Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

M’Cheyne Bible Reading Plan

The classic M'Cheyne plan--read the Old Testament, New Testament, and Psalms or Gospels every day.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
1 Mbiri 3-4

Ana a Davide

Ana aamuna a Davide amene anabadwira ku Hebroni anali awa:

Woyamba anali Amnoni, amayi ake anali Ahinoamu wa ku Yezireeli;

wachiwiri anali Danieli, amayi ake anali Abigayeli wa ku Karimeli;

wachitatu anali Abisalomu, mwana wa Maaka mwana wa Talimai mfumu ya Gesuri;

wachinayi anali Adoniya amayi ake anali Hagiti;

wachisanu anali Sefatiya, amayi ake anali Abitali;

wachisanu ndi chimodzi anali Itireamu, amayi ake anali Egila.

Ana asanu ndi mmodzi awa a Davide anabadwira ku Hebroni kumene analamulirako zaka zisanu ndi ziwiri ndi miyezi isanu ndi umodzi.

Davide analamuliranso mu Yerusalemu kwa zaka 33, ndipo ana amene anabadwira ku Yerusalemuko anali awa:

Samua, Sobabu, Natani ndi Solomoni. Ana anayi awa anali a Batisuwa mwana wa Amieli. Anaberekanso Ibihari, Elisua, Elipeleti, Noga, Nefegi, Yafiya, Elisama, Eliada ndi Elifeleti, onse analipo asanu ndi anayi. Onsewa anali ana a Davide, osawerengera ana a azikazi. Ndipo mlongo wawo anali Tamara.

Mafumu a Yuda

10 Mwana wa Solomoni anali Rehabiamu,

Rehabiamu anabereka Abiya,

Abiya anabereka Asa,

Asa anabereka Yehosafati,

11 Yehosafati anabereka Yehoramu,

Yehoramu anabereka Ahaziya,

Ahaziya anabereka Yowasi,

12 Yowasi anabereka Amaziya,

Amaziya anabereka Azariya,

Azariya anabereka Yotamu,

13 Yotamu anabereka Ahazi,

Ahazi anabereka Hezekiya,

Hezekiya anabereka Manase,

14 Manase anabereka Amoni,

Amoni anabereka Yosiya.

15 Ana a Yosiya anali awa:

Yohanani mwana wake woyamba,

Yehoyakimu mwana wake wachiwiri,

Zedekiya mwana wake wachitatu,

Salumu mwana wake wachinayi.

16 Ana a Yehoyakimu:

Yekoniya

ndi Zedekiya mwana wake.

Mayina a Mafumu Utatha Ukapolo

17 Zidzukulu za Yekoniya wa mʼndende zinali izi:

mwana wake Silatieli, 18 Malikiramu, Pedaya, Senazara, Yekamiya, Hosama ndi Nedabiya.

19 Ana a Pedaya anali awa:

Zerubabeli ndi Simei.

Ana a Zerubabeli anali awa:

Mesulamu ndi Hananiya.

Mlongo wawo anali Selomiti.

20 Panalinso ana ena asanu awa:

Hasubu, Oheli, Berekiya, Hasabiya ndi Yusabu-Hesedi.

21 Zidzukulu za Hananiya zinali izi:

Pelatiya ndi Yesaiya, ndiponso ana a Refaya, ana a Arinani, ana a Obadiya ndi ana a Sekaniya.

22 Zidzukulu za Sekaniya zinali izi:

Semaya ndi ana ake:

Hatusi, Igala, Bariya, Neariya ndi Safati. Onse anali asanu ndi mmodzi.

23 Ana a Neariya anali awa:

Eliyoenai, Hezekiya ndi Azirikamu. Onse anali atatu.

24 Ana a Eliyoenai: Hodaviya, Eliyasibu, Pelaya, Akubu,

Yohanani, Delaya ndi Anani, onse anali asanu ndi awiri.

Mabanja Ena a Yuda

Ana a Yuda anali awa:

Perezi, Hezironi, Karimi, Huri ndi Sobali.

Reaya mwana wa Sobala anabereka Yahati, ndipo Yahati anabereka Ahumai ndi Lahadi. Awa anali mabanja a Azorati.

Ana a Etamu anali awa:

Yezireeli, Isima ndi Idibasi. Dzina la mlongo wawo linali Hazeleliponi. Penueli anabereka Gedori, ndipo Ezeri anabereka Husa.

Awa anali ana a Huri, mwana wachisamba wa Efurata ndi abambo a Betelehemu.

