Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Beginning

Read the Bible from start to finish, from Genesis to Revelation.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Maliro 3:37-5:22

37 Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika
    ngati Ambuye sanavomereze?
38 Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka
    mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
39 Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula
    akalangidwa chifukwa cha machimo ake?

40 Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu,
    ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
41 Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu
    kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
42 “Ife tachimwa ndi kuwukira
    ndipo inu simunakhululuke.

43 “Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo
    mwatitha mopanda chifundo.
44 Mwadzikuta mu mtambo
    kotero mapemphero athu sakukufikani.
45 Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala
    pakati pa mitundu ya anthu.

46 “Adani anthu atitsekulira pakamwa.
47 Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje,
    tapasuka ndi kuwonongedwa.”
48 Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe
    chifukwa anthu anga akuwonongedwa.

49 Misozi idzatsika kosalekeza,
    ndipo sidzasiya,
50 mpaka Yehova ayangʼane pansi
    kuchokera kumwamba ndi kuona.
51 Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi
    chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.

52 Akundisaka ngati mbalame,
    amene anali adani anga, popanda chifukwa.
53 Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje
    ndi kundiponya miyala;
54 madzi anamiza mutu wanga
    ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.

55 Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova,
    kuchokera mʼdzenje lozama.
56 Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere
    kulira kwanga kopempha thandizo.”
57 Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani,
    ndipo munati, “Usaope.”

58 Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga;
    munapulumutsa moyo wanga.
59 Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira.
    Mundiweruzire ndinu!
60 Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo,
    chiwembu chawo chonse pa ine.

61 Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo,
    chiwembu chawo chonse pa ine,
62 manongʼonongʼo a adani anga
    ondiwukira ine tsiku lonse.
63 Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira,
    akundinyoza mu nyimbo zawo.

64 Inu Yehova, muwabwezere chowayenera,
    chifukwa cha zimene manja awo achita.
65 Phimbani mitima yawo,
    ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
66 Muwalondole mwaukali ndipo
    muwawonongeretu pa dziko lapansi.

Haa! Golide wathimbirira,
    golide wosalala wasinthikiratu!
Amwazamwaza miyala yokongola ya kumalo opatulika
    pamphambano ponse pa mzinda.

Haa! Ana a Ziyoni amtengowapatali
    amene kale anali ngati golide,
tsopano ali ngati miphika ya dothi,
    ntchito ya owumba mbiya!

Ngakhale nkhandwe zimapereka bere
    kuyamwitsa ana ake,
koma anthu anga asanduka ankhanza
    ngati nthiwatiwa mʼchipululu.

Lilime la mwana lakangamira kukhosi
    chifukwa cha ludzu,
ana akupempha chakudya,
    koma palibe amene akuwapatsa.

Iwo amene kale ankadya zonona
    akupemphetsa mʼmisewu ya mu mzinda.
Iwo amene kale ankavala zokongola
    tsopano akugona pa phulusa.

Kuyipa kwa anthu anga kunali kwakukulu
    kuposa anthu a ku Sodomu,
amene anawonongedwa mʼkamphindi kochepa
    popanda owathandiza.

Akalonga ake anali owala koposa chisanu chowundana
    ndi oyera kuposa mkaka.
Matupi awo anali ofiira kuposa miyala ya rubi,
    maonekedwe awo ngati miyala ya safiro.

Koma tsopano maonekedwe awo ndi akuda kuposa mwaye;
    palibe angawazindikire mʼmisewu ya mu mzinda.
Khungu lawo lachita makwinyamakwinya pa mafupa awo;
    lawuma gwaa ngati nkhuni.

Amene anaphedwa ndi lupanga aliko bwino kuposa
    amene anafa ndi njala;
chifukwa chosowa chakudya cha mʼmunda
    iwowa ankafowoka ndi njala mpaka kufa.

