Beginning
Tchimo, Kuvomereza ndi Chipulumutso
59 Taonani, mkono wa Yehova si waufupi kuti sungathe kupulumutsa,
kapena khutu lake kuti ndilogontha kuti sangamve.
2 Koma zoyipa zanu zakulekanitsani
ndi Mulungu wanu;
ndipo wakufulatirani chifukwa cha machimo anu,
kotero Iye sadzamva.
3 Pakuti manja anu ali psuu ndi magazi.
Munayipitsa zala zanu ndi zamphulupulu.
Pakamwa panu payankhula zabodza,
ndipo lilime lanu lanena zinthu zoyipa.
4 Palibe amene akuyimba mnzake mlandu molungama,
palibe amene akupita ku mlandu moona mtima.
Iwo amadalira mawu opanda pake ndipo amayankhula mabodza;
amalingalira za mphulupulu ndipo amachita zoyipa.
5 Iwo amayikira mazira a mamba
ndipo amaluka ukonde wakangawude.
Aliyense amene adzadya mazira awo adzafa,
ndipo ngati dzira limodzi lasweka limatulutsa mphiri.
6 Ukonde wawo wa kangawude sangawuvale ngati chovala;
ndipo chimene apangacho sangachifunde.
Ntchito zawo ndi zoyipa,
ndipo amakonda kuchita zandewu ndi manja awo.
7 Amathamangira kukachita zoyipa;
sachedwa kupha anthu osalakwa.
Maganizo awo ndi maganizo oyipa;
kulikonse kumene amapita amasiyako bwinja ndi chiwonongeko.
8 Iwo sadziwa kuchita za mtendere;
zonse zimene amachita nʼzopanda chilungamo.
Njira zawo zonse nʼzokhotakhota;
aliyense oyenda mʼnjira zimenezo sadzapeza mtendere.
9 Anthu akuti, “Chifukwa cha zimenezi chilungamo chatitalikira;
ndipo chipulumutso sichitifikira.
Timafunafuna kuwala koma timangopeza mdima okhaokha;
tinayembekezera kuyera koma timayenda mu mdima wandiweyani.
10 Timapapasapapasa khoma ngati munthu wosaona,
kuyangʼanayangʼana njira ngati anthu opanda maso.
Timapunthwa dzuwa lili paliwombo ngati kuti ndi usiku;
timakhala pansi mu mdima ngati anthu akufa.
11 Tonse timabangula ngati zimbalangondo:
Timalira modandaula ngati nkhunda.
Tinayembekezera kuweruza kolungama; koma sitikupeza.
Timayembekezera chipulumutso koma chimakhala nafe kutali.”
12 Pakuti zolakwa zathu nʼzochuluka pamaso panu,
ndipo machimo athu akutsutsana nafe.
Zolakwa zathu zili ndi ife nthawi zonse
ndipo tikuvomereza machimo athu:
13 Tawukira ndi kumukana Yehova.
Tafulatira Mulungu wathu,
pa kupondereza anzathu ndi kupandukira Yehova,
ndi pa kuyankhula mabodza amene tawaganiza mʼmitima mwathu.
14 Motero kuweruza kolungama kwalekeka
ndipo choonadi chili kutali ndi ife;
kukhulupirika sikukupezekanso mʼmabwalo a milandu,
ndipo kuona mtima sikukupezekanso mʼmenemo.
15 Choonadi sichikupezeka kumeneko,
ndipo wina akakana kuchita nawo zoyipa amapeza mavuto.
Yehova anaziona zimenezi ndipo zinamunyansa
kuti panalibe chiweruzo cholungama.
16 Yehova anaona kuti panalibe ndi mmodzi yemwe,
Iye anadabwa kuti panalibe ndi mmodzi yemwe woti nʼkupembedzera;
Choncho mphamvu zake zomwe zinamuthandiza,
ndipo anadzilimbitsa ndi kulungama kwake;
17 Iye anavala chilungamo ngati chovala chachitsulo chapachifuwa,
ndipo kumutu kwake amavala chipewa chachipulumutso;
anavala kulipsira ngati chovala
ndipo anadzikuta ndi mkwiyo ngati chofunda.
