Beginning
Za Chilango cha Turo
23 Uthenga wonena za Turo:
Lirani mofuwula, inu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi:
pakuti mzinda wa Turo wawonongedwa
ndipo mulibe nyumba kapena dooko.
Zimenezi anazimva
pochokera ku Kitimu.
2 Khalani chete inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja,
inu amalonda a ku Sidoni,
iwe amene unalemera ndi anthu oyenda pa nyanja.
3 Pa nyanja zazikulu
panabwera tirigu wa ku Sihori;
zokolola za ku Nailo, ndipo munachita malonda
ndi anthu a mitundu ina.
4 Chita manyazi, iwe Sidimu
pakuti nyanja yayankhula, linga la ku nyanja (Turo) layankhula kuti,
“Sindinamvepo zowawa za kubereka kapena kuberekapo mwana;
sindinalerepo ana aamuna kapena kulera ana aakazi.”
5 Mawuwa akadzamveka ku Igupto,
iwo adzachita mantha akadzamva kuti Turo wawonongeka.
6 Wolokerani ku Tarisisi,
lirani mofuwula, inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja.
7 Kodi uwu si mzinda wachisangalalo uja,
mzinda wakalekale,
umene anthu ake ankapita
kukakhala ku mayiko akutali?
8 Kodi ndani anakonza zimenezi kuti zigwere Turo, mzinda umene unakhazikitsa mizinda ina,
mzinda umene amalonda ake ndi akalonga
ndi otchuka
pa dziko lapansi?
9 Yehova Wamphamvuzonse anakonza zimenezi
kuti athetse kunyada kwawo
ndi kutsitsa anthu otchuka a pa dziko lapansi.
10 Mubalalike mʼdziko mwanu ngati mtsinje wa Nailo
inu anthu a ku Tarisisi,
pakuti mulibenso chokutetezani.
11 Yehova watambasula dzanja lake kuloza ku nyanja
ndipo wagwedeza maufumu ake.
Iye walamula kuti Kanaani
agwetse malinga ake.
12 Iye anati, “Simudzakondwanso konse,
inu anthu opanikizidwa a ku Sidoni, tsopano wamphwanyidwa!
“Ngakhale muwolokere ku Kitimu,
kumeneko simukapezako mpumulo.”
13 Onani dziko la Ababuloni,
anthu amenewa tsopano atheratu!
Asiriya asandutsa Turo kukhala
malo a zirombo za ku chipululu;
anamanga nsanja zawo za nkhondo,
anagumula malinga ake
ndipo anawasandutsa bwinja.
14 Lirani mofuwula, inu anthu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi;
chifukwa malinga ako agwetsedwa!
15 Pa nthawi imeneyo Turo adzayiwalika pa zaka 70, amene ndi masiku a moyo wa mfumu. Koma potsiriza pa zaka 70 zimenezi, Turo adzakhala ngati mkazi wachiwerewere woyimbidwa mu nyimbo:
16 “Tenga zeze wako uzungulire mzinda,
iwe mkazi wachiwerewere woyiwalika;
imba zeze mokometsera, imba nyimbo zambiri,
kuti anthu akukumbukire.”
17 Pakutha pa zaka 70, Yehova adzachitapo kanthu pa Turo. Iye adzabwerera ku ntchito yake yakale monga mkazi wachiwerewere ndipo adzachita zachiwerewere ndi maufumu onse a dziko lapansi. 18 Koma phindu lake ndi malipiro ake adzazipereka kwa Yehova; sadzazikundika kapena kuzisunga. Phindu lake lidzapita kwa mtumiki wa Yehova kuti agule zakudya zambiri ndi zovala zokongola.
Chilango cha Yehova pa Dziko Lapansi
24 Taonani, Yehova adzawononga dziko lapansi
ndi kulisandutsa chipululu;
Iye adzasakaza maonekedwe ake
ndi kumwaza anthu ake onse.
2 Aliyense zidzamuchitikira mofanana:
wansembe chimodzimodzi munthu wamba,
antchito aamuna mofanananso ndi ambuye awo aamuna,
antchito aakazi chimodzimodzi ambuye awo aakazi,
wogula chimodzimodzi wogulitsa,
wobwereka chimodzimodzi wobwereketsa,
okongola chimodzimodzi okongoza.
3 Dziko lapansi lidzawonongedwa kwathunthu
ndi kusakazikiratu.
Yehova wanena mawu awa.
4 Dziko lapansi likulira ndipo likufota,
dziko lonse likuvutika ndipo likuwuma,
anthu omveka a dziko lapansi akuvutika.
