M’Cheyne Bible Reading Plan
Samueli Adzoza Davide Kukhala Mfumu
16 Yehova anati kwa Samueli, “Kodi udzamulira Sauli mpaka liti, popeza Ine ndamukana kuti akhale mfumu ya Israeli? Dzaza mafuta mʼbotolo lako ndipo unyamuke kupita kwa Yese wa ku Betelehemu popeza ndadzisankhira mmodzi mwa ana ake kukhala mfumu.”
2 Koma Samueli anati, “Kodi ndingapite bwanji? Sauli akamva zimenezi adzandipha.”
Yehova anayankha, “Tenga ngʼombe yayikazi ndipo ukanene kuti, ‘Ndabwera kudzapereka nsembe kwa Yehova. 3 Ukamuyitane Yese ku mwambo wa nsembe, ndipo ine ndidzakuwuza choti ukachite. Ukandidzozere amene ndikakulozere.’ ”
4 Samueli anachita zimene Yehova ananena, ndipo anabweradi ku Betelehemu kuja. Akuluakulu a mu mzindawo anamuchingamira ali njenjenje ndi mantha ndipo anamufunsa kuti, “Kodi mwabwera mwa mtendere?”
5 Samueli anayankha kuti, “Inde, kwabwino. Ndabwera kudzapereka nsembe kwa Yehova. Mudzipatule ndipo mubwere kudzapereka nsembe pamodzi nane.” Kenaka iye anamupatula Yese ndi ana ake aamuna ndipo anawayitana kudzapereka nsembe.
6 Pamene anafika, Samueli anaona Eliabu ndipo anaganiza “Ndithu wodzozedwa wa Yehova uja ndi uyu wayima pamaso pakeyu.”
7 Koma Yehova anati kwa Samueli, “Usaone maonekedwe ake kapena msinkhu wake, pakuti ndamukana iyeyu. Yehova sapenya zimene munthu amapenya. Anthu amapenya zakunja, koma Mulungu amapenya za mu mtima.”
8 Kenaka Yese anayitana Abinadabu namubweretsa pamaso pa Samueli. Koma Samueli anati, “Yehova sanamusankhenso ameneyu.” 9 Ndipo Yese anayitana Sama, koma Samueli anati, “Ngakhale uyu Yehova sanamusankhe.” 10 Pambuyo pake, Yese anayitana ana ake amuna asanu ndi awiri kuti apite kwa Samueli. Koma Samueli anati, “Yehova sanasankhe amenewa.” 11 Tsono Samueli anafunsa Yese kuti, “Kodi awa ndi ana ako onse aamuna?”
Yese anayankha kuti, “Ayi, alipo wina wamngʼono amene watsala, koma akuweta nkhosa.”
Samueli anati, “Apite munthu akamutenge popeza sitipereka nsembe mpaka iye atabwera.”
12 Choncho anatuma munthu kukamutenga ndipo anabwera naye. Iye anali wofiirira, wa maonekedwe abwino ochititsa kaso.
Ndipo Yehova anati, “Mudzoze popeza ndi ameneyu.”
13 Samueli anatenga botolo la mafuta ndi kumudzoza pamaso pa abale ake, ndipo Mzimu wa Yehova unabwera mwamphamvu pa Davide kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo. Pambuyo pake Samueli anabwerera ku Rama.
Davide Atumikira Sauli
14 Nthawi imeneyo Mzimu wa Yehova unamuchokera Sauli, ndipo mzimu woyipa wochokera kwa Yehova unayamba kumuzunza.
15 Atumiki a Sauli anati, “Taonani mzimu woyipa wochokera kwa Mulungu ukukuzunzani. 16 Ndiyetu, inu mbuye wathu titumeni ife antchito anu kuti tikafune munthu wodziwa bwino kuyimba zeze. Tsono pamene mzimu woyipa wochokera kwa Mulungu wakufikirani, iye azidzayimba ndipo mudzakhala bwino.”