18 Iye adzawabwezera chilango adani a anthu ake
molingana ndi zimene anachita,
adzaonetsa ukali kwa adani ake
ndi kubwezera chilango odana naye.
Adzalanga ngakhale okhala mayiko akutali.
19 Choncho akadzabwera ngati madzi
oyendetsedwa ndi mphepo yamphamvu yamkuntho.
Anthu onse kuyambira kumadzulo mpaka kummawa
adzaopa dzina la Yehova ndi ulemerero wake.
20 “Mpulumutsi adzabwera ku Ziyoni
kudzapulumutsa anthu a fuko la Yakobo amene analapa machimo awo,”
akutero Yehova.
21 Yehova akuti, “Kunena za pangano lake ndi iwo, Mzimu wanga umene uli pa inu, ndiponso mawu anga amene ndayika mʼkamwa mwanu sadzachoka mʼkamwa mwanu, kapena kuchoka mʼkamwa mwa ana anu, kapena mʼkamwa mwa zidzukulu zawo kuyambira tsopano mpaka kalekale,”
akutero Yehova.
Ulemerero wa Ziyoni
60 “Dzuka, wala, pakuti kuwala kwako kwafika,
ndipo ulemerero wa Yehova wakuwalira.
2 Taona, mdima waphimba dziko lapansi
ndipo mdima wandiweyani wagwa pa anthu a mitundu ina,
koma Yehova adzakuwalira iwe,
ndipo ulemerero wake udzaoneka pa iwe.
3 Mitundu ya anthu idzatsata kuwunika kwako
ndipo mafumu adzalondola kunyezimira kwa mʼbandakucha wako.
4 “Tukula maso ako, yangʼanayangʼana ndipo ona zimene zikuchitika.
Onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe;
ana ako a amuna akubwera kuchokera kutali
ndipo ana ako aakazi anyamulidwa mʼmanja.
5 Ukadzaona zimenezi udzasangalala kwambiri,
mtima wako udzalumpha ndi kudzaza ndi chimwemwe;
chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe
chuma cha mitundu ya anthu chidzabwera kwa iwe.
6 Gulu la ngamira lidzaphimba dziko lako,
ngamira zingʼonozingʼono zidzachokera ku Midiyani ndi ku Efai.
Ndipo onse a ku Seba adzabwera
atanyamula golide ndi lubani
uku akutamanda Yehova.
7 Ziweto zonse za ku Kedara adzazisonkhanitsa kwa inu,
nkhosa zazimuna za ku Nabayoti zidzakutumikirani;
zidzalandiridwa monga chopereka pa guwa langa la nsembe,
ndipo ndidzakongoletsa Nyumba yanga.
8 “Kodi ndi zayani izo zikuwuluka ngati mitambo,
ngati kapena nkhunda zobwerera ku zisa zawo?
9 Ndithu, izi ndi sitima za pa madzi zochokera ku mayiko akutali;
patsogolo pali sitima zapamadzi za ku Tarisisi,
zikubweretsa ana ako ochokera kutali,
pamodzi ndi siliva wawo ndi golide wawo,
kudzalemekeza Yehova Mulungu wako,
Woyerayo wa Israeli,
pakuti Iye wakuvekani inu ulemerero.
10 “Alendo adzamanganso malinga ako,
ndipo mafumu awo adzakutumikira.
Ngakhale ndinakukantha ndili wokwiya,
koma tsopano ndidzakukomera mtima ndikukuchitira chifundo.
11 Zipata zako zidzakhala zotsekula nthawi zonse,
sadzazitseka nthawi zonse, usana ndi usiku,
kotero anthu adzabwera kwa iwe ndi chuma chawo,
akuyenda pa mdipiti mafumu awo ali patsogolo.
12 Pakuti mtundu wa anthu ndi mafumu amene sakutumikira iwe;
adzawonongeka kotheratu.
13 “Adzabwera nayo kwa iwe mitengo ya payini,
mkuyu ndi naphini imene ili mʼnkhalango ya Lebanoni
kuti adzakongoletsere malo a nyumba yanga yopatulika;
ndipo ndidzalemekeza malo amene Ine ndimapondapo.
14 Ana aja amene anakuzunzani adzabwera ndipo adzakugwadirani;
onse amene anakunyozani adzagwada pansi pa mapazi anu.
