M’Cheyne Bible Reading Plan
Samueli Adzudzula Sauli
13 Sauli analowa ufumu ali ndi zaka makumi atatu, ndipo analamulira Israeli kwa zaka 42.
2 Nthawi ina Sauli anasankha Aisraeli 3,000. Mwa iwowa, 2,000 anali ndi Sauliyo ku Mikimasi ndi ku dziko la mapiri ku Beteli, ndipo 1,000 anali ndi Yonatani ku Gibeya ku Benjamini. Anthu ena onse otsala anawabweza kwawo.
3 Yonatani anakantha mkulu wa ankhondo wa Afilisti ku Geba, ndipo Afilisti anamva kuti Aheberi awukira. Tsono Sauli anawuza amithenga kuti alize lipenga mʼdziko lonse la Israeli. 4 Choncho Aisraeli onse anamva kuti Sauli wakantha mkulu wa ankhondo Wachifilisiti ndi kuti Afilisti anayipidwa nawo Aisraeli. Ndiye anthu anayitanidwa kuti abwere kwa Sauli ku Giligala.
5 Tsono Afilisti anasonkhana kuti amenyane ndi Aisraeli. Iwo anali ndi magaleta 3,000, okwera pa akavalo 2,000 ndiponso asilikali kuchuluka kwake ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja. Iwo anapita ndi kukamanga misasa yawo ku Mikimasi, kummawa kwa Beti-Aveni. 6 Pamene Aisraeli anaona kuti anali pamavuto akulu, poti anali atapanikizidwa kwambiri, anabisala mʼmapanga, mʼmaenje, mʼmatanthwe, mʼmakwalala ndi mʼzitsime. 7 Ahebri ena anawoloka Yorodani mpaka kukafika ku dziko la Gadi ndi ku Giliyadi.
Koma Sauli anakhalabe ku Giligala ndipo ankhondo onse amene anali naye anali njenjenje ndi mantha. 8 Saulo anadikirira masiku asanu ndi awiri, monga mwa nthawi imene ananena Samueli. Koma Samueli sanabwere ku Giligala, ndipo anthu anayamba kumuthawa Sauli uja. 9 Kotero iye anati, “Bwera nayoni nsembe yopsereza ndi nsembe ya chiyanjano.” Ndipo Sauli anapereka nsembe yopsereza. 10 Atangomaliza kupereka nsembe, anangoona Samueli watulukira ndipo Sauli anapita kukamulonjera.
11 Samueli anafunsa kuti, “Nʼchiyani chimene wachita?”
Sauli anayankha kuti, “Nditaona kuti anthu ayamba kundithawa, ndi kuti inu simunabwere pa nthawi munanena ija, ndiponso kuti Afilisti akusonkhana ku Mikimasi, 12 ndinati, ‘Tsopano Afilisti abwera kudzandithira nkhondo ku Giligala kuno, chonsecho sindinapemphe Yehova kuti andikomere mtima.’ Motero ndinakakamizika kupereka nsembe yopsereza.”
13 Samueli anati, “Mwachita zopusa. Simunatsate zimene Yehova Mulungu wanu anakulamulani kuti muchite. Mukanazitsata, Yehova akanawukhazikitsa ufumu wanu mu Israeli mpaka kalekale. 14 Koma tsopano ufumu wanu sudzakhalitsa. Yehova wapeza munthu wapamtima pake ndipo wamusankha kukhala mtsogoleri wa anthu ake chifukwa inu simunasunge malamulo a Yehova.”
15 Kenaka Samueli anachoka ku Giligala ndi kupita ku Gibeyati ku dziko la Benjamini. Saulo anawerenga anthu amene anali naye ndipo analipo 600.
Sauli Akonzekera Nkhondo
16 Sauli ndi mwana wake Yonatani pamodzi ndi asilikali amene anali naye aja amakhala ku Geba ku dziko la Benjamini. Koma Afilisti anamanga misasa yawo ku Mikimasi. 17 Ankhondo a Afilisti anatuluka mʼmisasa yawo mʼmagulu atatu. Gulu lina linapita ku Ofiri ku dziko la Suwala. 18 Gulu lina linalunjika ku Beti-Horoni, ndipo gulu lachitatu linalunjika ku malire oyangʼanana ndi chigwa cha Zeboimu cha ku chipululu.