Asihuri abambo a Tekowa anali ndi akazi awiri, Hela ndi Naara.

Naara anamuberekera Ahuzamu, Heferi, Temani ndi Haahasitari. Awa ndiwo anali ana a Naara.

Ana a Hela:

Zereti, Zohari, Etinani, ndi Kozi, amene anali abambo ake a Anubi ndi Hazo-Beba ndi mabanja a Ahariheli mwana wa Harumi.

Yabesi anali munthu wolemekezeka kwambiri kuposa abale ake. Amayi ake anamutcha Yabesi kutanthauza kuti, “Chifukwa ndinamubala ndi ululu wambiri.” 10 Yabesi analira kwa Mulungu wa Israeli kuti, “Mundidalitse ndipo mukulitse dziko langa! Dzanja lanu likhale pa ine ndipo mundisunge kuti choyipa chisandigwere ndi kundisautsa.” Ndipo Mulungu anamupatsa chopempha chakecho.

11 Kelubi, mʼbale wa Suha, anabereka Mehiri, amene anabereka Esitoni. 12 Esitoni anabereka Beti-Rafa, Paseya ndi Tehina amene anabereka Iri Nahasi. Amenewa ndiwo anthu a ku Reka.

13 Ana a Kenazi anali awa:

Otanieli ndi Seraya.

Ana a Otanieli anali awa:

Hatati ndi Meonotai. 14 Meonotai anabereka Ofura.

Seraya anabereka Yowabu,

amene anabereka Ge-Harasimu. Anawatcha dzina ili chifukwa anthu ake anali amisiri.

15 Ana a Kalebe mwana wa Yefune anali awa:

Iru, Ela ndi Naama.

Mwana wa Ela anali

Kenazi.

16 Ana a Yehaleleli anali awa:

Zifi, Zifa, Tiriya ndi Asareli.

17 Ana a Ezara anali awa:

Yeteri, Meredi, Eferi ndi Yaloni. Mmodzi mwa akazi a Meredi anabereka Miriamu, Samai ndi Isiba abambo ake a Esitemowa. 18 (Mkazi wake wa Chiyuda anabereka Yaredi abambo ake a Gedori, Heberi abambo ake a Soko ndi Yekutieli abambo a Zanowa). Awa anali ana a mwana wamkazi wa Farao, Bitia, amene Meredi anakwatira.

19 Ana a mkazi wa Hodiya, mlongo wa Nahamu anali awa:

abambo ake a Keila wa ku Garimi ndi Esitemowa wa ku Maaka.

20 Ana a Simeoni anali awa:

Amnoni, Rina, Beni-Hanani ndi Tiloni.

Ana a Isi anali awa:

Zoheti ndi Beni-Zoheti.

21 Ana a Sela mwana wa Yuda anali awa:

Eri amene anabereka Leka, Laada amene anabereka Maresa ndi mabanja a anthu owomba nsalu zofewa ndi zosalala a ku Beti-Asibeya, 22 Yokimu, anthu a ku Kozeba, ndiponso Yowasi ndi Sarafi, amene ankalamulira Mowabu ndi Yasibu-Lehemu. (Nkhani zimenezi ndi zakalekale). 23 Iwo anali owumba mbiya amene ankakhala ku Netaimu ndi Gederi. Ankakhala kumeneko ndi kumatumikira mfumu.

Simeoni

24 Ana a Simeoni anali awa:

Nemueli, Yamini, Yaribu, Zera ndi Sauli;

25 Salumu anali mwana wa Sauli, Mibisamu anali mwana wa Salumu ndipo Misima anali mwana wa Mibisamu.

26 Zidzukulu za Misima zinali izi:

Hamueli, Zakuri ndi Simei.

27 Simei anali ndi ana aamuna 16 ndi ana aakazi 6, koma abale ake sanabereke ana ambiri; kotero banja lawo silinakule ngati anthu ena a ku Yuda. 28 Iwo amakhala ku Beeriseba, Molada, Hazari-Suwali, 29 Biliha, Ezemu, Toladi, 30 Betueli, Horima, Zikilagi, 31 Beti-Marikaboti, Hazari-Susimu, Beti-Biri ndi Saaraimu. Iyi inali mizinda yawo mpaka pa nthawi ya ulamuliro wa Davide. 32 Midzi yowazungulira inali Etamu, Aini, Rimoni, Tokeni ndi Asani, midzi isanu 33 ndi midzi yonse yozungulira mizinda imeneyi mpaka ku Baala. Awa anali malo awo okhalapo. Ndipo anasunga mbiri ya makolo awo.