5 Anthu ayipitsa dziko lapansi;
posamvera malangizo ake;
pophwanya mawu ake
ndi pangano lake lamuyaya.
6 Nʼchifukwa chake matemberero akuwononga dziko lapansi;
anthu a mʼdzikomo akuzunzika chifukwa cha kulakwa kwawo,
iwo asakazika
ndipo atsala ochepa okha.
7 Vinyo watsopano watha ndipo mphesa zikufota;
onse okonda zosangalatsa ali ndi chisoni.
8 Kulira kokometsera kwa matambolini kwatha,
phokoso la anthu osangalala latha,
zeze wosangalatsa wati zii.
9 Anthu sadzayimbanso akumwa vinyo;
akadzamwa zaukali zidzakhala zowawa mʼkamwa mwawo.
10 Mzinda wachisokonezo uja wawonongeka;
nyumba iliyonse yatsekedwa.
11 Anthu akulira mʼmisewu kufuna vinyo;
chimwemwe chonse chatheratu,
palibenso chisangalalo pa dziko lapansi.
12 Mzinda wasanduka bwinja
zipata zake zagumuka.
13 Zimenezi ndizo zidzachitikire mitundu yonse ya dziko lapansi
ndiponso pakati pa mitundu ya anthu.
Zidzakhala ngati pamene mitengo ya olivi yayoyoledwa,
kapena ngati nthawi ya kunkha la mphesa atatsiriza kukolola.
14 Koma otsala onse akufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe;
anthu akumadzulo akutamanda ukulu wa Yehova.
15 Nʼchifukwa chake inu akummawa, tamandani Yehova;
ndi inu okhala mʼmphepete mwa nyanja kwezani dzina la Yehova, Mulungu wa Israeli.
16 Kuchokera kumalekezero a dziko lapansi tikumva kuyimba kotamanda
“Wolungamayo.”
Koma ine ndinati, “Ndatheratu, ndatheratu!
Tsoka kwa ine!
Anthu achinyengo akupitirizabe kuchita zachinyengo,
inde chinyengo chawo chikunkerankera mʼtsogolo.”
17 Inu anthu adziko lapansi, zoopsa, dzenje
ndi msampha zikukudikirani.
18 Aliyense wothawa phokoso la zoopsa
adzagwa mʼdzenje;
ndipo aliyense wotuluka mʼdzenjemo
adzakodwa ndi msampha.
Zitseko zakumwamba zatsekulidwa,
ndipo maziko a dziko lapansi agwedezeka.
19 Dziko lapansi lathyokathyoka,
ndipo lagawika pakati,
dziko lapansi lagwedezeka kotheratu.
20 Dziko lapansi likudzandira ngati munthu woledzera
likugwedezeka ndi mphepo ngati chisimba;
lalemedwa ndi machimo ake.
Lidzagwa ndipo silidzadzukanso.
21 Tsiku limenelo Yehova adzalanga
amphamvu a kumwamba
ndiponso mafumu apansi pano.
22 Mulungu adzawasonkhanitsa pamodzi
ngati amʼndende amene ali mʼdzenje.
Adzawatsekera mʼndende
ndipo adzalangidwa patapita nthawi yayitali.
23 Mwezi udzanyazitsidwa, dzuwa lidzachita manyazi;
pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzakhala mfumu ndipo adzalamulira;
pa Phiri la Ziyoni ndi ku Yerusalemu,
ndipo adzaonetsa ulemerero wake pamaso pa akuluakulu.
Nyimbo Yotamanda Yehova
25 Yehova ndinu Mulungu wanga;
ine ndidzakukwezani ndi kutamanda dzina lanu,
pakuti mwachita zodabwitsa
zimene munakonzekeratu kalekale
mokhulupirika kwambiri.
2 Inu mwasandutsa mzinda uja kukhala mulu wamiyala.
Ndipo mzinda wamalinga wasanduka bwinja,
linga la anthu achilendo lero si mzindanso
ndipo sidzamangidwanso.
3 Nʼchifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani;
mizinda ya mitundu ya anthu ankhanza idzakuopani.
4 Inu mwakhala ngati populumukira pa anthu osauka,
mwakhala ngati kobisalirako munthu wovutika pa nthawi ya masautso ake.
Mwakhala ngati pobisalirapo
pa nthawi ya mphepo yamkuntho ndi mthunzi pa nthawi ya dzuwa.
Pakuti anthu ankhanza
ali ngati mphepo yamkuntho yowomba pa khoma,
5 ndiponso ngati kutentha mʼdziko lowuma.