19 Nthawi imeneyo nʼkuti mulibe osula zitsulo mʼdziko lonse la Israeli, pakuti Afilisti anati, “Tisawalole Aheberi kudzipangira okha malupanga kapena mikondo!” 20 Kotero Aisraeli onse amapita kwa Afilisti kukanoletsa mapulawo, makasu, nkhwangwa ndi zikwakwa zawo. 21 Mtengo wonolera mapulawo ndi makasu unali zigawo ziwiri za sekeli, mtengo wonolera zisonga ndi nkhwangwa unali gawo limodzi la Sekeli.
22 Motero tsiku la nkhondolo panalibe lupanga kapena mkondo mʼdzanja la aliyense amene anatsatira Saulo ndi Yonatani. Koma Saulo ndi Yonatani, iwo okha ndiwo anali ndi zida.
Yonatani Athira Nkhondo Afilisti
23 Tsono gulu lina lankhondo la Chifilisti linapita kukalonda mpata wa Mikimasi.
Aisraeli Otsala
11 Ine ndikufunsa kuti kodi Mulungu anakana anthu ake? Ayi. Ndi pangʼono pomwe! Inenso ndine Mwisraeli, mmodzi mwa zidzukulu za Abrahamu, ndiponso wa fuko la Benjamini. 2 Mulungu sanawakane anthu ake amene Iye anawadziwiratu. Kodi inu simukudziwa zimene Malemba akunena pa ndime imene Eliya akudandaula kwa Mulungu kuneneza Aisraeli? Iye anati, 3 “Ambuye, anthuwa apha aneneri anu ndi kugwetsa maguwa anu ansembe. Ndatsala ine ndekha wamoyo ndipo akufuna kundipha?” 4 Ndipo yankho la Mulungu linali lotani? “Ine ndadzisungira ndekha anthu 7,000 amene sanapembedzepo Baala.” 5 Chimodzimodzinso lero lino, alipo Aisraeli pangʼono osankhidwa mwachisomo. 6 Ndipo ngati ndi mwachisomo, sikungakhalenso mwa ntchito. Ngati zikanatero, chisomo sichikanakhalanso chisomo ayi.
7 Nʼchiyani tsopano? Chimene Aisraeli anachifuna ndi mtima wonse sanachipeze koma osankhidwawo anachipeza. Enawo anawumitsidwa mtima 8 monga kwalembedwa kuti,
“Mulungu anawapatsa mzimu wosatha kumvetsa zinthu,
maso osatha kupenya;
makutu osatha kumva
mpaka lero lino.”
9 Ndipo Davide akuti,
“Maphwando awo asanduke msampha ndi diwa lowakola
ndi chopunthwitsa kuti alandire chilango.
10 Maso awo atsekedwe kuti asaone,
ndi misana yawo ikhale yokhota nthawi zonse.”
Nthambi Zomangiriridwa
11 Ine ndikufunsanso kuti, kodi iwo anapunthwa ndi kugwa kotheratu? Ayi. Ndi pangʼono pomwe! Koma chifukwa cha kulakwa kwawo, chipulumutso chinafika kwa a mitundu ina kuti Aisraeli achite nsanje. 12 Koma ngati kulakwa kwawo kwapindulitsa dziko lapansi ndi kulephera kwawo kwapindulitsa a mitundu ina, nanga kudzakhala kupindula kwakukulu chotani iwo akadzabwera chonse!
13 Ine ndikuyankhula kwa inu a mitundu ina monga ine ndili mtumwi wa kwa a mitundu ina ndipo ndimawunyadira utumiki wangawu. 14 Ine cholinga changa nʼchakuti ndichititse nsanje anthu a mtundu wanga kuti ena mwa iwo apulumutsidwe. 15 Pakuti ngati kukanidwa kwawo kunayanjanitsa anthu a dziko lapansi ndi Mulungu, nanga kudzatani, Iye akadzawalandiranso? Kudzakhala monga ngati anthu akufa akuuka. 16 Ngati chigawo chimodzi cha buledi woperekedwa monga zipatso zoyamba ndi choyera, ndiye kuti zonsezo ndi zoyera. Ngati muzu ndi oyera, nʼchimodzimodzinso nthambi zake.
