Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

M’Cheyne Bible Reading Plan

The classic M'Cheyne plan--read the Old Testament, New Testament, and Psalms or Gospels every day.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
1 Samueli 18

Sauli Achitira Nsanje Davide

18 Davide atatha kuyankhula ndi Sauli, mtima wa Yonatani unagwirizana ndi mtima wa Davide, ndipo iye ankamukonda Davide monga momwe ankadzikondera yekha. Choncho Sauli anamusunga Davideyo kuyambira tsiku limenelo ndipo sanamulole kuti abwerere ku nyumba ya abambo ake. Ndipo Yonatani anapanga pangano ndi Davide chifukwa ankamukonda monga momwe ankadzikondera. Yonatani anavula mkanjo umene anavala ndipo anamupatsa Davide pamodzi ndi zovala za nkhondo, lupanga, uta ndi lamba.

Davide ankapita kulikonse kumene Sauli ankamutuma kuti apite kukamenya nkhondo, ndipo ankapambana. Choncho Sauli anamupatsa udindo woyangʼanira gulu lankhondo. Ichi chinakondweretsa anthu onse ngakhalenso atsogoleri a nkhondo a Sauli.

Anthu akubwerera kwawo Davide atapha Mfilisiti uja, amayi anatuluka mʼmizinda yonse ya Israeli, akuyimba ndi kuvina kukachingamira mfumu Sauli. Ankayimba ndi kuvina mokondwa, kwinaku ngʼoma ndi zitoliro zikulira. Amayiwo ankalandizana nyimbo mokondwera namati:

“Sauli wapha 1,000,
    Koma Davide wapha miyandamiyanda.”

Koma Sauli anapsa mtima kwambiri ndipo mawu amenewa anamuyipira. Iye anati, “Iwo amuwerengera Davide miyandamiyanda, koma ine 1,000 okha. Nanga chatsalanso nʼchiyani kuti atenge? Si ufumu basi?” Ndipo kuyambira tsiku limeneli Sauli ankamuchitira nsanje Davide.

10 Mmawa mwake mzimu woyipa uja unabwera mwamphamvu pa Sauli. Sauli anayamba kubwebweta mʼnyumba mwake. Davide ankamuyimbira zeze monga nthawi zonse. Sauli anali ndi mkondo mʼdzanja lake. 11 Tsono anawuponya mkondowo, namati mu mtima mwake, “Ndimubaya Davide ndi kumukhomera ku khoma.” Koma Davide anawulewa kawiri konse.

12 Pambuyo pake Sauli amamuopa Davide chifukwa Yehova anali ndi Davideyo, nʼkumusiya Sauli. 13 Kotero Sauli anamuchotsa Davide pamaso pake ndi kumuyika kukhala mtsogoleri wa ankhondo 1,000. Choncho Davide ankapita ndi kubwera akutsogolera ankhondowa. 14 Davide ankapambana kwambiri pa chilichonse chimene amachita chifukwa Yehova anali naye. 15 Sauli ataona momwe Davide ankapambanira, iye anamuopa kwambiri. 16 Koma Aisraeli onse ndi anthu a Yuda ankamukonda Davide chifukwa ankawatsogolera pa nkhondo zawo.

17 Tsiku lina Sauli anawuza Davide kuti, “Nayu Merabi mwana wanga wamkazi wamkulu. Ine ndakupatsa kuti umukwatire. Koma unditumikire molimba mtima pomenya nkhondo za Yehova.” Poteropo Sauli ankanena kuti, “Ndisamuphe ndi manja angawa koma aphedwe ndi Afilisti!”

18 Ndipo Davide anati kwa Sauli, “Ine ndine yani, ndipo abale anga kapena banja la abambo anga ndife yani mʼdziko la Israeli kuti ndikhale mpongozi wa mfumu?” 19 Koma pa nthawi yoti Merabi mwana wa Sauli akwatiwe ndi Davide, Sauli anamupereka kwa Adrieli wa ku Mehola kuti amukwatire.

