Beginning
106 Tamandani Yehova.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;
pakuti chikondi chake ndi chosatha.
2 Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova
kapena kumutamanda mokwanira?
3 Odala ndi amene amasunga chilungamo,
amene amachita zolungama nthawi zonse.
4 Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu,
bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
5 kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika,
kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu
ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
6 Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu;
tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
7 Pamene makolo athu anali mu Igupto,
sanalingalire za zozizwitsa zanu;
iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka,
ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
8 Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake,
kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
9 Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma;
anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
10 Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo;
anawawombola mʼdzanja la mdani.
11 Madzi anamiza adani awo,
palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
12 Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake
ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
13 Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita,
ndipo sanayembekezere uphungu wake.
14 Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo;
mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
15 Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha,
koma anatumiza nthenda yowondetsa.
16 Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni,
amene Yehova anadzipatulira.
17 Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani;
inakwirira gulu la Abiramu.
18 Moto unayaka pakati pa otsatira awo;
lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
19 Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu
ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
20 Anasinthanitsa ulemerero wawo
ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
21 Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa,
amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
22 zozizwitsa mʼdziko la Hamu
ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
23 Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga,
pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa,
kuyima pamaso pake,
ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
24 Motero iwo ananyoza dziko lokoma;
sanakhulupirire malonjezo ake.
25 Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo
ndipo sanamvere Yehova.
26 Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake,
kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
27 kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina
ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
28 Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori
ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
29 anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa,
ndipo mliri unabuka pakati pawo.
30 Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo,
ndipo mliri unaleka.
31 Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake,
kwa mibado yosatha imene ikubwera.
32 Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova
ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
33 pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu,
ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
34 Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu
monga momwe Yehova anawalamulira.
35 Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo
ndi kuphunzira miyambo yawo.
36 Ndipo anapembedza mafano awo,
amene anakhala msampha kwa iwowo.
37 Anapereka nsembe ana awo aamuna
ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
38 Anakhetsa magazi a anthu osalakwa,
magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi,
amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani,
ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
39 Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita;
ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
40 Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake
ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
41 Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina,
ndipo adani awo anawalamulira.
42 Adani awo anawazunza
ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
43 Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri,
koma iwo ankatsimikiza za kuwukira
ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
44 Koma Iye anaona kuzunzika kwawo
pamene anamva kulira kwawo;
45 Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake
ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
46 Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo
awamvere chisoni.
47 Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu,
ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina
kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera
ndi kunyadira mʼmatamando anu.
48 Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli,
Kuyambira muyaya mpaka muyaya.
Anthu onse anene kuti, “Ameni!”
Tamandani Yehova.
BUKU LACHISANU
Masalimo 107–150
107 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;
pakuti chikondi chake ndi chosatha.
2 Owomboledwa a Yehova anene zimenezi
amene Iyeyo anawawombola mʼdzanja la mdani,
3 iwo amene anawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko,
kuchokera kumadzulo ndi kummawa, kuchokera kumpoto ndi kummwera.
4 Ena anayendayenda mʼchipululu mopanda kanthu,
osapeza njira yopitira ku mzinda kumene akanakakhazikikako.
5 Iwo anamva njala ndi ludzu,
ndipo miyoyo yawo inafowokeratu.
6 Pamenepo analirira Yehova mʼmavuto awo
ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.
7 Iye anawatsogolera mʼnjira yowongoka
kupita ku mzinda umene anakakhazikikako.
8 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
ndi chifukwa cha machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,
9 pakuti Iye wapha ludzu la munthu womva ludzu
ndipo wakhutitsa wanjala ndi zinthu zabwino.
10 Ena anakhala mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu,
amʼndende ovutika mʼmaunyolo achitsulo,
11 pakuti iwowo anawukira mawu a Mulungu
ndi kunyoza uphungu wa Wammwambamwamba.
12 Kotero Iye anawapereka kuti agwire ntchito yakalavulagaga;
anagwa pansi ndipo panalibe woti awathandize.
13 Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo
ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.
14 Yehova anawatulutsa mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu
ndipo anadula maunyolo awo.
15 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,
16 pakuti Iye amathyola zipata zamkuwa
ndi kudula pakati mipiringidzo yachitsulo.
17 Ena anakhala zitsiru chifukwa cha njira zawo zowukira,
ndipo anamva zowawa chifukwa cha mphulupulu zawo.
18 Iwo ananyansidwa ndi chakudya chilichonse
ndipo anafika pafupi ndi zipata za imfa.
19 Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo
ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awowo.
20 Iye anatumiza mawu ake ndi kuwachiritsa;
anawalanditsa ku manda.
21 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.
22 Apereke nsembe yachiyamiko
ndi kufotokoza za ntchito zake ndi nyimbo zachimwemwe.
23 Ena anayenda pa nyanja mʼsitima zapamadzi;
Iwo anali anthu amalonda pa nyanja yayikulu.
24 Anaona ntchito za Yehova,
machitidwe ake odabwitsa mʼnyanja yakuya.
25 Pakuti Iye anayankhula ndi kuwutsa mphepo yamkuntho
imene inabweretsa mafunde ataliatali.
26 Sitima za pamadzizo zinatukulidwa mmwamba ndi kutsikira pansi pakuya;
pamene amawonongeka, kulimba mtima kwawo kunasungunuka.
27 Anachita chizungulire ndi kudzandira ngati anthu oledzera;
anali pa mapeto a moyo wawo.
28 Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo
ndipo Iyeyo anawapulumutsa ku masautso awo.
29 Yehova analetsa namondwe,
mafunde a mʼnyanja anatontholetsedwa.
30 Anali osangalala pamene kunakhala bata,
ndipo Iye anawatsogolera ku dooko limene amalifuna.
31 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.
32 Akuze Iye mu msonkhano wa anthu
ndi kumutamanda pabwalo la akuluakulu.
33 Iye anasandutsa mitsinje kukhala chipululu,
akasupe otuluka madzi kukhala nthaka yowuma,
34 ndiponso nthaka yachonde kukhala nthaka yamchere,
chifukwa cha kuyipa kwa amene amakhala kumeneko.
35 Anasandutsa chipululu kukhala mayiwe a madzi
ndi nthaka yowuma kukhala akasupe a madzi oyenda;
36 kumeneko Iye anabweretsa anthu anjala kuti azikhalako,
ndipo iwo anamanga mzinda woti akhazikikeko.
37 Anafesa mbewu mʼminda ndi kudzala mipesa
ndipo anakolola zipatso zochuluka;
38 Yehova anawadalitsa, ndipo chiwerengero chawo chinachuluka kwambiri,
ndipo Iye sanalole kuti ziweto zawo zithe.
39 Kenaka chiwerengero chawo chinachepa ndipo iwo anatsitsidwa
chifukwa cha mazunzo, mavuto ndi chisoni;
40 Iye amene amakhuthulira mʼnyozo pa olemekezeka
anawachititsa kuyendayenda mʼmalo owumawo wopanda njira.
41 Koma Iyeyo anakweza anthu osowa kuchoka ku masautso awo
ngati magulu a nkhosa.
42 Anthu olungama mtima amaona ndi kusangalala,
koma anthu onse oyipa amatseka pakamwa pawo.
43 Aliyense wanzeru asamalitse zinthu zimenezi
ndi kuganizira za chikondi chachikulu cha Yehova.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.