17 Choncho Sauli anati kwa atumiki ake, “Chabwino, kandipezereni munthu wodziwa bwino kuyimba ndipo mubwere naye kuno.”
18 Mmodzi mwa antchito ake anati, “Ine ndinaona mwana wa Yese wa ku Betelehemu. Ndiye munthu wodziwa bwino kuyimba, wolimba mtima, ngwazi pa nkhondo, wodziwa kuyankhula ndi wokongola. Ndipotu Yehova ali ndi iye.”
19 Ndipo Sauli anatumiza amithenga kwa Yese kukanena kuti, “Nditumizireni mwana wanu Davide, amene amaweta nkhosa.” 20 Choncho Yese anatenga bulu namunyamulitsa buledi, thumba la vinyo ndi mwana wambuzi mmodzi. Zonsezi anamupatsa mwana wake Davide kuti akapereke kwa Sauli.
21 Davide anafika kwa Sauli ndipo anayamba ntchito. Sauli anamukonda kwambiri Davide ndipo anamusandutsa wonyamula zida zake za nkhondo. 22 Kenaka Sauli anatumiza mawu kwa Yese ndi kuti, “Mulole kuti Davide azinditumikira, pakuti ndamukonda kwambiri.”
23 Nthawi zonse mzimu woyipa wochokera kwa Mulungu umati ukamufikira Sauli, Davide ankatenga zeze wake nʼkumamuyimbira. Choncho Sauli ankapeza bwino, ndipo mzimu woyipa uja unkamusiya.
Ofowoka ndi Amphamvu
14 Mulandire amene ndi ofowoka mʼchikhulupiriro, osatsutsana naye pa maganizo ake. 2 Chikhulupiriro cha munthu wina chimamulola kudya china chilichonse koma munthu wina, amene chikhulupiriro chake ndi chofowoka, amangodya zamasamba zokha. 3 Munthu amene amadya chilichonse sayenera kunyoza amene satero, ndipo munthu amene samadya chilichonse asaweruze munthu amene amatero, pakuti Mulungu anamulandira. 4 Kodi ndiwe ndani kuti uweruze wantchito wamwini? Mbuye wake yekha ndiye aweruze ngati iye wakhoza kapena walephera pa ntchito yake. Ndipo adzakhoza popeza kuti Mbuye wake angathe kumukhozetsa.
5 Munthu wina amayesa tsiku limodzi lopatulika kuposa lina. Munthu wina amayesa masiku onse ofanana. Aliyense akhale otsimikiza mʼmaganizo ake. 6 Iye amene amaganiza kuti tsiku limodzi ndi lopambana, amatero kwa Ambuye. Iye amene amadya nyama, amadya mwa Ambuye pakuti amayamika Mulungu. Ndipo iye amene sadya, amatero kwa Ambuye ndi kuyamika Mulungu. 7 Pakuti palibe wina wa ife amene amakhala moyo pa yekha ndiponso palibe wina wa ife amene amafa pa yekha. 8 Ngati ife tikhala ndi moyo, ife tikhala ndi moyo kwa Ambuye. Ndipo ngati ife tifa, tifa kwa Ambuye. Choncho, ngati tikhala ndi moyo kapena kufa, ndife ake a Ambuye.
9 Pa chifukwa ichi, Khristu anafa ndi kuukanso kotero kuti Iye akhale ndi Ambuye wa akufa ndi amoyo. 10 Tsono nʼchifukwa chiyani iwe ukuweruza mʼbale wako? Kapena nʼchifukwa chiyani ukumunyoza mʼbale wako? Pakuti ife tonse tidzayima pa mpando wakuweruza wa Mulungu. 11 Kwalembedwa, akutero Ambuye,
“Pamene Ine ndili ndi moyo,
aliyense adzandigwadira
ndipo lilime lililonse lidzavomereza Mulungu.”