Ndipo adzakutchani kuti Mzinda wa Yehova;
Ziyoni mzinda wa Woyerayo wa Israeli.
15 “Ngakhale anthu anakusiya nadana nawe,
koma Ine ndidzakukuza mpaka muyaya,
ndipo udzakhala malo a chimwemwe
cha anthu amibado yonse.
16 Udzamwa mkaka wa mitundu ya anthu
ndi kuleredwa pa maere aufumu,
motero udzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wako,
Momboli wako ndiye Wamphamvu wa Yakobo.
17 Ndidzakupatsa golide mʼmalo mwa mkuwa,
ndi siliva mʼmalo mwa chitsulo.
Ndidzakupatsa mkuwa mʼmalo mwa thabwa
ndi chitsulo mʼmalo mwa miyala.
Olamulira ako adzakhala a mtendere.
Ndidzasandutsa okulamulira kuti akhale achilungamo.
18 Ziwawa sizidzamvekanso mʼdziko lako,
bwinja kapena chiwonongeko sizidzapezeka mʼdziko lako,
ndidzakhala malinga ako okuteteza
ndipo udzanditamanda.
19 Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire,
kapena mwezi kuti uwunikire usiku,
pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya,
ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.
20 Dzuwa lako silidzalowanso,
ndipo mwezi wako sudzazimiriranso;
Yehova adzakhala kuwunika kwako kwamuyaya,
ndipo masiku a mavuto ako adzatha.
21 Ndipo anthu ako onse adzakhala olungama
ndipo dzikolo lidzakhala lawo mpaka muyaya.
Iwo ndi mphukira imene Ine ndayidzala,
ntchito ya manja anga,
kuti aonetse ulemerero wanga.
22 Kabanja kakangʼono kadzasanduka fuko,
kafuko kakangʼono kudzasanduka mtundu wamphamvu.
Ine ndine Yehova,
nthawi yake ikafika ndidzazichita zimenezi mofulumira.”
Uthenga Wabwino wa Yehova
61 Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine,
chifukwa Yehova wandidzoza
kuti ndilalikire uthenga wabwino kwa anthu osauka.
Wandituma kuti ndikatonthoze anthu osweka mtima,
ndikalengeze kwa akapolo kuti alandire ufulu
ndiponso kuti ndikamasule a mʼndende.
2 Wandituma kuti ndikalengeze nthawi imene Yehova adzapulumutsa anthu ake;
za tsiku limene Yehova adzalanga adani a anthu ake.
Wandituma kuti ndikatonthoze olira.
3 Wandituma kuti ndiwakonzere olira a ku Ziyoni,
nkhata ya maluwa yokongola
mʼmalo mwa phulusa,
ndiwapatse mafuta achikondwerero
mʼmalo mwa kulira.
Ndiwapatse chovala cha matamando
mʼmalo mwa mtima wopsinjika.
Ndipo iwo adzatchedwa mitengo ya thundu yamphamvu yachilungamo,
yoyidzala Yehova
kuti Iye mwini apezemo ulemerero wake.
4 Adzamanganso mabwinja akale a mzinda
ndipo malo amene anawonongeka kalekale aja adzakonzanso.
Adzakonzanso mizinda imene inapasuka,
imene yakhala yowonongeka kwa nthawi yayitali kwambiri.
5 Anthu achilendo adzakutumikirani; adzazidyetsa ziweto zanu;
iwo adzagwira ntchito mʼminda yanu ya mpesa.
6 Ndipo inu mudzatchedwa ansembe a Yehova,
adzakutchulani kuti ndinu atumiki a Mulungu wathu.
Mudzadyerera chuma cha mitundu ya anthu,
ndipo mudzanyadira ulemu umene mwalandira.
7 Chifukwa manyazi awo anali owirikiza;
ndi kuti munalandira
chitonzo ndi kutukwana,
adzakondwera ndi cholowa chawo,
tsono adzalandira cholowa chawo cha chigawo cha dziko mowirikiza,
ndipo chimwemwe chamuyaya chidzakhala chawo.
8 “Pakuti Ine Yehova, ndimakonda chilungamo;
ndimadana ndi zakuba ndi zoyipa.
Anthu anga ndidzawapatsa mphotho mokhulupirika
ndikupangana nawo pangano losatha.