20 Koma Mikala mwana wamkazi wa Sauli anamukonda Davide ndipo Sauli atamva za zimenezi, anakondwera. 21 Sauli ankaganiza kuti, “Ndimupatse amukwatire kuti akhale ngati msampha kwa Davideyo, ndipo adzaphedwe ndi Afilisti.” Choncho Sauli anawuza Davide kachiwiri, “Tsopano udzakhala mkamwini wanga.”

22 Sauli analamulanso nduna zake kuti, “Muyankhuleni Davide mwamseri ndi kumuwuza kuti, ‘Taona, mfumu imakondwera nawe, ndipo nduna zake zonse zimakukonda. Tsono ukhale mkamwini wa mfumu.’ ”

23 Iwo anakamuwuza Davide mawu amenewa, koma Davide anati, “Kodi inu mukuganiza kuti ndi chinthu chapafupi kukhala mpongozi wa mfumu? Ine ndine wosauka ndiponso wosatchuka.”

24 Nduna za Sauli zinamuwuza zonse zimene anayankha Davide. 25 Sauli anayankha kuti, “Kamuwuzeni Davide kuti, ‘Mfumu sikufuna malowolo a mtundu wina uliwonse koma timakungu ta msonga za mavalo a Afilisti 100 kuti ilipsire adani ake.’ ” Maganizo a Sauli anali akuti Davide aphedwe ndi Afilisti.

26 Nduna za Saulizo zitamuwuza Davide zimenezi, anakondwera kuti akhale mpongozi wa mfumu. Koma nthawi imene anapatsidwa isanathe, 27 Davide ndi anyamata ake anapita ndi kukapha Afilisti 200. Iye anabwera ndi timakungu tija natipereka tonse kwa mfumu kuti akhale mpongozi wa mfumu. Kotero Sauli anapereka mwana wake wamkazi, Mikala, kwa Davide kuti amukwatire.

28 Sauli atazindikira kuti Yehova anali ndi Davide ndiponso kuti mwana wake Mikala amamukonda Davide, 29 iye anapitirirabe kumuopa Davide ndi kumadana naye moyo wake wonse.

30 Nthawi zonse pamene atsogoleri a Afilisti ankatuluka kukamenya nkhondo, Davide ankapambana kuposa nduna zonse za Sauli. Choncho dzina lake linatchuka kwambiri.

Aroma 16

Mawu Olawirana

16 Ine ndikupereka kwa inu mlongo wathu Febe, mtumiki wa mpingo wa ku Kenkreya. Ine ndikukupemphani kuti mumulandire mwa Ambuye mʼnjira yoyenera oyera mtima ndi kumupatsa thandizo lililonse limene akulifuna kuchokera kwa inu, pakuti iye wakhala thandizo lalikulu kwa anthu ambiri kuphatikiza ine.

Perekani moni kwa Prisila ndi Akura, atumiki anzanga mwa Khristu Yesu. Iwo anapereka miyoyo yawo chifukwa cha ine. Osati ine ndekha komanso mipingo yonse ya a mitundu ina ikuyamika.

Perekaninso moni kwa mpingo umene umasonkhana mʼnyumba mwawo.

Perekani moni kwa mʼbale wanga wokondedwa Epeneto, amene ndi woyamba kukhulupirira Khristu mʼchigawo cha Asiya.

Perekani moni kwa Mariya, amene wakhala akukugwirirani ntchito kwambiri.

Perekani moni kwa Androniko ndi Yuniya abale anga amene anali mʼndende pamodzi ndi ine. Iwo amadziwika ndi atumwi, ndipo iwo anali mwa Khristu ine ndisanakhale.

Perekani moni kwa Ampliato, amene ine ndimamukonda mwa Ambuye.

Perekani moni kwa Urbano, mtumiki mnzathu mwa Khristu ndi wokondedwa wanga Staku.

10 Perekani moni kwa Apele, woyesedwa ndi wovomerezeka mwa Khristu.

Perekani moni kwa a mʼbanja la Aristobulo.

11 Perekani moni kwa Herodiona, mʼbale wanga.

Perekani moni kwa a mʼbanja la Narkiso amene ali mwa Ambuye.

