Beginning
Alefu
119 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa,
amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake,
amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
3 Sachita cholakwa chilichonse;
amayenda mʼnjira zake.
4 Inu mwapereka malangizo
ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika
pa kumvera zophunzitsa zanu!
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi,
poganizira malamulo anu onse.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama,
pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu;
musanditaye kwathunthu.
Beti
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake?
Akawasamala potsata mawu anu.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse;
musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga
kuti ndisakuchimwireni.
12 Mutamandike Inu Yehova;
phunzitseni malamulo anu.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse
amene amachokera pakamwa panu.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu
monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
15 Ndimalingalira malangizo anu
ndipo ndimaganizira njira zanu.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu;
sindidzayiwala konse mawu anu.
Gimeli
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo;
kuti tsono ndisunge mawu anu.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona
zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi;
musandibisire malamulo anu.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka
malamulo anu nthawi zonse.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa,
amene achoka pa malamulo anu.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo
pakuti ndimasunga malamulo anu.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza,
mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24 Malamulo anu amandikondweretsa;
ndiwo amene amandilangiza.
Daleti
25 Moyo wanga wakangamira fumbi;
tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha;
phunzitseni malamulo anu.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu;
pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni;
limbikitseni monga mwa mawu anu.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo;
mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30 Ndasankha njira ya choonadi;
ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova;
musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu,
pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
He
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu;
ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu
ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu,
pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu,
osati chuma.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe;
sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu,
kuti Inu muopedwe.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa,
pakuti malamulo anu ndi abwino.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu!
Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Wawi
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova,
chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza,
popeza ndimadalira mawu anu.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga,
pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse,
ku nthawi za nthawi.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu,
chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu
ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu
chifukwa ndimawakonda.
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda,
ndipo ndimalingalira malangizo anu.
Zayini
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu,
popeza mwandipatsa chiyembekezo.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi:
lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa,
koma sindichoka pa malamulo anu.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale,
ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa
amene ataya malamulo anu.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga
kulikonse kumene ndigonako.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova,
ndipo ndidzasunga malamulo anu.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita:
ndimasunga malangizo anu.
Heti
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa;
ndalonjeza kumvera mawu anu.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse;
mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59 Ndinalingalira za njira zanga
ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza
kumvera malamulo anu.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe,
sindidzayiwala lamulo lanu.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu
chifukwa cha malamulo anu olungama.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani,
kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika,
phunzitseni malamulo anu.
Teti
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu
molingana ndi mawu anu.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino,
pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera,
koma tsopano ndimamvera mawu anu.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino;
phunzitseni malamulo anu.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza,
ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa,
koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa
kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri
kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
Yodi
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba;
patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona,
chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama
ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa,
molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo,
popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa;
koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine,
iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu
kuti ndisachititsidwe manyazi.
Kafu
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu,
koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu;
Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi
sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti?
Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85 Anthu osalabadira za Mulungu,
odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika;
thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi
koma sindinataye malangizo anu.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika,
ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.