17 Ngati nthambi zina zinakhadzulidwa ndipo inu, inu ndiye nthambi za olivi wakuthengo, nʼkulumikizidwa pamalo pa nthambi zimenezo, ndipo tsopano mukulandira nawo zakudya zochokera ku mizu ya olivi, 18 musadzitame kunyoza nthambi zinazo. Ngati mutero, ganizirani ichi kuti Inu simugwiriziza mizu, koma muzu ukugwiriziza inu. 19 Tsono mudzati, “Nthambizo zinakhadzulidwa kuti ine ndilumikizidwepo.” 20 Nʼzoona. Koma iwo anakhadzulidwa chifukwa chosakhulupirira ndipo inu mukuyima mwachikhulupiriro. Musadzitukumule, koma muchite mantha. 21 Pakuti ngati Mulungu sanalekerere nthambi zachibadwidwe, Iye sadzakulekererani inunso.
22 Nʼchifukwa chake ganizirani za kukoma mtima ndi za ukali wa Mulungu. Ukali uli kwa iwo amene anagwa koma kukoma mtima kwa inu, malinga ngati musamala kukoma mtima kwakeko kupanda kutero inunso mudzakhadzulidwanso. 23 Ngati iwo asiya kukhala osakhulupirira, adzalumikizidwanso pakuti Mulungu akhoza kuwalumikizanso. 24 Pakuti ngati inu, mwa chilengedwe munali mtengo wa olivi wa kuthengo, Mulungu anakukhadzulani nakulumikizani ku mtengo wa olivi wodzalidwa, zomwe ndi zotsutsana ndi chilengedwe, kodi sikudzakhala kwapafupi kwa Iye kuwalumikizanso mu mtengo wawowawo wa olivi?
Aisraeli Onse Adzapulumuka
25 Abale, ine sindifuna kuti mukhale osadziwa za chinsinsi ichi, kuti mungadziyese nokha anzeru. Kuwuma mtima kumene Aisraeli akuchita ndi kwa kanthawi kufikira chiwerengero cha a mitundu chitalowa. 26 Kotero tsono Aisraeli onse adzapulumuka, monga kwalembedwa kuti,
“Mpulumutsi adzachokera ku Ziyoni;
Iye adzachotsa zoyipa zonse za Yakobo.
27 Ndipo ili lidzakhala pangano langa ndi iwo
pamene Ine ndidzachotsa machimo awo.”
28 Chifukwa cha Uthenga Wabwino, Aisraeli asanduka adani a Mulungu kuti inu mupindule. Koma kunena za kusankhidwa, iwo ndi okondedwa ndi Mulungu chifukwa cha makolo awo aja. 29 Pakuti Mulungu akayitana munthu ndi kumupatsa mphatso sangasinthenso. 30 Monga mmene inu munalili, osamvera Mulungu pa nthawi ina, tsopano mwalandira chifundo chifukwa cha kusamvera kwawo. 31 Chonchonso iwo akhala osamvera tsopano kuti iwonso alandire chifundo chifukwa cha chifundo cha Mulungu kwa inu. 32 Pakuti Mulungu anasandutsa anthu onse a mʼndende ya kusamvera kuti Iye akaonetse chifundo kwa onse.
Kulemekeza Mulungu
33 Aa! Nzeru za Mulungu ndi chidziwitso chake ndi zozama kwambiri!
Ndani angazindikire maweruzidwe ake,
ndipo njira zake angazitulukire ndani?
34 “Kodi wadziwa ndani maganizo a Ambuye?
Kapena ndani anakhalapo mlangizi wake?”
35 “Kodi ndani anapereka mphatso kwa Mulungu,
kuti Mulunguyo amubwezere iye?”
36 Pakuti zinthu zonse nʼzochokera kwa Iye, nʼzolengedwa ndi Iye ndipo zimabweretsa ulemerero kwa Iye.
Kwa Iye kukhale ulemerero mpaka muyaya! Ameni.