12 Perekani moni kwa Trufena ndi Trufosa, amayi aja amene amagwira ntchito ya Ambuye molimbika.

Perekani moni kwa mnzanga wokondedwa Persida, mayi winanso amene wagwira ntchito kwambiri mwa Ambuye.

13 Perekani moni kwa Rufo, wosankhidwa mwa Ambuye, ndi amayi ake, amene akhala amayi anganso.

14 Perekani moni kwa Asunkrito, Felego, Herima, Patroba, Herima ndi abale amene ali nawo pamodzi.

15 Perekani moni kwa Filologo, Yuliya, Neriya ndi mlongo wake, ndi Olumpa ndi oyera mtima onse amene ali nawo pamodzi.

16 Mupatsane moni wina ndi mnzake mwachikondi choona.

Mipingo yonse ya Khristu ikupereka moni.

17 Abale, ine ndikukupemphani kuti musamale chifukwa cha amene ayambitsa mipatuko ndi kuyika zokhumudwitsa panjira yanu, motsutsana ndi chiphunzitso chimene mwachiphunzira. Muwapewe iwo. 18 Pakuti otero sakutumikira Ambuye athu Khristu koma zilakolako zawo. Ndi mawu okoma ndi oshashalika iwo amanamiza anthu osalakwa. 19 Aliyense anamva za kumvera kwanu, choncho ndine odzaza ndi chimwemwe chifukwa cha inu. Koma ine ndikufuna kuti inu mukhale anzeru pa zabwino, ndi wopanda cholakwa pa zimene zili zoyipa.

20 Mulungu wamtendere adzaphwanya Satana msanga pansi pa mapazi anu.

Chisomo cha Ambuye athu Yesu chikhale ndi inu.

21 Timoteyo, mtumiki mnzanga, akupereka moni. Nawonso, Lusio, Yasoni ndi Sosipatro, abale anga akutero.

22 Ine Tertio, amene ndalemba kalatayi, ndi kupereka moni mwa Ambuye.

23 Gayo, amene chifukwa cha chisamaliro chake, ine ndi mpingo wonse kuno tikusangalala, akupereka moni.

Erasto, amene ndi msungichuma wa mzinda wonse ndiponso mʼbale wathu Kwato, akupereka moni.

24 Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale ndi inu nonse. Ameni.

25 Tsopano kwa Iye amene ali ndi mphamvu yokhazikitsa monga mwa uthenga wanga wabwino ndikulalikidwa kwa Yesu Khristu, monga mwa vumbulutso lachinsinsi chobisika kwa nthawi yayitali, 26 koma tsopano chavumbulutsidwa ndi kudziwika kudzera mʼMalemba a uneneri mwa lamulo la Mulungu wosatha, kuti mitundu yonse ikhulupirire ndi kumvera Iye, 27 kwa Mulungu yekhayo wanzeru kukhale ulemerero kwamuyaya kudzera mwa Yesu Khristu! Ameni.

Maliro 3

Ine ndine munthu amene ndaona masautso
    ndi ndodo ya ukali wake.
Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa
    mu mdima osati mʼkuwala;
zoonadi anandikantha ndi dzanja lake
    mobwerezabwereza tsiku lonse.

Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga,
    ndipo waphwanya mafupa anga.
Wandizinga ndi kundizungulira
    ndi zowawa ndi zolemetsa.
Wandikhazika mu mdima
    ngati amene anafa kale.

Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe,
    wandimanga ndi maunyolo.
Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo,
    amakana pemphero langa.
Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema;
    ndipo wakhotetsa tinjira tanga.

10 Wandidikirira ngati chimbalangondo,
    wandibisalira ngati mkango.
11 Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba,
    ndipo wandisiya wopanda thandizo.
12 Wakoka uta wake
    ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.

13 Walasa mtima wanga
    ndi mivi ya mʼphodo mwake.
14 Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse;
    amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
15 Wandidyetsa zowawa
    ndipo wandimwetsa ndulu.

