la Siriya lagwirizana ndi Efereimu.” Choncho mfumu Ahazi ndi anthu ake ananjenjemera, monga momwe mitengo ya mʼnkhalango imagwedezekera ndi mphepo.

Pamenepo Yehova anawuza Yesaya kuti, “Tuluka, iwe ndi mwana wako Seariyasubu, mupite mukakumane ndi Ahazi kumapeto kwa ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu wopita ku Munda wa mmisiri wochapa nsalu. Ukamuwuze kuti, ‘Chenjera, khala phee ndipo usaope. Usataye mtima chifukwa cha zitsa ziwiri zomwe zikufuka, chifukwa cha ukali woopsa wa Rezini ndi Siriya, ndiponso wa Peka mwana wa Remaliya. Mfumu ya Siriya, Efereimu ndi mwana wa Remaliya apangana kuti akuchitire choyipa. Akunena kuti, ‘Tiyeni tikalimbane ndi Yuda. Tiyeni tiliwononge ndi kuligawa; tiligawane pakati pathu, ndipo tilonge ufumu mwana wa Tabeeli kumeneko.’ Komabe zimene akunena Ambuye Yehova ndi izi:

“ ‘Zimenezo sizidzatheka,
    sizidzachitika konse,
pakuti Siriya amadalira Damasiko,
    ndipo Damasiko amadalira mfumu Rezini basi.
Zisanathe zaka 65
    Efereimu adzawonongedwa kotheratu, sadzakhalanso mtundu wa anthu.
Dziko la Efereimu limadalira Samariya
    ndipo Samariya amadalira mwana wa Remaliya basi.
Mukapanda kulimbika pa chikhulupiriro chanu,
    ndithu simudzalimba konse.’ ”

10 Yehova anayankhulanso ndi Ahazi, 11 “Pempha chizindikiro kwa Yehova Mulungu wako, chikhale chozama ngati manda kapena chachitali ngati mlengalenga.”

12 Koma Ahazi anati, “Ine sindipempha; sindikufuna kuyesa Yehova.”

13 Apo Yesaya anati, “Imva tsopano, iwe nyumba ya Davide! Kodi sikokwanira kutopetsa anthu? Kodi mudzayeseranso kutopetsa Mulungu wanga? 14 Nʼchifukwa chake Ambuye mwini adzakupatsani chizindikiro: Onani, namwali adzakhala woyembekezera ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo mwanayo adzamutcha Imanueli. 15 Azidzadya chambiko ndi uchi, mpaka atadziwa kukana choyipa ndi kusankha chabwino. 16 Koma nthawi yokana choyipa ndi kusankha chabwino kwa mwanayo isanafike, mayiko a mafumu awiri amene amakuopsaniwo adzakhala atasanduka bwinja. 17 Yehova adzabweretsa pa inu, pa anthu anu ndiponso pa nyumba ya bambo wanu masiku a mavuto woti sanakhalepo kuyambira tsiku limene Efereimu anapatukana ndi Yuda. Yehova adzabweretsa mfumu ya ku Asiriya.”

18 Tsiku limenelo Yehova adzalizira likhweru ntchentche zochokera ku mitsinje yakutali ku Igupto, ndiponso njuchi zochokera ku dziko la Asiriya. 19 Onsewo adzafika ndi kudzakhazikika mu zigwa zozama, mʼmingʼalu ya matanthwe ndi mʼzitsamba zonse zaminga ndiponso ponse pamene pali malo omwetsera ziweto. 20 Tsiku limenelo Ambuye adzalemba ganyu ometa ochokera kutsidya kwa Mtsinje, ndiye mfumu ya ku Asiriya, kudzameta tsitsi lanu la ku mutu ndi la mʼmiyendo ndi ndevu zomwe. 21 Tsiku limenelo adzangosunga ngʼombe yayikazi yayingʼono ndi mbuzi ziwiri. 22 Ndipo chifukwa cha kuchuluka kwa mkaka umene ziwetozi zidzapereka, munthuyo azidzadya chambiko. Aliyense amene adzatsalire mʼdzikomo azidzadya chambiko ndi uchi. 23 Tsiku limenelo, paliponse pamene panali mitengo ya mpesa 1,000 ndipo mtengo wake ndi wokwana masekeli asiliva 1,000, padzamera mkandankhuku ndi minga. 24 Anthu adzapita kumeneko kukachita uzimba ali ndi uta ndi mivi, popeza kuti mʼdziko monsemo mudzakhala mkandankhuku ndi minga. 25 Ndipo mʼmapiri monse mʼmene kale munkalimidwa ndi khasu, simudzapitamo kuopa mkandankhuku ndi minga; malowo adzasanduka odyetserako ngʼombe ndi nkhosa.