Uthenga Wonena za Babuloni
50 Uthenga umene Yehova anayankhula ndi mneneri Yeremiya wonena za mzinda wa Babuloni ndi anthu ake ndi uwu:
2 “Lengeza ndi kulalika pakati pa anthu a mitundu ina,
kweza mbendera ndipo ulengeze;
usabise kanthu, koma uwawuze kuti,
‘Babuloni wagwa;
mulungu wawo Beli wachititsidwa manyazi,
nayenso Mariduku wagwidwa ndi mantha.
Milungu yake yagwidwa ndi mantha
ndipo mafano ake adzagwidwa ndi mantha.’
3 Mtundu wa anthu wochokera kumpoto wadzathira nkhondo Babuloni
ndi kusandutsa bwinja dziko lake.
Kumeneko sikudzakhalanso
munthu kapena nyama.
4 “Masiku amenewo, nthawi imeneyo,”
akutero Yehova,
“anthu a ku Israeli ndi anthu a ku Yuda
onse pamodzi adzabwera akulira. Adzafunitsitsa kuchita zimene Yehova Mulungu wawo akufuna.
5 Adzafunsa njira ya ku Ziyoni
ndi kuyamba ulendo wopita kumeneko.
Iwo adzadzipereka kwa Yehova
pochita naye pangano lamuyaya
limene silidzayiwalika.
6 “Anthu anga ali ngati nkhosa zotayika;
abusa awo
anawasocheretsa mʼmapiri.
Iwo anayendayenda mʼmapiri ndi mʼzitunda
mpaka kuyiwala kwawo.
7 Aliyense amene anawapeza anawawononga;
adani awo anati, ‘Ife si olakwa,
chifukwa iwo anachimwira Yehova, amene ali mpumulo wawo weniweni
ndi amene makolo awo anamukhulupirira.’
8 “Thawaniko ku Babuloni;
chokani mʼdziko la Ababuloni.
Muyambe inu kutuluka ngati atonde amene amatsogolera ziweto.
9 Taonani, ndidzaukitsa gulu lankhondo lamphamvu la mitundu ina
ndi kubwera nalo kuchokera kumpoto
kudzamenyana ndi Babuloni.
Iwo adzandandalika ankhondo awo ndi kugonjetsa Babuloni.
Mivi yawo ili ngati ya ankhondo aluso,
yosapita padera.
10 Motero Ababuloni adzafunkhidwa;
ndipo onse omufunkha adzakhuta,”
akutero Yehova.
11 “Inu Ababuloni, munawononga anthu anga osankhika.
Ndiye pano mukukondwa, mukusangalala.
Mukulumphalumpha mokondwa ngati mwana wangʼombe wopuntha tirigu
ndiponso mukulira monyada ngati ngʼombe zazimuna.
12 Koma mzinda wanu udzachititsidwa manyazi kwambiri.
Mzinda umene uli ngati mayi wanu udzanyazitsidwa.
Babuloni adzasanduka chitsirizira cha anthu onse.
Mzinda wawo udzakhala ngati thengo, ngati dziko lowuma lachipululu.
13 Chifukwa cha mkwiyo wa Yehova Babuloni adzakhala wopanda anthu
ndipo adzakhala chipululu chokhachokha.
Onse odutsa kumeneko adzachita mantha ndipo azidzangotsonya
chifukwa cha chiwonongeko chake chachikulu.
14 “Inu okoka uta,
konzekani kuti muthire nkhondo mzinda wa Babuloni mbali zonse.
Muponyereni mivi yanu yonse
chifukwa anachimwira Yehova.
15 Mufuwulireni mbali zonse pakuti wagonja.
Nsanja zake zagwa.
Malinga ake agwetsedwa.
Kumeneku ndiko kulipsira kwa Yehova.
Mulipsireni,
mumuchite zomwe iye anachitira anthu ena.
16 Chotsani ku Babuloni munthu wofesa mbewu aliyense,
ndiponso wodula tirigu ndi chikwakwa chake pa nthawi yokolola.
Poona lupanga la ozunza anzawo,
aliyense adzabwerera kwa anthu ake;
adzathawira ku dziko la kwawo.