34 Mesobabu, Yamuleki, Yosa mwana wa Amaziya, 35 Yoweli, Yehu mwana wa Yosibiya, mwana wa Seraya, mwana wa Asieli, 36 komanso Eliyoenai, Yaakoba, Yesohaya, Asaya, Adieli, Yesimieli, Benaya, 37 ndiponso Ziza mwana wa Sifi, mwana wa Aloni, mwana wa Yedaya, mwana wa Simiri, mwana wa Semaya.

38 Anthu amene atchulidwawa anali atsogoleri a mabanja awo. Mabanja awo anakula kwambiri 39 ndipo anakafika ku malire a Gedori ku chigwa cha kummawa kufuna msipu wodyetsa ziweto zawo. 40 Anapeza msipu wobiriwira ndi wabwino ndipo dziko linali lalikulu, la mtendere ndi bata. Kumeneko kunkakhala fuko la Hamu poyamba.

41 Anthu amene mayina awowa alembedwa, anabwera pa nthawi ya Hezekiya mfumu ya Yuda. Iwo anathira nkhondo fuko la Hamu mʼmalo awo amene amakhala komanso Ameuni amene anali kumeneko ndipo anawononga onsewo kotero kuti mbiri yawo simvekanso mpaka lero lino. Kotero iwo anakhala mʼmalo awo chifukwa kunali msipu wa ziweto zawo. 42 Ndipo anthu 500 a fuko la Simeoni, motsogozedwa ndi Pelatiya, Neariya, Refaya ndi Uzieli, ana a Isi, analanda dziko lamapiri la Seiri. 43 Iwo anapha Aamaleki otsala amene anali atapulumuka ndipo akukhala kumeneko mpaka lero lino.

Ahebri 9

Kupembedza mʼTenti ya Dziko Lapansi

Pangano loyamba lija linali ndi malamulo okhudza chipembedzo, ndi malo opembedzeramo omangidwa ndi anthu. Anthu ankamanga chihema. Mʼchipinda choyamba munali choyikapo nyale, tebulo ndi buledi woperekedwa kwa Mulungu. Chipinda chimenechi chinkatchedwa Malo Opatulika. Kuseri kwa chinsalu chotchinga chachiwiri kunkatchedwa Malo Opatulika kwambiri. Mʼmenemo munali guwa lansembe lagolide lofukizirapo lubani. Munalinso Bokosi la Chipangano lokutidwa ndi golide. Mʼbokosimo munali mʼphika wagolide mʼmene ankasungiramo mana ndi ndodo ya Aaroni imene inaphuka ija, ndiponso miyala ya pangano. Pamwamba pa bokosilo panali zifanizo za angelo otchedwa akerubi aulemerero, ataphimba chivundikiro cha bokosilo chimene chinali malo okhululukirapo machimo. Koma nʼzosatheka tsopano kufotokoza zinthu mwatsatanetsatane.

Zinthu zonsezi zitakonzedwa, ansembe ankalowamo mʼchipinda choyamba chija nthawi ndi nthawi kumatumikiramo. Koma Mkulu wa ansembe yekha ndiye ankalowa chipinda chachiwiri chija kamodzi kokha pa chaka. Iye sankalowamo wopanda magazi. Magaziwo ankapereka nsembe kwa Mulungu chifukwa cha iye mwini ndiponso chifukwa cha machimo a anthu amene ankachita mosazindikira. Mwa njira imeneyi Mzimu Woyera ankaonetsa kuti njira yolowera ku malo opatulika inali isanaonetsedwe pamene Chihema choyamba chinali chilipo. Zimenezi nʼzofanizira chabe, ndipo zinkalozera nthawi ino, kusonyeza kuti mphatso ndi nsembe zimene zinkaperekedwa sizinkachotsa chikumbumtima cha wopembedzayo. 10 Inali nkhani ya zakudya, ya zakumwa ndi ya miyambo yosiyanasiyana ya masambidwe. Anali malamulo akunja kokha mpaka pa nthawi imene anakonzanso zonse mwatsopano.

