Beginning
22 Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri;
kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.
2 Wolemera ndi wosauka ndi ofanana;
onsewa anawalenga ndi Yehova.
3 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala,
koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.
4 Mphotho ya munthu wodzichepetsa
ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.
5 Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha,
koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.
6 Mwana muzimuphunzitsa njira yake,
ndipo akadzakalamba sadzachokamo.
7 Wolemera amalamulira wosauka,
ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.
8 Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto,
ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.
9 Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika,
pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.
10 Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha;
mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.
11 Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino,
adzakhala bwenzi la mfumu.
12 Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu,
koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.
13 Munthu waulesi amati,
“Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”
14 Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama;
amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.
15 Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana,
koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.
16 Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake,
ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.
Malangizo a Anthu Anzeru
17 Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru;
uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.
18 Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako
ndi wokonzeka kuziyankhula.
19 Ndakuphunzitsa zimenezi lero
koma makamaka uziopa Yehova.
20 Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu
okuchenjeza ndi okupatsa nzeru,
21 malangizo okudziwitsa zolungama
ndi zoona
ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?
22 Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka,
ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,
23 pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo
ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.
24 Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima
ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya
25 kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake
ndi kukodwa mu msampha.
26 Usakhale munthu wopereka chikole
kapena kukhala mboni pa ngongole;
27 ngati ulephera kupeza njira yolipirira
adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.
28 Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale
amene anayikidwa ndi makolo ako.
29 Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake?
Iye adzatumikira mafumu;
sadzatumikira anthu wamba.
23 Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira,
uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
2 ngati ndiwe munthu wadyera
udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
3 Usasirire zakudya zake,
pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
4 Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma,
ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
5 Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo.
Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi
ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
6 Usadye chakudya cha munthu waumbombo,
usalakalake zakudya zake zokoma;
7 paja iye ndi munthu amene
nthawi zonse amaganizira za mtengo wake
ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,”
koma sakondweretsedwa nawe.
8 Udzasanza zimene wadyazo
ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
9 Usayankhule munthu wopusa akumva,
pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
10 Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale
kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
11 paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu;
iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
12 Mtima wako uzikhala pa malangizo
ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
13 Usaleke kumulangiza mwana;
ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
14 Ukamukwapula ndi tsatsa
udzapulumutsa moyo wake.
15 Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru,
inenso mtima wanga udzakondwera.
16 Mtima wanga udzakondwera
pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
17 Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa,
koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
18 Ndithu za mʼtsogolo zilipo
ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
19 Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru,
mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
20 Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera
kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
21 Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi
ndipo aulesi adzavala sanza.
22 Mvera abambo ako amene anakubala,
usanyoze amayi ako pamene akalamba.
23 Gula choonadi ndipo usachigulitse;
ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
24 Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu;
Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
25 Abambo ndi amayi ako asangalale;
amene anakubereka akondwere!
26 Mwana wanga, undikhulupirire
ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
27 Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama;
ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
28 Amabisala ngati mbala yachifwamba,
ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
29 Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni?
Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo?
Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
30 Ndi amene amakhalitsa pa mowa,
amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
31 Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo,
pamene akuwira mʼchikho
pamene akumweka bwino!
32 Potsiriza pake amaluma ngati njoka,
ndipo amajompha ngati mphiri.
33 Maso ako adzaona zinthu zachilendo
ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
34 Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja,
kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
35 Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe!
Andimenya koma sindinamve kanthu!
Kodi ndidzuka nthawi yanji?
Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.