16 Wathyola mano anga ndi miyala;
    wandiviviniza mʼfumbi;
17 Wandichotsera mtendere;
    ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
18 Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka
    ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”

19 Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala,
    zili ngati zowawa ndi ndulu.
20 Ine ndikuzikumbukira bwino izi,
    ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
21 Komabe ndimakumbukira zimenezi,
    nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.

22 Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu,
    ndi chifundo chake ndi chosatha.
23 Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse;
    kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
24 Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse;
    motero ndimamuyembekezera.”

25 Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye,
    kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
26 nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha
    Yehova modekha.
27 Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli
    pamene ali wamngʼono.

28 Akhale chete pa yekha,
    chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
29 Abise nkhope yake mʼfumbi
    mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
30 Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye,
    ndipo amuchititse manyazi.

31 Chifukwa Ambuye satayiratu
    anthu nthawi zonse.
32 Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo,
    chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
33 Pakuti sabweretsa masautso mwadala,
    kapena zowawa kwa ana a anthu.

34 Kuphwanya ndi phazi
    a mʼndende onse a mʼdziko,
35 kukaniza munthu ufulu wake
    pamaso pa Wammwambamwamba,
36 kumana munthu chiweruzo cholungama—
    kodi Ambuye saona zonsezi?

37 Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika
    ngati Ambuye sanavomereze?
38 Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka
    mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
39 Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula
    akalangidwa chifukwa cha machimo ake?

40 Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu,
    ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
41 Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu
    kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
42 “Ife tachimwa ndi kuwukira
    ndipo inu simunakhululuke.

43 “Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo
    mwatitha mopanda chifundo.
44 Mwadzikuta mu mtambo
    kotero mapemphero athu sakukufikani.
45 Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala
    pakati pa mitundu ya anthu.

46 “Adani anthu atitsekulira pakamwa.
47 Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje,
    tapasuka ndi kuwonongedwa.”
48 Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe
    chifukwa anthu anga akuwonongedwa.

49 Misozi idzatsika kosalekeza,
    ndipo sidzasiya,
50 mpaka Yehova ayangʼane pansi
    kuchokera kumwamba ndi kuona.
51 Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi
    chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.

52 Akundisaka ngati mbalame,
    amene anali adani anga, popanda chifukwa.
53 Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje
    ndi kundiponya miyala;
54 madzi anamiza mutu wanga
    ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.

55 Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova,
    kuchokera mʼdzenje lozama.
56 Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere
    kulira kwanga kopempha thandizo.”
57 Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani,
    ndipo munati, “Usaope.”

58 Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga;
    munapulumutsa moyo wanga.
59 Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira.
    Mundiweruzire ndinu!
60 Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo,
    chiwembu chawo chonse pa ine.

61 Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo,
    chiwembu chawo chonse pa ine,
62 manongʼonongʼo a adani anga
    ondiwukira ine tsiku lonse.
63 Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira,
    akundinyoza mu nyimbo zawo.

64 Inu Yehova, muwabwezere chowayenera,
    chifukwa cha zimene manja awo achita.
65 Phimbani mitima yawo,
    ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
66 Muwalondole mwaukali ndipo
    muwawonongeretu pa dziko lapansi.

Masalimo 34

Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka.

34 Ndidzayamika Yehova nthawi zonse;
    matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
Moyo wanga udzanyadira Yehova;
    anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine;
    tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.

Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha;
    anandilanditsa ku mantha anga onse.
Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira;
    nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva;
    Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye
    ndi kuwalanditsa.

Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino;
    wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
Wopani Yehova inu oyera mtima ake,
    pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
10 Mikango itha kulefuka ndi kumva njala
    koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.

11 Bwerani ana anga, mundimvere;
    ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
12 Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake
    ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
13 asunge lilime lake ku zoyipa
    ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
14 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino;
    funafuna mtendere ndi kuwulondola.

15 Maso a Yehova ali pa olungama
    ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
16 nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa,
    kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.

17 Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva;
    Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
18 Yehova ali pafupi kwa osweka mtima
    ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.

19 Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri,
    Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
20 Iye amateteza mafupa ake onse,
    palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.

21 Choyipa chidzapha anthu oyipa;
    adani a olungama adzapezeka olakwa.
22 Yehova amawombola atumiki ake;
    aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.