10 Amayi achifundo afika
    pophika ana awo enieni,
ndiwo anali chakudya chawo pamene anthu
    anga anali kuwonongeka.

11 Yehova wakwaniritsa ukali wake;
    wagwetsa pansi mkwiyo wake woopsa.
Ndipo wayatsa moto mʼZiyoni
    kuti uwononge maziko ake.

12 Mafumu a pa dziko lapansi sanakhulupirire,
    kapena wina aliyense wokhala pa dziko lonse,
kuti adani kapena ankhondo akhoza kulowa
    pa zipata za Yerusalemu.

13 Koma izi zinachitika chifukwa cha kuchimwa kwa aneneri ake
    ndi mphulupulu za ansembe ake,
amene ankapha anthu osalakwa pakati pawo.

14 Tsopano akungoyendayenda mʼmisewu ya mu mzinda
    ngati anthu osaona.
Iwo ndi odetsedwa kwambiri ndi magazi
    palibe yemwe angayerekeze nʼkukhudza komwe chovala chawo.

15 Anthu akuwafuwulira kuti, “Chokani! Inu anthu odetsedwa!”
    “Chokani! Chokani! Musatikhudze ife!”
Akamathawa ndi kumangoyendayenda,
    pakati pa anthu a mitundu yonse amati,
    “Asakhalenso ndi ife.”

16 Yehova mwini wake wawabalalitsa;
    Iye sakuwalabadiranso.
Ansembe sakulandira ulemu,
    akuluakulu sakuwachitira chifundo.

17 Ndiponso maso athu atopa nʼkuyangʼana,
    chithandizo chosabwera nʼkomwe,
kuchokera pa nsanja zathu tinadikirira mtundu
    wa anthu umene sukanatipulumutsa.

18 Anthu ankalondola mapazi athu,
    choncho sitikanayenda mʼmisewu yathu mu mzinda.
Chimaliziro chathu chinali pafupi, masiku athu anali owerengeka,
    chifukwa chimaliziro chathu chinali chitafika.

19 Otilondola akuthamanga kwambiri
    kuposa ziwombankhanga mu mlengalenga;
anatithamangitsa mpaka ku mapiri
    ndi kutibisalira mʼchipululu.

20 Wodzozedwa wa Yehova, mpweya wathu wotipatsa moyo,
    anakodwa mʼmisampha yawo.
Tinaganiza kuti tidzakhala pansi pa mthunzi wake
    pakati pa mitundu ya anthu.

21 Kondwera ndi kusangalala, mwana wamkazi wa Edomu.
    Iwe amene umakhala mʼdziko la Uzi.
Koma iwenso chikho chidzakupeza;
    udzaledzera mpaka kukhala maliseche.

22 Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, chilango chako chidzatha;
    Iye sadzatalikitsa nthawi yako ya ukapolo.
Koma Yehova adzalanga machimo ako, iwe mwana wamkazi wa Edomu,
    ndi kuyika poyera mphulupulu zako.

Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira;
    yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
Apereka cholowa chathu kwa obwera,
    nyumba zathu kwa alendo.
Takhala amasiye ndi wopanda abambo,
    amayi athu ali ngati akazi amasiye.
Tiyenera kugula madzi amene timamwa,
    nkhuni zathunso nʼzogula.
Otilondola atigwira pakhosi;
    tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya
    kuti tipeze chakudya.
Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale,
    koma chilango chawo chili pa ife.
Akapolo akutilamulira,
    ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe
    chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
10 Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo,
    chifukwa cha kuwawa kwa njala.
11 Amayi agwiriridwa mu Ziyoni,
    ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
12 Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo,
    akuluakulu sakuwalemekeza.
13 Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu;
    anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
14 Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda;
    achinyamata aleka nyimbo zawo.
15 Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu;
    kuvina kwathu kwasanduka maliro.
16 Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu.
    Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
17 Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi,
    chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
18 pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja,
    nkhandwe zikungoyendayendapo.

19 Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya;
    mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
20 Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse?
    Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
21 Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere;
    mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
22 pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu,
    ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.