Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

M’Cheyne Bible Reading Plan

The classic M'Cheyne plan--read the Old Testament, New Testament, and Psalms or Gospels every day.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Yoswa 3

Aisraeli Awoloka Yorodani

Yoswa ndi Aisraeli onse anadzuka mmamawa nanyamuka ku Sitimu kupita ku Yorodani. Iwo anagona kumeneko asanawoloke mtsinje wa Yorodaniwo. Patatha masiku atatu, atsogoleri anayendera misasa yonse, kulangiza anthu kuti, “Mukaona ansembe a Chilevi atanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu, inu munyamuke pa malo ano ndi kumalitsatira. Potero mudzadziwa njira yoti mudzere, popeza simunayendepo njira ino nʼkale lomwe. Koma musaliyandikire. Pakati pa inu ndi bokosilo pakhale mtunda pafupifupi kilomita imodzi.”

Yoswa anawuza anthu kuti, “Dzipatuleni tsono pakuti mawa Yehova adzachita zodabwitsa pakati panu.”

Mmawa mwake Yoswa ananena kwa ansembe kuti, “Nyamulani Bokosi la Chipangano muwoloke ndipo mukhale patsogolo pa anthu.” Motero iwo analinyamula ndi kupita patsogolo pawo.

Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, “Lero Ine ndidzayamba kukukweza pamaso pa Aisraeli onse kuti adziwe kuti ndili nawe monga ndinalili ndi Mose. Ansembe amene akunyamula Bokosi la Chipangano uwalamule kuti, ‘Mukafika ku mtsinje wa Yorodani mulowe mu mtsinjemo ndi kuyima mʼmphepete.’ ”

Yoswa anati kwa Aisraeli, “Bwerani pano mudzamve mawu a Yehova Mulungu wanu. 10 Umu ndi mmene mudzadziwira kuti Mulungu wamoyo ali pakati panu. Inu mukamadzapita patsogolo Iye adzathamangitsa Akanaani, Ahiti, Ahivi, Aperezi, Agirigasi, Aamori ndi Ayebusi. 11 Pamenepo, Bokosi la Chipangano la Mbuye wa dziko lonse lapansi lidzawoloka mu Yorodani patsogolo panu. 12 Musankhe amuna khumi ndi awiri kuchokera ku fuko lililonse la Israeli. 13 Mapazi a ansembe onyamula Bokosi la Yehova, Mbuye wa dziko lapansi, akadzangoponda mu Yorodani, madzi ake onse ochokera ku mtunda adzaleka kuyenda ndipo adzayima ngati chipupa.”

14 Tsono Aisraeli anachoka ku misasa yawo kukawoloka mtsinje wa Yorodani. Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano ndiwo anatsogolera anthuwo. 15 Nyengo imeneyi inali yokolola ndipo mtsinje wa Yorodani umakhala wodzaza. Komabe, ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anafika ku Yorodani, ndipo atangoponda mʼmadzimo, 16 madzi ochokera ku mtunda anasiya kuyenda. Madzi a Yorodani ochokera ku mtunda anawunjikana pamodzi ngati khoma lalitali pa mtunda wautali ndithu ndi mzinda wa Adama chapafupi ndi mzinda wa Zaretani. Madzi othamangira ku nyanja ya Araba, ngakhalenso amene amachokera kuti Nyanja ya Mchere amathera pamenepo. Choncho anthu anawoloka tsidya lina moyangʼanana ndi Yeriko. 17 Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova anali chiyimire powuma, pakati pa Yorodani pamene Aisraeli amawoloka mpaka gulu lonse linamaliza kuwoloka powuma.

Masalimo 126-128

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

126 Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni,
    tinali ngati amene akulota.
Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka;
    malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe.
Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti,
    “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
Yehova watichitira zinthu zazikulu,
    ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.

Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova,
    monga mitsinje ya ku Negevi.
Iwo amene amafesa akulira,
    adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
Iye amene amayendayenda nalira,
    atanyamula mbewu yokafesa,
adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe,
    atanyamula mitolo yake.

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Solomoni.

127 Yehova akapanda kumanga nyumba,
    omanga nyumbayo agwira ntchito pachabe.
Yehova akapanda kulondera mzinda,
    mlonda akanangolondera pachabe.
Mumangodzivuta nʼkulawirira mmamawa
    ndi kusagona msanga madzulo,
kuvutikira chakudya choti mudye,
    pakuti Iye amapereka tulo kwa amene amawakonda.

Ana ndiye cholowa chochokera kwa Yehova,
    ana ndi mphotho yochokera kwa Iye.
Ana a pa unyamata ali ngati mivi mʼmanja
    mwa munthu wankhondo.
Wodala munthu
    amene motengera mivi mwake mwadzaza.
Iwo sadzachititsidwa manyazi
    pamene alimbana ndi adani awo pa zipata.

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

128 Odala ndi onse amene amaopa Yehova,
    amene amayenda mʼnjira zake.
Udzadya chipatso cha ntchito yako;
    madalitso ndi chuma zidzakhala zako.
Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka
    mʼkati mwa nyumba yako;
ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi
    kuzungulira tebulo lako.
Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa
    amene amaopa Yehova.

Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni
    masiku onse a moyo wako;
uwone zokoma za Yerusalemu,
    ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako.

Mtendere ukhale ndi Israeli.

Yesaya 63

Yehova Agonjetsa Anthu a Mitundu Ina

63 Kodi ndani uyo akubwera kuchokera ku Edomu,
    atavala zovala za ku Bozira za madontho ofiira?
Kodi uyu ndani, amene wavala zovala zokongola,
    akuyenda mwa mphamvu zake?

“Ndi Ineyo, woyankhula zachilungamo
    ndiponso wamphamvu zopulumutsa.”

Nanga bwanji zovala zanu zili psuu,
    ngati za munthu wofinya mphesa?

“Ndapondereza ndekha anthu a mitundu ina ngati mphesa,
    palibe ndi mmodzi yemwe anali nane.
Ndinawapondereza ndili wokwiya
    ndipo ndinawapondereza ndili ndi ukali;
magazi awo anadothera pa zovala zanga,
    ndipo zovala zanga zonse zinathimbirira.
Pakuti ndinatsimikiza mu mtima mwanga kuti lafika tsiku lolipsira anthu anga;
    ndipo chaka cha kuwomboledwa kwanga chafika.
Ndinayangʼana ndipo panalibe munthu wondithandiza.
    Ndinadabwa kwambiri kuti panalibe wondichirikiza;
choncho ndinapambana ndi mphamvu zanga,
    ndipo mkwiyo wanga unandilimbitsa.
Ndinapondereza mitundu ya anthu ndili wokwiya;
    ndipo ndinawasakaza
    ndipo ndinathira magazi awo pansi.”

Matamando ndi Pemphero

Ndidzafotokoza za kukoma mtima kwa Yehova,
    ntchito zimene Iye ayenera kutamandidwa.
    Ndidzatamanda Yehova chifukwa cha zonse zimene watichitira.
Inde, mwa chifundo ndi kukoma mtima kwake
    Yehova wachitira nyumba ya Israeli
    zinthu zabwino zambiri.
Yehova anati, “Ndithu awa ndi anthu anga,
    ana anga amene sadzandinyenga Ine.”
    Choncho anawapulumutsa.
Iyenso anasautsidwa mʼmasautso awo onse,
    ndipo mngelo wochokera kwa Iye anawapulumutsa.
Mwa chikondi ndi chifundo chake iye anawapulumutsa,
    anawanyamula ndikuwatenga
    kuyambira kale lomwe.
10 Komabe iwo anawukira
    ndi kumvetsa chisoni Mzimu Woyera.
Motero Yehova anatembenuka nakhala mdani wawo
    ndipo Iye mwini anamenyana nawo.

11 Pamenepo anthu ake anakumbukira masiku amakedzana,
    masiku a Mose mtumiki wake;
ndipo anafunsa kuti, “Ali kuti Yehova amene anawawolotsa pa nyanja,
    pamodzi ndi Mose mʼbusa wawo?
Ali kuti Iye amene anayika
    Mzimu Woyera pakati pawo?
12 Ali kuti amene anachita zinthu zodabwitsa
    ndi mphamvu zake zazikulu kudzera mwa Mose?
Ali kuti amene anagawa madzi pa nyanja anthu ake akuona,
    kuti dzina lake limveke mpaka muyaya,
13 amene anawayendetsa pa nyanja yozama?
Monga kavalo woyendayenda mʼchipululu,
    iwo sanapunthwe;
14 Mzimu Woyera unawapumulitsa
    ngati mmene ngʼombe zimapumulira.
Umu ndi mmene Inu munatsogolera anthu anu
    kuti dzina lanu lilemekezeke.”

15 Inu Yehova amene muli kumwambako, pa mpando wanu wolemekezeka,
    wopatulika ndi waulemerero, tiyangʼaneni ife.
Kodi changu chanu ndi mphamvu zanu zili kuti?
    Simukutionetsanso kukoma mtima kwanu ndi chifundo chanu.
16 Koma Inu ndinu Atate athu,
    ngakhale Abrahamu satidziwa
    kapena Israeli kutivomereza ife;
Inu Yehova, ndinu Atate athu,
    kuyambira kale dzina lanu ndinu Mpulumutsi wathu.
17 Chifukwa chiyani, Inu Yehova, mukutisocheretsa pa njira zanu?
    Bwanji mukutilola kuti tikhale owuma mitima kotero kuti sitikukuopaninso?
Bwererani chifukwa cha atumiki anu;
    mafuko a anthu amene ali cholowa chanu.
18 Anthu anu atangokhala pa malo anu opatulika pa kanthawi kochepa,
    adani athu anasakaza malo anu opatulika.
19 Ife tili ngati anthu amene
    simunawalamulirepo
    ngati iwo amene sanakhalepo anthu anu.

Mateyu 11

Otumidwa ndi Yohane Mʼbatizi

11 Ndipo Yesu atamaliza kulangiza ophunzira ake khumi ndi awiri aja, anachoka kumeneko kupita kukaphunzitsa ndi kukalalikira ku mizinda ya ku Galileya.