9 Ana awo adzakhala odziwika pakati pa mitundu ya anthu
ndipo adzukulu awo adzakhala otchuka pakati pa anthu a mitundu ina.
Aliyense wowaona adzazindikira
kuti ndi anthu amene Yehova wawadalitsa.”
10 Ine ndikusangalala kwambiri chifukwa cha Yehova;
moyo wanga ukukondwera chifukwa cha Mulungu wanga.
Pakuti Iye wandiveka zovala zachipulumutso,
ndipo wandiveka mkanjo wachilungamo.
Zili ngati mkwati wovala nkhata ya maluwa mʼkhosi mwake,
ndiponso ngati mkwatibwi wovala mikanda yamtengowapatali.
11 Monga momwe nthaka imameretsa mbewu
ndiponso monga munda umakulitsa mbewu zimene anadzala,
momwemonso Ambuye Yehova adzaonetsa chilungamo ndi matamando
pamaso pa mitundu yonse ya anthu.
Dzina Latsopano la Ziyoni
62 Chifukwa chokonda Ziyoni sindidzakhala chete,
chifukwa chokonda Yerusalemu sindidzakhala chete,
mpaka chilungamo chake chitaoneka poyera ngati kuwala,
ndi chipulumutso chake chitaoneka ngati sakali yoyaka.
2 Mitundu ya anthu idzaona iwe utapambana pa nkhondo
ndipo mafumu onse adzaona ulemerero wako.
Adzakuyitanira dzina latsopano
limene adzakupatse ndi Yehova.
3 Udzakhala ngati chipewa chaulemerero mʼdzanja la Yehova,
ndi ngati nduwira yaufumu mʼdzanja la Mulungu wako.
4 Sadzakutchanso “Wosiyidwa,”
ndipo dziko lako silidzatchedwanso “Chipululu.”
Koma dzina lako latsopano lidzakhala “Ndakondwera naye.”
Ndipo dziko lako lidzatchedwa “Wokwatiwa.”
Chifukwa Yehova akukondwera nawe,
ndipo adzakhala ngati mwamuna wa dziko lako.
5 Monga mnyamata amakwatira namwali,
momwenso mmisiri wodzakumanga adzakukwatira;
monga mkwati amakondwera ndi mkwatibwi,
chonchonso Mulungu adzakondwera nawe.
6 Iwe Yerusalemu, pa malinga ako ndayikapo alonda;
sadzakhala chete usana kapena usiku.
Inu amene mumakumbutsa Yehova za malonjezo ake
musapumule.
7 Musamupatse mpata wopuma mpaka atakhazikitsa Yerusalemu
kukhala mzinda umene dziko lapansi lidzawutamande.
8 Yehova analumbira atakweza dzanja lake.
Anati,
“Sindidzaperekanso tirigu wako
kuti akhale chakudya cha adani ako,
ndipo alendo sadzamwanso vinyo wako watsopano
pakuti unamuvutikira.
9 Koma amene amakakolola ndiwo amene adzadye buledi
ndi kutamanda Yehova,
ndipo amene amasonkhanitsa pamodzi mphesa ndiwo amene adzamwe vinyo
mʼmabwalo a Nyumba yanga.”
10 Tulukani, dutsani pa zipata!
Konzerani anthu njira.
Lambulani, lambulani msewu waukulu!
Chotsani miyala.
Kwezani mbendera kuti mitundu ya anthu izione.
11 Yehova walengeza
ku dziko lonse lapansi kuti,
Awuzeni anthu a ku Yerusalemu kuti,
“Taonani, chipulumutso chanu chikubwera;
Yehova akubwera ndi mphotho yake
akubwera nazo zokuyenerani.”
12 Iwo adzatchedwa Anthu Opatulika,
owomboledwa a Yehova;
ndipo adzakutchani “Okondwa a Yehova”
“Mzinda umene Yehova sanawusiye.”
Yehova Agonjetsa Anthu a Mitundu Ina
63 Kodi ndani uyo akubwera kuchokera ku Edomu,
atavala zovala za ku Bozira za madontho ofiira?
Kodi uyu ndani, amene wavala zovala zokongola,
akuyenda mwa mphamvu zake?
