Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Beginning

Read the Bible from start to finish, from Genesis to Revelation.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 140-145

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

140 Landitseni Yehova kwa anthu oyipa;
    tetezeni kwa anthu ankhanza,
amene mu mtima mwawo amakonza zinthu zoyipa
    ndi kuyambitsa nkhondo tsiku lililonse.
Iwo amanola malilime awo kukhala akuthwa ngati a njoka;
    pa milomo yawo pali ululu wa mamba.
            Sela

Tetezeni Inu Yehova, kwa anthu oyipa;
    tchinjirizeni kwa anthu ankhanza
    amene amakonza zokola mapazi anga.
Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika;
    iwo atchera zingwe za maukonde awo
    ndipo anditchera misampha pa njira yanga.
            Sela

Inu Yehova, ine ndikuti, “Ndinu Mulungu wanga.”
    Imvani kupempha kwanga Yehova.
Inu Ambuye Wamphamvuzonse, Mpulumutsi wanga wamphamvu,
    mumateteza mutu wanga tsiku lankhondo.
Musawapatse anthu oyipa zokhumba zawo, Inu Yehova;
    musalole kuti zokonza zawo zitheke,
    mwina iwo adzayamba kunyada.
            Sela

Mitu ya amene andizungulira
    iphimbidwe ndi masautso amene milomo yawo yayambitsa.
10 Makala amoto agwere pa iwo;
    aponyedwe pa moto,
    mʼmaenje amatope, asatulukemonso.
11 Musalole kuti anthu achipongwe akhazikike mʼdziko;
    choyipa chilondole anthu ankhanza.

12 Ndikudziwa kuti Yehova amapereka chiweruzo cholungama kwa anthu osauka,
    ndipo amateteza zolinga za anthu osowa.
13 Zoonadi anthu olungama adzatamanda dzina lanu,
    ndipo anthu owongoka mtima adzakhala pamaso panu.

Salimo la Davide.

141 Inu Yehova ndikukuyitanani; bwerani msanga kwa ine.
    Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu.
Pemphero langa lifike kwa Inu ngati lubani;
    kukweza manja kwanga kukhale ngati nsembe yamadzulo.

Yehova ikani mlonda pakamwa panga;
    londerani khomo la pa milomo yanga.
Musalole kuti mtima wanga ukokedwere ku zoyipa;
    kuchita ntchito zonyansa
pamodzi ndi anthu amene amachita zoyipa;
    musalole kuti ndidye nawo zokoma zawo.

Munthu wolungama andikanthe, chimenecho ndiye chifundo;
    andidzudzule ndiye mafuta pa mutu wanga.
    Mutu wanga sudzakana zimenezi.

Komabe pemphero langa nthawi zonse ndi lotsutsana ndi ntchito za anthu ochita zoyipa.
    Olamulira awo adzaponyedwa pansi kuchokera pa malo okwera kwambiri,
    ndipo anthu oyipa adzaphunzira kuti mawu anga anayankhulidwa bwino.
Iwo adzati, “Monga momwe nkhuni zimamwazikira akaziwaza,
    ndi momwenso mafupa athu amwazikira pa khomo la manda.”

Koma maso anga akupenyetsetsa Inu Ambuye Wamphamvuzonse;
    ndimathawira kwa Inu, musandipereke ku imfa.
Mundipulumutse ku misampha imene anditchera,
    ku makhwekhwe amene anthu oyipa andikonzera.
10 Anthu oyipa akodwe mʼmaukonde awo,
    mpaka ine nditadutsa mwamtendere.

Ndakatulo ya Davide, pamene iyeyo anali mʼphanga. Pemphero.

142 Ndikulirira Yehova mofuwula;
    ndikukweza mawu anga kwa Yehova kupempha chifundo.
Ndikukhuthula madandawulo anga pamaso pake;
    ndikufotokoza za masautso anga pamaso pake.

Pamene mzimu wanga walefuka mʼkati mwanga,
    ndinu amene mudziwa njira yanga.
Mʼnjira imene ndimayendamo
    anthu anditchera msampha mobisa.
Yangʼanani kumanja kwanga ndipo onani;
    palibe amene akukhudzika nane.
Ndilibe pothawira;
    palibe amene amasamala za moyo wanga.

Ndilirira Inu Yehova;
    ndikuti, “Ndinu pothawirapo panga,
    gawo langa mʼdziko la anthu amoyo.”
Mverani kulira kwanga
    pakuti ndathedwa nzeru;
pulumutseni kwa amene akundithamangitsa
    pakuti ndi amphamvu kuposa ine.
Tulutseni mʼndende yanga
    kuti nditamande dzina lanu.

Ndipo anthu olungama adzandizungulira
    chifukwa cha zabwino zanu pa ine.

Salimo la Davide.

143 Yehova imvani pemphero langa,
    mvetserani kulira kwanga kopempha chifundo;
mwa kukhulupirika kwanu ndi chilungamo chanu
    bwerani kudzandithandiza.
Musazenge mlandu mtumiki wanu,
    pakuti palibe munthu wamoyo amene ndi wolungama pamaso panu.