Magazi a Yesu

11 Koma Khristu atafika monga Mkulu wa ansembe wa zinthu zokoma zimene zilipo tsopano, Iye analowa mʼChihema chachikulu ndiponso changwiro chimene sichinamangidwe ndi munthu, ndiye kuti sichili pansi pano. 12 Iye sanalowemo ndi magazi ambuzi yayimuna, ana angʼombe amphongo, koma analowa Malo Opatulika kamodzi kokha ndi magazi ake, atatikonzera chipulumutso chosatha. 13 Ngati magazi ambuzi yayimuna, angʼombe yayimuna ndi phulusa la mwana wangʼombe wamkazi zimati zikawazidwa pa odetsedwa zimawayeretsa kotero kuti amakhala oyeretsedwa ku thupi, 14 nʼkoposa kotani magazi a Khristu, amene mwa Mzimu wamuyaya anadzipereka yekha kwa Mulungu kukhala nsembe yopanda chilema. Iye adzayeretsa chikumbumtima chathu pochotsa ntchito za imfa, kuti ife titumikire Mulungu wamoyo.

15 Pa chifukwa chimenechi Khristu ndi mʼkhalapakati wa pangano latsopano, kuti iwo amene anayitanidwa alandire chuma chamuyaya, pakuti Iye tsopano anafa ngati dipo lomasula iwo ku machimo amene anachita ali pansi pa pangano loyamba lija.

16 Ngati munthu alemba pangano losiyira ena chuma, pafunika kutsimikiza kuti wolemba panganolo wamwaliradi, 17 chifukwa pangano lotere limakhala ndi mphamvu ngati wolembayo wamwalira. Siligwira ntchito pamene wolembayo ali ndi moyo. 18 Nʼchifukwa chake pangano loyamba lija silinachitike popanda kukhetsa magazi. 19 Mose atawawuza anthu onse malamulo, anatenga magazi a ana angʼombe amphongo ndi ambuzi yayimuna pamodzi ndi madzi, ubweya wofiira ndiponso chitsamba chotchedwa hisope, ndi kuwaza pa buku ndi anthu onse. 20 Iye anati, “Awa ndi magazi a pangano limene Mulungu wakulamulirani kuti mulisunge.” 21 Momwemonso Mose anawaza magazi pa Chihema chija ndiponso pa zipangizo zonse zogwiritsa ntchito pa chipembedzo. 22 Monga mwa malamulo titha kunena kuti, pafupifupi zinthu zonse zimayeretsedwa ndi magazi ndipo popanda kukhetsa magazi palibe kukhululukidwa machimo.

23 Tsono panafunika kuti zinthu zingofanizira zenizeni za kumwamba, ziyeretsedwe ndi nsembe zimenezi, koma zinthu za kumwamba zenizenizo kuti ziyeretsedwe panafunika nsembe zina zoposa zimenezo. 24 Pakuti Khristu sanalowe mʼmalo opatulika omangidwa ndi anthu amene anali chifaniziro cha malo enieniwo. Iye analowa kumwamba kwenikweniko kuti azionekera pamaso pa Mulungu chifukwa cha ife. 25 Iye sanalowe kumwamba kuti azikadziperekanso nsembe kachiwiri monga momwe mkulu wa ansembe ankachitira chaka ndi chaka ku Malo Opatulika kwambiri ndi magazi amene sanali ake. 26 Zikanatero bwenzi Khristu atamva zowawa kambirimbiri chilengedwere cha dziko lapansi. Koma tsopano anaoneka kamodzi kokha chifukwa cha onse pa nthawi yotsiriza kuti achotse tchimo podzipereka yekha nsembe. 27 Popeza kunayikika kwa munthu kufa kamodzi ndipo kenaka kuweruzidwa, 28 momwemonso Khristu anadzipereka nsembe kamodzi kokha kuchotsa machimo a anthu ambiri. Ndipo Iye adzaonekanso kachiwiri, osati kudzachotsa tchimo, koma kudzapereka chipulumutso kwa amene akumudikira.

Amosi 3

Mboni Zotsutsa Israeli

Inu Aisraeli, imvani mawu awa amene Yehova wayankhula kutsutsana nanu, kutsutsana ndi banja lonse limene analitulutsa mu Igupto:

“Inu nokha ndi amene ndinakusankhani
    pakati pa mabanja onse a dziko lapansi;
nʼchifukwa chake ndidzakulangani
    chifukwa cha machimo anu onse.”

Kodi anthu awiri nʼkuyendera limodzi
    asanapangane?
Kodi mkango umabangula mʼnkhalango
    usanagwire nyama?
Kodi msona wamkango umalira mʼphanga mwake
    pamene sunagwire kanthu?
Kodi mbalame nʼkutera pa msampha
    pamene palibe nyambo yake?
Kodi msampha umafwamphuka
    usanakole kanthu?
Kodi pamene lipenga la nkhondo lalira mu mzinda,
    anthu sanjenjemera?
Pamene tsoka lafika mu mzinda,
    kodi si Yehova amene wachititsa zimenezo?