“Ndi Ineyo, woyankhula zachilungamo
ndiponso wamphamvu zopulumutsa.”
2 Nanga bwanji zovala zanu zili psuu,
ngati za munthu wofinya mphesa?
3 “Ndapondereza ndekha anthu a mitundu ina ngati mphesa,
palibe ndi mmodzi yemwe anali nane.
Ndinawapondereza ndili wokwiya
ndipo ndinawapondereza ndili ndi ukali;
magazi awo anadothera pa zovala zanga,
ndipo zovala zanga zonse zinathimbirira.
4 Pakuti ndinatsimikiza mu mtima mwanga kuti lafika tsiku lolipsira anthu anga;
ndipo chaka cha kuwomboledwa kwanga chafika.
5 Ndinayangʼana ndipo panalibe munthu wondithandiza.
Ndinadabwa kwambiri kuti panalibe wondichirikiza;
choncho ndinapambana ndi mphamvu zanga,
ndipo mkwiyo wanga unandilimbitsa.
6 Ndinapondereza mitundu ya anthu ndili wokwiya;
ndipo ndinawasakaza
ndipo ndinathira magazi awo pansi.”
Matamando ndi Pemphero
7 Ndidzafotokoza za kukoma mtima kwa Yehova,
ntchito zimene Iye ayenera kutamandidwa.
Ndidzatamanda Yehova chifukwa cha zonse zimene watichitira.
Inde, mwa chifundo ndi kukoma mtima kwake
Yehova wachitira nyumba ya Israeli
zinthu zabwino zambiri.
8 Yehova anati, “Ndithu awa ndi anthu anga,
ana anga amene sadzandinyenga Ine.”
Choncho anawapulumutsa.
9 Iyenso anasautsidwa mʼmasautso awo onse,
ndipo mngelo wochokera kwa Iye anawapulumutsa.
Mwa chikondi ndi chifundo chake iye anawapulumutsa,
anawanyamula ndikuwatenga
kuyambira kale lomwe.
10 Komabe iwo anawukira
ndi kumvetsa chisoni Mzimu Woyera.
Motero Yehova anatembenuka nakhala mdani wawo
ndipo Iye mwini anamenyana nawo.
11 Pamenepo anthu ake anakumbukira masiku amakedzana,
masiku a Mose mtumiki wake;
ndipo anafunsa kuti, “Ali kuti Yehova amene anawawolotsa pa nyanja,
pamodzi ndi Mose mʼbusa wawo?
Ali kuti Iye amene anayika
Mzimu Woyera pakati pawo?
12 Ali kuti amene anachita zinthu zodabwitsa
ndi mphamvu zake zazikulu kudzera mwa Mose?
Ali kuti amene anagawa madzi pa nyanja anthu ake akuona,
kuti dzina lake limveke mpaka muyaya,
13 amene anawayendetsa pa nyanja yozama?
Monga kavalo woyendayenda mʼchipululu,
iwo sanapunthwe;
14 Mzimu Woyera unawapumulitsa
ngati mmene ngʼombe zimapumulira.
Umu ndi mmene Inu munatsogolera anthu anu
kuti dzina lanu lilemekezeke.”
15 Inu Yehova amene muli kumwambako, pa mpando wanu wolemekezeka,
wopatulika ndi waulemerero, tiyangʼaneni ife.
Kodi changu chanu ndi mphamvu zanu zili kuti?
Simukutionetsanso kukoma mtima kwanu ndi chifundo chanu.
16 Koma Inu ndinu Atate athu,
ngakhale Abrahamu satidziwa
kapena Israeli kutivomereza ife;
Inu Yehova, ndinu Atate athu,
kuyambira kale dzina lanu ndinu Mpulumutsi wathu.
17 Chifukwa chiyani, Inu Yehova, mukutisocheretsa pa njira zanu?
Bwanji mukutilola kuti tikhale owuma mitima kotero kuti sitikukuopaninso?
Bwererani chifukwa cha atumiki anu;
mafuko a anthu amene ali cholowa chanu.
18 Anthu anu atangokhala pa malo anu opatulika pa kanthawi kochepa,
adani athu anasakaza malo anu opatulika.
19 Ife tili ngati anthu amene
simunawalamulirepo
ngati iwo amene sanakhalepo anthu anu.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.