Mdani akundithamangitsa,
    iye wandipondereza pansi;
wachititsa kuti ndikhale mu mdima
    ngati munthu amene anafa kale.
Choncho mzimu wanga ukufowoka mʼkati mwanga;
    mʼkati mwanga, mtima wanga uli ndi nkhawa.

Ndimakumbukira masiku amakedzana;
    ndimalingalira za ntchito yanu yonse,
    ndimaganizira zimene manja anu anachita.
Ndatambalitsa manja anga kwa Inu;
    moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu monga nthaka yowuma.
            Sela

Yehova ndiyankheni msanga;
    mzimu wanga ukufowoka.
Musandibisire nkhope yanu,
    mwina ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
Lolani kuti mmawa ubweretse mawu achikondi chanu chosasinthika,
    pakuti ine ndimadalira Inu.
Mundisonyeze njira yoti ndiyendemo,
    pakuti kwa Inu nditukulira moyo wanga.
Pulumutseni kwa adani anga, Inu Yehova,
    pakuti ndimabisala mwa Inu.
10 Phunzitseni kuchita chifuniro chanu,
    popeza ndinu Mulungu wanga;
Mzimu wanu wabwino unditsogolere
    pa njira yanu yosalala.

11 Sungani moyo wanga Inu Yehova chifukwa cha dzina lanu;
    mwa chilungamo chanu tulutseni mʼmasautso anga.
12 Mwa chikondi chanu chosasinthika khalitsani chete adani anga;
    wonongani adani anga,
    pakuti ndine mtumiki wanu.

Salimo la Davide.

144 Atamandike Yehova Thanthwe langa,
    amene amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo;
    zala zanga kumenya nkhondo.
Iye ndiye Mulungu wanga wachikondi ndi malo anga otetezedwa,
    linga langa ndi mpulumutsi wanga,
chishango changa mmene ine ndimathawiramo,
    amene amagonjetsa mitundu ya anthu pansi panga.

Inu Yehova, munthu nʼchiyani kuti mumamusamalira,
    mwana wa munthu kuti muzimuganizira?
Munthu ali ngati mpweya;
    masiku ake ali ngati mthunzi wosakhalitsa.

Ngʼambani mayiko akumwamba, Inu Yehova, ndipo tsikani pansi;
    khudzani mapiri kuti atulutse utsi.
Tumizani zingʼaningʼani ndi kubalalitsa adani;
    ponyani mivi yanu ndi kuwathamangitsa.
Tambasulani dzanja lanu kuchokera kumwamba;
    landitseni ndi kundipulumutsa,
ku madzi amphamvu,
    mʼmanja mwa anthu achilendo,
amene pakamwa pawo ndi podzala ndi mabodza,
    amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.

Ndidzakuyimbirani nyimbo yatsopano Inu Mulungu;
    ndidzakuyimbirani nyimbo pa zeze wa nsambo khumi,
10 kwa Iye amene amapambanitsa mafumu,
    amene amapulumutsa Davide mtumiki wake ku lupanga loopsa.

11 Landitseni ndi kundipulumutsa,
    mʼmanja mwa anthu achilendo,
amene pakamwa pawo ndi podzaza ndi mabodza,
    amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.

12 Ndipo ana aamuna pa chinyamata chawo
    adzakhala ngati mbewu yosamalidwa bwino,
ana athu aakazi adzakhala ngati zipilala
    zosemedwa bwino, zokongoletsera nyumba yaufumu.
13 Nkhokwe zathu zidzakhala zodzaza
    ndi zokolola za mtundu uliwonse.
Nkhosa zathu zidzaswana miyandamiyanda
    pa mabusa athu.
14     Ngʼombe zathu zidzanyamula katundu wolemera.
Sipadzakhala mingʼalu pa makoma,
    sipadzakhalanso kupita ku ukapolo,
    mʼmisewu mwathu simudzakhala kulira chifukwa cha mavuto.

15 Odala anthu amene adzalandira madalitso awa;
    odala anthu amene Mulungu wawo ndi Yehova.

Salimo la matamando la Davide.

145 Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga;
    ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku
    ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.

Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse;
    ukulu wake palibe angawumvetsetse.
Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina;
    Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu,
    ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri,
    ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu,
    ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.

Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo,
    wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
Yehova ndi wabwino kwa onse;
    amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
10 Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova;
    oyera mtima adzakulemekezani.
11 Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu
    ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
12 kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu
    ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
13 Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya,
    ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse.

Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse
    ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
14 Yehova amagwiriziza onse amene akugwa
    ndipo amakweza onse otsitsidwa.
15 Maso a onse amayangʼana kwa Inu,
    ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
16 Mumatsekula dzanja lanu
    ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.

17 Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse,
    ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
18 Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana,
    onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
19 Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa;
    amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
20 Yehova amayangʼana onse amene amamukonda
    koma adzawononga anthu onse oyipa.

21 Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova.
    Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera
    ku nthawi za nthawi.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.