Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Beginning

Read the Bible from start to finish, from Genesis to Revelation.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Miyambo 16-18

16 Zolinga za mu mtima ndi za munthu,
    koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.

Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake,
    koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.

Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova,
    ndipo zolinga zako zidzachitikadi.

Yehova amachita zonse ndi cholinga chake,
    ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.

Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova.
    Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.

Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake;
    chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.

Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova,
    ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.

Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo,
    kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.

Mtima wa munthu umalingalira zochita,
    koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.

10 Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu;
    ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.

11 Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova;
    miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.

12 Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu,
    pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.

13 Mawu owona amakondweretsa mfumu.
    Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.

14 Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa,
    koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.

15 Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo;
    ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.

16 Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide.
    Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.

17 Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa;
    wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.

18 Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko,
    ndipo munthu wodzikuza adzagwa.

19 Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa,
    kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.

20 Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino,
    ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.

21 A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu,
    ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.

22 Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako,
    koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.

23 Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru,
    ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.

24 Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi,
    amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.

25 Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu
    koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.

26 Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira;
    njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.

27 Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa
    ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.

28 Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano,
    ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.

29 Munthu wandewu amakopa mnansi wake,
    ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.

30 Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota;
    amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.

31 Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero;
    munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.

32 Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo,
    munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.

33 Maere amaponyedwa pa mfunga,
    koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.
17 Nʼkwabwino kudya mkute koma pali mtendere,
    kuposa kuchita madyerero mʼnyumba mʼmene muli mikangano.

Kapolo wanzeru adzalamulira mwana wochititsa manyazi,
    ndipo kapoloyo adzagawana nawo cholowa ngati mmodzi mwa abale.

Siliva amamuyesa mʼngʼanjo ndipo golide amamuyesa mʼngʼanjo,
    koma Yehova amayesa mitima.

Munthu woyipa amamvera malangizo oyipa;
    munthu wabodza amatchera khutu mawu osakaza.

Iye amene amalalatira mʼmphawi amanyoza mlengi wake;
    amene amakondwerera tsoka la mnzake sadzakhala osalangidwa.

Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba,
    ndipo makolo ndiye ulemerero wa ana.

Kuyankhula bwino sikuyenerana ndi chitsiru,
    nanji kuyankhula bodza kungayenerane kodi ndi mfumu?

Chiphuphu chili ngati mankhwala amwayi kwa wochiperekayo;
    kulikonse kumene amapita zinthu zimamuyendera.

Iye amene amakhululukira zolakwa za wina, amafunitsitsa chikondi;
    wobwerezabwereza nkhani amapha chibwenzi.

10 Munthu wanzeru amamva kamodzi kokha,
    munthu wopanda nzeru ndi samvamkunkhu.

11 Munthu woyipa maganizo ake ali pa kuwukira basi;
    ndipo bwana adzamutumizira wamthenga wankhanza.

12 Nʼkwabwino kukumana ndi chimbalangondo cholandidwa ana ake
    kusiyana ndi kukumana ndi chitsiru mu uchitsiru wake.

13 Ngati munthu abwezera choyipa kusinthana ndi zabwino,
    ndiye choyipa sichidzachoka mʼnyumba mwake.

14 Chiyambi cha mikangano chili ngati kukhamulira madzi,
    choncho uzichokapo mkangano usanayambe.

15 Kumasula munthu wolakwa kapena kumanga munthu wosalakwa,
    zonse ziwirizi Yehova zimamunyansa.

16 Ndalama zogulira nzeru zili ndi phindu lanji mʼmanja mwa chitsiru
    poti iyeyo mutu wake sumayenda bwino?

17 Bwenzi lako limakukonda nthawi zonse,
    ndipo mʼbale wako anabadwa kuti azikuthandiza pamavuto.

18 Munthu wopanda nzeru amavomereza zopereka chikole
    ndipo iyeyo amasanduka chikole cha mnansi wake.

19 Wokonda zolakwa amakonda mkangano,
    ndipo wokonda kuyankhula zonyada amadziyitanira chiwonongeko.

20 Munthu wamtima woyipa zinthu sizimuyendera bwino;
    ndipo woyankhula zachinyengo amagwa mʼmavuto.

21 Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake,
    abambo a chitsiru sakhala ndi chimwemwe.

22 Mtima wosangalala uli ngati mankhwala abwino,
    koma mtima wokhumudwa umafowoketsa mafupa.

23 Munthu woyipa amalandira chiphuphu chamseri
    kuti apotoze chiweruzo cholungama.

24 Munthu wozindikira zinthu, maso ake amakhala pa nzeru,
    koma chitsiru chimwazamwaza maso ake pa dziko lonse lapansi.

25 Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake
    ndipo amapweteketsa mtima amayi ake.

26 Sibwino kulipitsa munthu wosalakwa,
    kapena kulanga anthu osalakwa.

27 Munthu wosunga pakamwa ndiye wodziwa zinthu,
    ndipo wodekha mtima ndiye womvetsa bwino zinthu.

28 Ngakhale chitsiru chimakhala ngati chanzeru chikakhala chete;
    ndipo chikatseka pakamwa chimakhala ngati munthu wochenjera.
18 Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha;
    iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.

Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu,
    koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.

Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera.
    Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.

Mawu a munthu ali ngati madzi akuya,
    kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.

Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu;
    kapena kupondereza munthu wosalakwa.

Mawu a chitsiru amautsa mkangano;
    pakamwa pake pamayitana mkwapulo.

Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake,
    ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.

Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma;
    amalowa mʼmimba mwa munthu.

Munthu waulesi pa ntchito yake
    ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.

10 Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba;
    wolungama amathawiramo napulumuka.

11 Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba;
    chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.

12 Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada,
    koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.

13 Ukayankha usanamvetse bwino nkhani,
    umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.

14 Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda,
    koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.

15 Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina;
    amafunafuna kudziwa bwino zinthu.

16 Mphatso ya munthu imamutsekulira njira
    yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.

17 Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye
    mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.

18 Kuchita maere kumathetsa mikangano;
    amalekanitsa okangana amphamvu.

19 Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba,
    koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.

20 Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake.
    Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.

21 Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo.
    Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.

22 Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino
    ndipo Yehova amamukomera mtima.

23 Munthu wosauka amapempha
    koma munthu wolemera amayankha mwaukali.

24 Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso,
    koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.