Zoonadi Ambuye Yehova sachita kanthu
    asanawulule zimene akufuna kuchita
    kwa atumiki ake, aneneri.

Mkango wabangula,
    ndani amene sachita mantha?
Ambuye Yehova wayankhula,
    ndani amene sanganenere?

Lengezani zimenezi ku nyumba zaufumu za ku Asidodi
    ndiponso ku nyumba zaufumu za ku Igupto:
“Sonkhanani ku mapiri a ku Samariya;
    onani chisokonezo pakati pake
    ndiponso kuponderezana pakati pa anthu ake.”

10 “Iwo sadziwa kuchita zolungama,
    ndipo amadzaza malo awo otetezedwa ndi zinthu zolanda ku nkhondo ndi zakuba,” akutero Yehova.

11 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akunena izi:

“Mdani adzalizungulira dzikoli;
    iye adzagwetsa malinga ako,
    ndi kufunkha nyumba zako zaufumu.”

12 Yehova akuti,

“Monga mʼbusa amalanditsa mʼkamwa mwa mkango
    miyendo iwiri yokha kapena msonga yokha ya khutu,
    moteronso ndimo mmene adzapulumukire Aisraeli
amene amakhala mu Samariya
    pa msonga za mabedi awo,
    ndi ku Damasiko pa akakhutagona awo.”

13 “Imvani izi ndipo mupereke umboni wotsutsa nyumba ya Yakobo,” akutero Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.

14 “Pa tsiku limene ndidzalange Israeli chifukwa cha machimo ake,
    ndidzagumula maguwa ansembe a ku Beteli;
nyanga za guwa zidzathyoka
    ndipo zidzagwa pansi.
15 Ndidzagwetsa nyumba ya pa nthawi yozizira
    pamodzi ndi nyumba ya pa nthawi yotentha;
nyumba zokongoletsedwa ndi minyanga ya njovu zidzawonongedwa
    ndipo nyumba zikuluzikulu zidzaphwasulidwa,”
            akutero Yehova.

Masalimo 146-147

146 Tamandani Yehova.

Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
    Ndidzatamanda Yehova ndi moyo wanga wonse;
    ndidzayimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.

Musamadalire mafumu,
    anthu osakhalitsa, amene sangathe kupulumutsa.
Pamene mizimu yawo yachoka, iwo amabwerera ku dothi;
    zimene ankafuna kuchita zimatha tsiku lomwelo.

Wodala ndi amene thandizo lake ndi
    Mulungu wa Yakobo.
Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi,
    nyanja ndi zonse zili mʼmenemo;
    Yehova, amene ndi wokhulupirika kwamuyaya.
Iye amachitira chilungamo anthu oponderezedwa
    ndipo amapereka chakudya kwa anthu anjala.
Yehova amamasula amʼndende,
    Yehova amatsekula maso anthu osaona,
Yehova amadzutsa onse amene awerama pansi,
    Yehova amakonda anthu olungama.
Yehova amasamalira alendo
    ndipo amathandiza ana ndi akazi amasiye,
    koma amasokoneza njira za anthu oyipa.

10 Yehova ndiye Mfumu mpaka muyaya,
    Mulungu wako iwe Ziyoni, pa mibado yonse.

Tamandani Yehova.
147 Tamandani Yehova.

Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu,
    nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!

Yehova akumanga Yerusalemu;
    Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
Akutsogolera anthu osweka mtima
    ndi kumanga mabala awo.

Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi,
    ndipo iliyonse amayitchula dzina.
Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri;
    nzeru zake zilibe malire.
Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa,
    koma amagwetsa pansi anthu oyipa.

Imbirani Yehova ndi mayamiko;
    imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo;
    amapereka mvula ku dziko lapansi
    ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe
    ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.

10 Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo,
    kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
11 Yehova amakondwera ndi amene amamuopa,
    amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.

12 Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu;
    tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
13 pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako
    ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
14 Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako
    ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.

15 Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi;
    mawu ake amayenda mwaliwiro.
16 Amagwetsa chisanu ngati ubweya
    ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
17 Amagwetsa matalala ngati miyala.
    Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
18 Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka;
    amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.

19 Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo,
    malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
20 Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu;
    anthu enawo sadziwa malamulo ake.

Tamandani Yehova.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.