Inu mumaletsa phokoso la anthu achilendo.
Monga momwe mthunzi wa mtambo umachepetsa kutentha,
inu munaletsa nyimbo za anthu ankhanza.
6 Pa phiri ili Yehova Wamphamvuzonse adzakonzera
anthu a mitundu yonse madyerero a zakudya zokoma ndi vinyo wabwino.
Phwando la nyama yonona
ndi vinyo wabwino kwambiri.
7 Iye adzachotsa kulira
kumene kwaphimba anthu ngati nsalu.
Adzachotsa chinsalu chimene chakuta mitundu yonse ya anthu.
8 Yehova adzathetsa imfa mpaka muyaya,
Ambuye Yehova adzapukuta misozi mʼmaso
mwa munthu aliyense;
adzachotsa manyazi a anthu ake
pa dziko lonse lapansi,
Yehova wayankhula.
9 Tsiku limenelo iwo adzati,
“Ndithudi, uyu ndiye Mulungu wathu;
ife tinamudalira ndipo anatipulumutsa.
Uyu ndiye Yehova, ife tinamudalira;
tiyeni tikondwe ndi kusangalala chifukwa watipulumutsa.”
10 Yehova adzateteza phiri limeneli ndi dzanja lake;
ndipo Amowabu adzawapondereza pomwe alilipo,
ngati mmene amapondera manyowa mʼdzenje.
11 Amowabuwo adzatambasula manja awo mʼmenemo,
ngati mmene amachitira munthu wosambira.
Koma Mulungu adzathetsa kunyada kwawo
ngakhale luso la manja awo.
12 Iye adzagumula malinga awo ataliatali
ndipo adzawagwetsa
ndi kuwaponya pansi,
pa fumbi penipeni.
Nyimbo ya Matamando
26 Tsiku limenelo anthu a mʼdziko la Yuda adzayimba nyimbo iyi.
Tili ndi mzinda wolimba.
Mulungu amawuteteza ndi zipupa
ndi malinga.
2 Tsekulani zipata za mzinda
kuti mtundu wolungama
ndi wokhulupirika ulowemo.
3 Inu mudzamupatsa munthu
wa mtima wokhazikika
mtendere weniweni.
4 Mudalireni Yehova mpaka muyaya,
chifukwa Yehova Mulungu ndiye Thanthwe losatha.
5 Iye amatsitsa anthu amene amadziyika pamwamba,
iye amagwetsa pansi mzinda wodzitukumula,
amagumula makoma ake
ndi kuwagwetsa pansi pa fumbi penipeni.
6 Mapazi a anthu akuwupondereza,
mapazi a anthu oponderezedwa,
mapazi anthu osauka.
7 Njira ya munthu wolungama ndi yosalaza,
Inu Wolungamayo, mumasalaza njira ya wolungama.
8 Inde Yehova, timayenda mʼnjira zanu zolungama,
ife timayembekezera Inu;
mitima yathu imakhumba kukumbukira
ndi kulemekeza dzina lanu.
9 Moyo wanga umalakalaka Inu usiku wonse;
nthawi yammawa ndimafunafuna Inu.
Pamene muweruza dziko lapansi
anthu amaphunzira kuchita chilungamo.
10 Ngakhale mukomere mtima anthu oyipa,
saphunzira chilungamo.
Amachita zoyipa mʼdziko la chilungamo,
ndipo sazindikira ululu wa Yehova.
11 Inu Yehova, mwatukula dzanja lanu kuti muwalange,
koma iwo sakuliona dzanjalo.
Aloleni anthu aone ndi kuchita manyazi poona mmene mukondera anthu anu;
ndipo moto umene mwasonkhera adani anu uwapsereze.
12 Yehova, mumatipatsa mtendere;
ndipo zonse zimene ife tinazichita munatichitira ndinu.
13 Inu Yehova Mulungu wathu, ngakhale takhala tikulamulidwa ndi ena mʼmalo mwanu,
koma ife timalemekeza dzina lanu lokha.
14 Iwo tsopano sadzadzukanso;
mizimu yawo sidzabwera kudzativutitsa
pakuti mwawalanga ndipo mwawawononga;
palibenso amene amawakumbukira.
15 Inu Yehova, mwaukulitsa mtundu wathu;
mwauchulukitsa ndithu
ndipo mwalandirapo ulemu;
mwaukuza mbali zonse za dziko.
16 Yehova, anthu anu anabwera kwa Inu pamene anali mʼmasautso;
pamene munawalanga,
iwo anapemphera kwa Inu.