12 Choncho tsopano, aliyense wa ife adzafotokoza yekha kwa Mulungu.
13 Motero, tiyeni tisiye kuweruzana wina ndi mnzake. Mʼmalo mwake, tsimikizani mʼmaganizo anu kuti musayike chokhumudwitsa kapena chotchinga mʼnjira ya mʼbale wanu. 14 Monga mmodzi amene ndili mwa Ambuye Yesu, ndine wotsimikiza mtima kuti palibe chakudya chimene pachokha ndi chodetsedwa. Koma ngati wina atenga china chake kukhala chodetsedwa, kwa iyeyo ndi chodetsedwa. 15 Ngati mʼbale wako akuvutika chifukwa cha chimene umadya, iwe sukuchitanso mwachikondi. Usamuwononge mʼbale wako amene Khristu anamufera chifukwa cha chakudya chakocho. 16 Musalole kuti chimene muchiyesa chabwino achinene ngati choyipa. 17 Pakuti Ufumu wa Mulungu si nkhani yakudya ndi kumwa, koma chilungamo, mtendere ndi chimwemwe mwa Mzimu Woyera. 18 Nʼchifukwa chake aliyense amene atumikira Khristu mʼnjira iyi akondweretsa Mulungu ndi kuvomerezedwa ndi anthu.
19 Tsono tiyeni tiyesetse kuchita zimene zidzabweretsa mtendere ndi kulimbikitsana mwachikondi. 20 Musawononge ntchito ya Mulungu chifukwa cha chakudya. Chakudya chonse ndi choyera, koma munthu amalakwa ngati adya chilichonse chimene chimakhumudwitsa wina. 21 Nʼkwabwino kusadya kapena kumwa vinyo kapena kuchita chilichonse chimene chidzachititsa mʼbale wako kugwa.
22 Tsono zimene ukukhulupirira pa zinthu izi zikhale pakati pa iwe ndi Mulungu. Wodala munthu amene sadzitsutsa yekha pa zimene amazivomereza. 23 Koma munthu amene akukayika atsutsidwa ngati adya, chifukwa kudya kwake si kwa chikhulupiriro; ndipo chilichonse chosachokera mʼchikhulupiriro ndi tchimo.
1 Haa! Mzinda uja wasiyidwa wokhawokha,
umene kale unali wodzaza ndi anthu!
Kale unali wotchuka pakati pa mitundu ya anthu!
Tsopano wasanduka ngati mkazi wamasiye.
Kale unali mfumukazi ya onse pa dziko lapansi,
tsopano wasanduka kapolo.
2 Ukulira mowawidwa mtima usiku wonse,
misozi ili pa masaya pake.
Mwa abwenzi ake onse,
palibe ndi mmodzi yemwe womutonthoza.
Abwenzi ake onse amuchitira chiwembu;
onse akhala adani ake.
3 Yuda watengedwa ku ukapolo,
kukazunzika ndi kukagwira ntchito yolemetsa.
Iye akukhala pakati pa anthu a mitundu ina;
ndipo alibe malo opumulira.
Onse omuthamangitsa iye amupitirira,
ndipo alibe kwina kothawira.
4 Misewu yopita ku Ziyoni ikulira,
chifukwa palibe ndi mmodzi yemwe akubwera ku maphwando ake.
Zipata zake zonse zili pululu,
ansembe akubuwula.
Anamwali ake akulira,
ndipo ali mʼmasautso woopsa.
5 Adani ake asanduka mabwana ake;
odana naye akupeza bwino.
Yehova wamubweretsera mavuto
chifukwa cha machimo ake ambiri.
Ana ake atengedwa ukapolo
pamaso pa mdani.
6 Ulemerero wonse wa mwana wamkazi wa Ziyoni
wachokeratu.
Akalonga ake ali ngati mbawala
zosowa msipu;
alibe mphamvu zothawira
owathamangitsa.
7 Pa masiku a masautso ndi kuzunzika kwake,
Yerusalemu amakumbukira chuma chonse
chimene mʼmasiku amakedzana chinali chake.
Anthu ake atagwidwa ndi adani ake,
panalibe aliyense womuthandiza.
Adani ake ankamuyangʼana
ndi kumuseka chifukwa cha kuwonongeka kwake.