Asiriya, Chida cha Yehova

Yehova anati kwa ine, “Tenga cholembapo chachikulu ndipo ulembepo malemba odziwika bwino: Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira. Ndipo ndidzayitana wansembe Uriya ndi Zekariya mwana wa Yeberekiya kuti akhale mboni zanga zodalirika.”

Ndipo ine ndinapita kwa mneneri wamkazi, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Ndipo Yehova anati kwa ine, “Umutche dzina lakuti, ‘Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.’ Mwanayo asanayambe kudziwa kuyitana kuti, ‘Ababa’ kapena ‘Amama’ chuma cha Damasiko ndi zofunkha za Samariya zidzatengedwa ndi mfumu ya ku Asiriya.”

Yehova anayankhulanso ndi Ine;

“Popeza anthu a dziko ili akana
    madzi anga oyenda mwachifatse a ku Siloamu,
ndipo akukondwerera Rezini
    ndi mwana wa Remaliya,
nʼchifukwa chake Ambuye ali pafupi kubweretsa
    madzi amkokomo a mtsinje wa Yufurate kudzalimbana nawo;
    mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo.
Madziwo adzasefukira mʼngalande zake zonse
    ndi mʼmagombe ake onse.
Ndipo adzalowa mwamphamvu mʼdziko la Yuda, adzasefukira,
    adzapitirira mpaka kumuyesa mʼkhosi.
Mapiko ake otambasuka adzaphimba dziko lako lonse,
    iwe Imanueli!”

Chitani phokoso lankhondo, inu mitundu ya anthu, ndipo munjenjemere!
    Tamverani, inu mayiko onse akutali.
Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere!
    Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere!
10 Konzani kachitidwe kanu kankhondo, koma simudzaphula kanthu,
    kambiranani zochita, koma zidzalephereka,
pakuti Mulungu ali nafe.

Yehova Achenjeza Mneneri

11 Yehova anandiyankhula ine mwamphamvu, ndipo anandichenjeza kuti ndisamayende mʼnjira za anthuwa. Iye anati:

12 “Usamanene kuti ndi chiwembu,
    chilichonse chimene anthuwa amati ndi chiwembu
usamaope zimene anthuwa amaziopa,
    ndipo usamachite nazo mantha.
13 Yehova Wamphamvuzonse ndiye amene uyenera kumuona kuti ndi woyera,
    ndiye amene uyenera kumuopa,
    ndiye amene uyenera kuchita naye mantha,
14 ndipo ndiye amene adzakhala malo opatulika;
    koma kwa anthu a ku Yuda ndi kwa anthu a ku Israeli adzakhala
mwala wopunthwitsa,
    mwala umene umapunthwitsa anthu,
thanthwe limene limagwetsa anthu.
    Ndipo kwa anthu a mu Yerusalemu adzakhala ngati msampha ndi khwekhwe.
15 Anthu ambiri adzapunthwapo
    adzagwa ndi kuthyokathyoka,
    adzakodwa ndi kugwidwa.”

16 Manga umboniwu
    ndipo umate malamulowa pamaso pa ophunzira anga.
17 Ndidzayembekezera Yehova,
    amene akubisira nkhope yake nyumba ya Yakobo.
Ine ndidzakhulupirira Iyeyo.

18 Onani, ine ndili pano pamodzi ndi ana amene Yehova wandipatsa, ndife zizindikiro ndi zodabwitsa kwa Aisraeli zochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, amene amakhala pa Phiri la Ziyoni.

19 Anthu akakuwuza kuti kafunsire kwa oyankhula ndi mizimu, amene amayankhula monongʼona ndi mongʼungʼudza, kodi anthu sayenera kukafunsira kwa Mulungu wawo? Chifukwa chiyani amafunsira kwa anthu akufa mʼmalo mwa kwa anthu amoyo, 20 kuti akalandireko mawu enieni ndi malangizo? Ngati anthuwo sayankhula monga mwa mawu awa, mwa iwo mulibe kuwala. 21 Anthu adzayendayenda mʼdziko movutika kwambiri ali ndi njala; pamene afowokeratu ndi njala, iwo adzakwiya kwambiri ndipo adzayangʼana kumwamba ndi kutemberera mfumu yawo ndi Mulungu wawo. 22 Ndipo akadzayangʼana pa dziko lapansi adzangoona mavuto okhaokha ndi mdima woopsa ndi wodetsa nkhawa, ndipo adzaponyedwa mu mdima wandiweyani.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.