17 Monga mayi woyembekezera pamene nthawi yake yobereka yayandikira
amamva kupweteka ndipo amalira ndi ululu,
ifenso tinali chimodzimodzi pamaso panu, Inu Yehova.
18 Ife chimodzimodzi tinamva ululu, ngati mayi pa nthawi yobala mwana,
koma sitinapindulepo kanthu,
kapena kupulumutsa dziko lapansi;
sitinabadwitse anthu atsopano pa dziko pano.
19 Koma anthu anu amene anafa adzakhalanso ndi moyo;
matupi awo adzadzuka.
Iwo amene ali ku fumbi tsopano
adzadzuka ndi kuyimba mosangalala.
Monga mame amafewetsa pansi kutsitsimutsa zomera,
momwenso Yehova adzaukitsa anthu amene anafa kale.
20 Abale anga, pitani mukalowe mʼnyumba zanu
ndipo mukadzitsekere;
mukabisale kwa kanthawi kochepa
mpaka ukali wake utatha.
21 Taonani, Yehova akubwera kuchokera kumene amakhala;
akubwera kudzalanga anthu a dziko lapansi chifukwa cha machimo awo.
Dziko lapansi lidzawulula magazi amene anakhetsedwa pa dzikolo;
dziko lapansi silidzabisanso mitembo ya anthu ophedwa.
Za Munda Wamphesa wa Yehova
27 Tsiku limenelo,
Yehova ndi lupanga lake
lakuthwa, lalikulu ndi lamphamvu,
adzalanga Leviyatani chinjoka chothawa chija,
Leviyatani chinjoka chodzikulunga;
adzapha chirombo choopsa cha mʼnyanja.
2 Tsiku limenelo Yehova adzati,
“Tidzayimba nyimbo ya munda wamphesa wobereka bwino:
3 Ine, Yehova, ndimawuyangʼanira;
ndimawuthirira nthawi zonse.
Ndimawulondera usana ndi usiku
kuti wina angawononge.
4 Ine sindinakwiye.
Ngati mkandankhuku ndi minga zikanaoneka ndikanalimbana nazo!
Ndikachita nazo nkhondo;
ndikanazitentha zonse ndi moto.
5 Koma ngati apo ayi, abweretu kwa Ine adani angawo kuti ndidzawateteze;
apangane nane za mtendere,
ndithu, apangane nane za mtendere.”
6 Masiku akubwerawo Yakobo adzazika mizu,
Israeli adzaphukira ndi kuchita maluwa,
ndipo adzadzaza dziko lonse lapansi ndi zipatso.
7 Kodi Yehova anakantha Israeli
ngati momwe anakanthira anthu amene anazunza Israeli?
Kapena kodi Yehova anapha Israeli
ngati mmene anthu ena anaphera Israeli?
8 Yehova mwawalanga powapirikitsa ndi kuwatumiza ku ukapolo,
mwawachotsa ndi mpweya wanu woopsa,
monga zimachitikira pa tsiku la mkuntho wochokera kummawa.
9 Yehova adzakhululuka kulakwa kwa Yakobo.
Iwo adzaonetsa kuti alapadi pamene adzaphwanya miyala yonse ya guwa lachikunja,
ngati mmene anthu amaphwanyira miyala yanjereza
mpaka kukhala ngati fumbi lokhalokha.
Sipadzapezekanso mafano a Asera
kapena maguwa ofukiza lubani.
10 Mzinda wamalinga uja wasanduka bwinja,
wasanduka malo osiyidwa, ndi kutayidwa ngati chipululu;
kumeneko amadyetselako ana angʼombe
kumeneko zimapumulako ziweto
ndi kumwetula nthambi za mitengo kotheratu.
11 Pamene nthambi za mitengoyo zauma, zimathyoka
ndipo amayi amabwera nazitola ndi kuzisandutsa nkhuni.
Pakuti awa ndi anthu opanda nzeru;
kotero Mulungu amene anawapanga sadzachitira chisoni,
ndipo Mlengi wawo sawakomera mtima.
12 Tsiku limenelo Yehova adzasonkhanitsa pamodzi anthu ake mmodzimmodzi kumalo opunthira tirigu, kuchokera ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku mtsinje wa ku Igupto. 13 Ndipo tsiku limenelo lipenga lalikulu lidzalira. Amene akuzunzika ku Asiriya iwo amene ali ku ukapolo ku Igupto adzabwera ndi kudzalambira Yehova pa phiri lopatulika mu Yerusalemu.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.