Beginning
Mawu a Aguri
30 Nawa mawu a Aguri mwana wa Yake wa ku Masa:
Munthuyo anati kwa Itieli, “Inu Mulungu, ine ndatopa.
Inu Mulungu, ine ndatopa. Ndalefukiratu.
2 “Ine ndine munthu wopusa kuposa anthu onse;
ndilibe nzeru zomvetsa zinthu zonga za munthu.
3 Sindinaphunzire nzeru,
ndipo Woyerayo sindimudziwa.
4 Kodi ndani anakwera kumwamba ndi kutsikako?
Ndani anafumbatapo mphepo mʼmanja mwake?
Ndani anamanga madzi mʼchovala chake?
Ndani anakhazikitsa mathero onse a dziko lapansi?
Dzina lake ndani? Ndiwuze ngati ukudziwa!
Ndipo mwana wake dzina lake ndani?
5 “Mawu ali wonse a Mulungu ndi opanda cholakwika;
Iye ndi chishango kwa amene amathawira kwa Iye.
6 Usawonjezepo kanthu pa mawu ake,
kuopa kuti Iye angadzakudzudzule ndi kukupeza kuti ndiwe wabodza.”
7 “Inu Yehova, ndikukupemphani zinthu ziwiri
musandimane zimenezo ndisanafe:
8 Choyamba, mundichotsere kutali nane mabodza ndi chinyengo.
Chachiwiri, ndisakhale mʼmphawi kapena munthu wachuma.
Koma muzindidyetsa chakudya chondikwanira tsiku ndi tsiku
9 kuopa kuti ndikakhuta kwambiri ndingayambe kukukanani,
nʼkumanena kuti, ‘Yehova ndiye yaninso?’
Kuopanso kuti ndikakhala wosauka ndingayambe kuba,
potero nʼkuyipitsa dzina la Mulungu wanga.”
10 “Usamusinjirire wantchito kwa mbuye wake
kuopa kuti angakutemberere ndipo iweyo nʼkupezeka wolakwa.”
11 “Alipo ena amene amatemberera abambo awo,
ndipo sadalitsa amayi awo.
12 Pali ena amene amadziyesa okha oyera mtima
komatu sanachotse zoyipa zawo.
13 Pali ena ndi odzitukumula kwambiri,
amene amakweza zikope modzitukumula.
14 Pali ena amene mano awo ali ngati malupanga
ndipo zibwano zawo zili ngati mipeni
moti amadya amphawi ndi kuwachotsa pa dziko lapansi.
Amachotsanso anthu osauka pakati pa anzawo.”
15 “Msundu uli ndi ana aakazi awiri
iwo amalira kuti, ‘Tipatseni! Tipatseni!’ ”
“Pali zinthu zitatu zimene sizikhuta,
zinthu zinayi zimene sizinena kuti, ‘Takhuta!’
16 Manda, mkazi wosabala,
nthaka yosakhuta madzi
ndiponso moto womangoyakirayakira!”
17 Aliyense amene amanyoza abambo ake,
ndi kunyozera kumvera amayi ake,
makwangwala a ku chigwa adzamukolowola maso
ndipo mphungu zidzadya mnofu wake.
18 Pali zinthu zitatu zimene zimandidabwitsa,
zinthu zinayi zimene ine sindizimvetsetsa.
19 Ndipo ndi izi: mmene chiwulukira chiwombankhanga mlengalenga;
mmene iyendera njoka pa thanthwe;
mmene chiyendera chombo pa nyanja;
ndiponso mmene mwamuna achitira akakhala ndi namwali.
20 Umu ndi mʼmene mkazi amachitira atachita chigololo:
Atatha kudya ndi kupukuta pakamwa pake
iye amanena kuti “Sindinachite kalikonse kolakwa.”
21 Pali zinthu zitatu zimene zimanjenjemeretsa dziko lapansi,
pali zinthu zinayi zimene dziko lapansi silingathe kuzipirira:
22 Kapolo amene wasanduka mfumu,
chitsiru chimene chakhuta,
23 mkazi wonyozeka akakwatiwa
ndiponso wantchito wamkazi akalanda mwamuna wa mbuye wake.
24 Pali zinthu zinayi zingʼonozingʼono pa dziko lapansi,
komatu ndi zochenjera kwambiri:
25 Nyerere zili ngati anthu opanda mphamvu,
komatu zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe;
26 mbira zili ngati anthu opanda mphamvu
komatu zimakonza pokhalapo pawo mʼmiyala;
27 dzombe lilibe mfumu,
komatu lonse limakhala mʼmagulumagulu poyenda.
28 Buluzi ungathe kumugwira mʼmanja
komatu amapezeka mʼnyumba za mafumu.
29 “Pali zinthu zitatu zimene zimayenda chinyachinya,
pali zinthu zinayi zimene zimayenda monyadira:
30 Mkango umene uli wamphamvu kuposa nyama zonse,
ndipo suthawa kanthu kalikonse.
31 Tambala woyenda chinyachinya, mbuzi yayimuna,
ndiponso mfumu yoyenda pakati pa anthu ake.
32 “Ngati wakhala ukupusa ndi kumadzikweza wekha,
kapena ngati wakhala ukukonzekera zoyipa,
ndiye khala kaye chete, uganizire bwino!
33 Paja pakutha mkaka mafuta amapangidwa,
ndipo ukapsinya mphuno, magazi amatuluka,
ndipo mikangano imakhalapo ukalimbikira kukwiya.”
Mawu a Mfumu Lemueli
31 Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake:
2 Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga?
Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro?
3 Usapereke mphamvu yako kwa akazi.
Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu.
4 Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu,
mafumu sayenera kumwa vinyo.
Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa
5 kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko,
nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka.
6 Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa,
vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa;
7 amwe kuti ayiwale umphawi wawo
asakumbukirenso kuvutika kwawo.
8 Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha.
Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera.
9 Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo.
Uwateteze amphawi ndi osauka.
Mathero: Mkazi Wangwiro
10 Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani?
Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.
11 Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira
ndipo mwamunayo sasowa phindu.
12 Masiku onse a moyo wake
mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.
13 Iye amafunafuna ubweya ndi thonje;
amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.
14 Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda,
amakatenga chakudya chake kutali.
15 Iye amadzuka kusanache kwenikweni;
ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya
ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.
16 Iye amalingalira za munda ndi kuwugula;
ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.
17 Iye amavala zilimbe
nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.
18 Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu,
choncho nyale yake sizima usiku wonse.
19 Iye amadzilukira thonje
ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.
20 Iye amachitira chifundo anthu osauka
ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.
21 Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu;
pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda.
22 Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake;
amavala zovala zabafuta ndi zapepo.
23 Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda,
ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo.
24 Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa;
amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.
25 Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake;
ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo.
26 Iye amayankhula mwanzeru,
amaphunzitsa anthu mwachikondi.
27 Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake
ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe.
28 Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala;
ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati,
29 “Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana
koma iwe umawaposa onsewa.”
30 Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa;
koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa.
31 Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita
ndipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.