17 “Aisraeli ali ngati nkhosa zomwe zabalalika
pothamangitsidwa ndi mikango.
Mfumu ya ku Asiriya ndiye inayamba kuwapha Aisraeliwo.
Wotsiriza anali Nebukadinezara
mfumu ya ku Babuloni
amene anachita ngati kuphwanya mafupa ake.”
18 Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti,
“Ndidzalanga mfumu ya ku Babuloni pamodzi ndi dziko lake
monga momwe ndinalangira mfumu ya ku Asiriya.
19 Koma ndidzabwezera Israeli ku msipu wake
ndipo adzadya mʼminda ya ku Karimeli ndi Basani;
adzadya nakhuta ku mapiri
a ku Efereimu ndi Giliyadi.
20 Masiku amenewo, nthawi imeneyo,”
akutero Yehova,
“anthu adzafunafuna zolakwa za Israeli
koma sadzapeza nʼchimodzi chomwe,
ndipo adzafufuza machimo a Yuda,
koma sadzapeza ndi limodzi lomwe,
chifukwa otsala amene ndawasiya ndidzawakhululukira.
21 “Lithireni nkhondo dziko la Merataimu
ndi anthu okhala ku Pekodi.
Muwaphe ndi lupanga ndi kuwawonongeratu,”
akutero Yehova.
“Chitani zonse monga momwe ndakulamulani.
22 Mʼdziko muli phokoso la nkhondo,
phokoso la chiwonongeko chachikulu!
23 Taonani mʼmene waphwanyikira ndi kuwonongekera
uja amati ndi nyundo ya dziko lonse lapansi.
Mzinda wa Babuloni wasanduka chinthu chochititsa mantha
pakati pa mitundu ina!
24 Ndinakutchera msampha, iwe Babuloni,
ndipo wakodwamo iwe wosazindikira kanthu;
unapezeka ndiponso unakodwa
chifukwa unalimbana ndi Yehova.
25 Yehova watsekula nyumba ya zida zake
ndipo watulutsa zida za ukali wake,
pakuti Ambuye Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ntchito yoti agwire
mʼdziko la Ababuloni.
26 Mumenyane naye Babuloni mbali zonse.
Anthu ake muwawunjike
ngati milu ya tirigu.
Muwawononge kotheratu
ndipo pasakhale wopulumuka ndi mmodzi yemwe.
27 Iphani ankhondo ake onse.
Onse aphedwe ndithu.
Tsoka lawagwera
pakuti tsiku lawo lachilango lafika.
28 Tikumva anthu othawa nkhondo ochokera ku Babuloni
akulengeza mu Yerusalemu
za kulipsira kwa Yehova Mulungu wathu.
Iye akulipsira chifukwa chowononga Nyumba yake.
29 “Itanani anthu oponya mivi kudzathira nkhondo Babuloni.
Muyitanenso onse amene amakoka mauta.
Mangani misasa ya nkhondo momuzungulira;
musalole munthu aliyense kuthawa.
Muchiteni monga momwe
iye anachitira anthu ena.
Iyeyu ananyoza
Yehova, Woyera wa Israeli.
30 Nʼchifukwa chake, anyamata ake adzaphedwa mʼmabwalo ake;
ankhondo ake onse adzaphedwa tsiku limenelo,”
akutero Yehova.
31 “Taona, ndikukuthira nkhondo, iwe wodzikuzawe,”
akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse,
“chifukwa tsiku lako lafika,
nthawi yoti ndikulange yakwana.
32 Wodzikuzawe udzapunthwa nʼkugwa
ndipo palibe amene adzakudzutse;
ndidzayatsa moto mʼmizinda yake
umene udzanyeketsa onse amene amuzungulira.”
33 Yehova Wamphamvuzonse akuti,
“Anthu a ku Israeli akuzunzidwa,
pamodzi ndi anthu a ku Yuda,
ndipo onse amene anawagwira ukapolo awagwiritsitsa,
akukana kuwamasula.
34 Koma Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu;
dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Iye adzawateteza molimba pa mlandu wawo
nʼcholinga choti abweretse mtendere mʼdziko lawo,
koma adzavutitsa okhala ku Babuloni.”