Yohane ali mʼndende anamva zimene Khristu ankachita, ndipo anatumiza ophunzira ake kukamufunsa Iye. Anamufunsa kuti, “Kodi Inu ndinu uja ankanena kuti mudzabwerayu kapena tidikire wina?”

Yesu anayankha kuti, “Bwererani ndi kukamuwuza Yohane zimene mwamva ndi kuona. Osaona akuona, olumala akuyenda, akhate akuchiritsidwa, osamva akumva, akufa akuukitsidwa ndipo Uthenga Wabwino ukulalikidwa kwa osauka. Odala ndi munthu amene sakhumudwa chifukwa cha Ine.”

Pamene ophunzira a Yohane ankachoka, Yesu anayamba kuyankhula kwa gulu la anthu za Yohane kuti, “Kodi munkapita ku chipululu kuti mukaone chiyani? Kodi bango logwedezeka ndi mphepo? Nanga munkapita kukaona chiyani, munthu wovala zokongola? Ayi, wovala zokongola amakhala mʼnyumba za mafumu. Nanga munkapita kukaona chiyani? Mneneri kodi? Inde ndikuwuzani kuti munkakaona woposa mneneri. 10 Uyu ndi amene malemba akunena za iye kuti,

“Ine ndidzatuma mthenga wanga patsogolo panu
    amene adzakonza njira yanu.

11 Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti pakati pa obadwa ndi mkazi sipanaoneke wina aliyense wamkulu woposa Yohane Mʼbatizi; komatu amene ndi wamngʼono kwambiri mu ufumu wakumwamba ndi wamkulu koposa iye. 12 Kuyambira masiku a Yohane Mʼbatizi mpaka tsopano, ufumu wakumwamba ndi wolimbirana ndipo anthu amphamvu okha ndi amene akuwulanda. 13 Pakuti aneneri onse ndi malamulo ananenera kufikira nthawi ya Yohane. 14 Ndipo ngati inu mufuna kulandira izi, iyeyu ndi Eliya amene ankanena kuti adzabwera uja. 15 Iye amene ali ndi makutu amve.

16 “Kodi mʼbado uwu ndingawufanizire ndi chiyani? Uli ngati ana opezeka mʼmisika amene akuyitana anzawo nʼkumati:

17 “ ‘Tinakuyimbirani zitoliro,
    koma inu simunavine;
ife tinayimba nyimbo zamaliro,
    koma inu simunalire.’

18 Pakuti Yohane sanabwerere kudya kapena kumwa koma iwo ankanena kuti, ‘Iye anali ndi chiwanda.’ 19 Mwana wa Munthu anabwera ndi kumadya ndi kumwa koma iwo akuti, ‘Munthu wadyera, woledzera, bwenzi la amisonkho ndi bwenzi la ochimwa.’ Koma nzeru imatsimikizika kuti ndi yolondola mwa ntchito zake.”

Tsoka la Mizinda Itatu Yosatembenuka mtima

20 Pamenepo Yesu anayamba kudzudzula mizinda imene zodabwitsa zake zambiri zinachitikamo, chifukwa chakuti sinatembenuke mtima. 21 “Tsoka kwa iwe Korazini! Tsoka kwa iwe Betisaida! Ngati zodabwitsa zimene zinachitika mwa iwe zikanachitidwa mu Turo ndi Sidoni, iwo akanalapa kale atavala ziguduli ndi kudzola phulusa. 22 Koma ndikuwuzani inu kuti pa tsiku lachiweruzo mlandu wa Turo ndi Sidoni udzachepako kusiyana ndi wanu. 23 Ndipo iwe Kaperenawo, kodi udzakwezedwa kufika kumwamba? Ayi, udzatsitsidwa mpaka pansi kufika ku Hade. Ngati zodabwitsa zimene zinachitika mwa iwe, zikanachitika mu Sodomu, bwenzi iye alipo kufikira lero. 24 Koma Ine ndikuwuzani kuti pa tsiku la chiweruziro mlandu wa Sodomu udzachepako kusiyana ndi wanu.”

Goli la Khristu

25 Pa nthawi imeneyo Yesu anati, “Ine ndikukuyamikani Inu Atate Ambuye akumwamba ndi dziko lapansi, chifukwa Inu mwawabisira zinthu izi anzeru ndi ophunzira ndi kuziwulula kwa ana angʼonoangʼono. 26 Inde, Atate, ichi chinali chokukomerani Inu.

27 “Zinthu zonse zapatsidwa kwa Ine ndi Atate anga. Palibe mmodzi amene adziwa Mwana kupatula Atate ndipo palibe mmodzi amene adziwa Atate kupatula Mwana ndi kwa iwo amene Mwana awasankha kuwawululira.

28 “Idzani kwa Ine, inu nonse otopa ndi olemedwa ndipo Ine ndidzakupatsani mpumulo. 29 Senzani goli langa ndipo phunzirani kwa Ine, pakuti ndine wofatsa ndi wodzichepetsa. Ndipo inu mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu. 30 Pakuti goli langa ndi losavuta ndipo katundu wanga ndi wopepuka.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.