35 Yehova akuti,
“Imfa yalunjika pa Ababuloni,
pa akuluakulu ake
ndi pa anthu ake a nzeru!
36 Imfa yalunjika pa aneneri abodza
kuti asanduke zitsiru.
Imfa yalunjika pa ankhondo ake
kuti agwidwe ndi mantha aakulu.
37 Imfa ilunjike pa akavalo ake ndi magaleta ake.
Ilunjikanso pa magulu ankhondo achilendo amene ali pakati pawo
kuti asanduke ngati akazi.
Chiwonongeko chilunjikenso pa chuma chake
kuti chidzafunkhidwe.
38 Chilala chilunjike pa madzi ake
kuti aphwe.
Babuloni ndi dziko la mafano,
ndipo anthu afika poyaluka nawo mafanowo.
39 “Nʼchifukwa chake nyama zakuthengo ndi afisi zidzakhala kumeneko
ndipo kudzakhalanso akadzidzi.
Kumeneko sikudzapezekako anthu,
ndithu anthu sadzakhalako pa mibado yonse.
40 Monga momwe Mulungu anawonongera Sodomu ndi Gomora
pamodzi ndi mizinda yonse yozungulira,”
akutero Yehova,
“momwemonso palibe amene adzakhale kumeneko;
anthu sadzayendanso mʼmenemo.
41 “Taonani! Gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto;
mtundu wa anthu amphamvu pamodzi ndi mafumu ambiri,
wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
42 Atenga mauta ndi mikondo;
ndi anthu ankhanza ndipo alibe chifundo.
Phokoso lawo likumveka ngati mkokomo wa nyanja.
Akwera pa akavalo awo,
ndipo akonzekera kudzakuthira nkhondo
iwe Babuloni.
43 Mfumu ya ku Babuloni yamva za mbiri yawo,
ndipo yalobodokeratu.
Ikuda nkhawa,
ikumva ululu ngati wa mayi pa nthawi yake yochira.
44 Taonani, monga mkango wochokera ku nkhalango ya ku Yorodani
kupita ku msipu wobiriwira,
momwemonso ine ndidzapirikitsa Babuloni mʼdziko lake mwadzidzidzi.
Pambuyo pake ndidzawayikira wowalamulira amene ndamufuna Ine.
Wofanana nane ndani ndipo ndani amene angalimbane nane?
Ndi mtsogoleri wa dziko uti amene anganditengere ku bwalo la milandu?”
45 Nʼchifukwa chake imvani.
Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Babuloni.
Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo
ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
46 Akadzagwa Babuloni padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera,
ndipo kulira kwawo kudzamveka pakati pa mitundu yonse ya anthu.
Salimo la Davide.
28 Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa;
musakhale osamva kwa ine.
Pakuti mukapitirira kukhala chete,
ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
2 Imvani kupempha chifundo kwanga
pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize,
pomwe ndikukweza manja anga
kuloza ku malo anu oyeretsetsa.
3 Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa,
pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa,
amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo
koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.
4 Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo
ndi ntchito zawo zoyipa;
abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita
ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.
5 Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova,
ndi zimene manja ake anazichita,
Iye adzawakhadzula
ndipo sadzawathandizanso.
6 Matamando apite kwa Yehova,
popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.
7 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa;
mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa.
Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe
ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.
8 Yehova ndi mphamvu ya anthu ake,
linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.
9 Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu;
mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.
Salimo la Davide.
29 Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu,
perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
2 Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake,
pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.
3 Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi;
Mulungu waulemerero abangula,
Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.
4 Liwu la Yehova ndi lamphamvu;
liwu la Yehova ndi laulemerero.
5 Liwu la Yehova limathyola mikungudza;
Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.
6 Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe,
Siriyoni ngati mwana wa njati:
7 Liwu la Yehova limakantha
ngati kungʼanima kwa mphenzi.
8 Liwu la Yehova limagwedeza chipululu;
Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.
9 Liwu la Yehova limapindapinda mibawa
ndi kuyeretsa nkhalango.
Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”
10 Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira,
Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.
11 Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake;
Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.