8 Yerusalemu wachimwa kwambiri
ndipo potero wakhala wodetsedwa.
Onse amene ankamulemekeza pano akumunyoza,
chifukwa aona umaliseche wake.
Iye mwini akubuwula
ndipo akubisa nkhope yake.
9 Uve wake umaonekera pa zovala zake;
iye sanaganizire za tsogolo lake.
Nʼchifukwa chake kugwa kwake kunali kwakukulu;
ndipo analibe womutonthoza.
“Inu Yehova, taonani masautso anga,
pakuti mdani wapambana.”
10 Adani amulanda
chuma chake chonse;
iye anaona mitundu ya anthu achikunja ikulowa mʼmalo ake opatulika,
amene Inu Mulungu munawaletsa
kulowa mu msonkhano wanu.
11 Anthu ake onse akubuwula
pamene akufunafuna chakudya;
asinthanitsa chuma chawo ndi chakudya
kuti akhale ndi moyo.
“Inu Yehova, taonani ndipo ganizirani,
chifukwa ine ndanyozeka.”
12 “Kodi zimenezi mukuziyesa zachabe, inu nonse mukudutsa?
Yangʼanani ndipo muone.
Kodi pali mavuto ofanana ndi
amene andigwerawa,
amene Ambuye anandibweretsera
pa tsiku la ukali wake?
13 “Anatumiza moto kuchokera kumwamba,
unalowa mpaka mʼmafupa anga.
Anayala ukonde kuti ukole mapazi anga
ndipo anandibweza.
Anandisiya wopanda chilichonse,
wolefuka tsiku lonse.
14 “Wazindikira machimo anga onse
ndipo ndi manja ake anawaluka pamodzi.
Machimowa afika pakhosi panga,
ndipo Ambuye wandithetsa mphamvu.
Iye wandipereka
kwa anthu amene sindingalimbane nawo.
15 “Ambuye wakana
anthu anga onse amphamvu omwe ankakhala nane:
wasonkhanitsa gulu lankhondo kuti lilimbane nane,
kuti litekedze anyamata anga;
mʼmalo ofinyira mphesa Ambuye wapondereza
anamwali a Yuda.
16 “Chifukwa cha zimenezi ndikulira
ndipo maso anga adzaza ndi misozi.
Palibe aliyense pafupi woti anditonthoze,
palibe aliyense wondilimbitsa mtima.
Ana anga ali okhaokha
chifukwa mdani watigonjetsa.
17 “Ziyoni wakweza manja ake,
koma palibe aliyense womutonthoza.
Yehova walamula kuti abale ake
a Yakobo akhale adani ake;
Yerusalemu wasanduka
chinthu chodetsedwa pakati pawo.
18 “Yehova ndi wolungama,
koma ndine ndinawukira malamulo ake.
Imvani inu anthu a mitundu yonse;
onani masautso anga.
Anyamata ndi anamwali anga
agwidwa ukapolo.
19 “Ndinayitana abwenzi anga
koma anandinyenga.
Ansembe ndi akuluakulu anga
anafa mu mzinda
pamene ankafunafuna chakudya
kuti akhale ndi moyo.
20 “Inu Yehova, onani mmene ine ndavutikira!
Ndikuzunzika mʼkati mwanga,
ndipo mu mtima mwanga ndasautsidwa
chifukwa ndakhala osamvera.
Mʼmisewu anthu akuphedwa,
ndipo ku mudzi kuli imfa yokhayokha.
21 “Anthu amva kubuwula kwanga,
koma palibe wonditonthoza.
Adani anga onse amva masautso anga;
iwo akusangalala pa zimene Inu mwachita.
Lifikitseni tsiku limene munalonjeza lija
kuti iwonso adzakhale ngati ine.
22 “Lolani kuti ntchito zawo zoyipa zifike pamaso panu;
muwalange
ngati mmene mwandilangira ine
chifukwa cha machimo anga onse.
Ndikubuwula kwambiri
ndipo mtima wanga walefuka.”
Salimo la Davide. Malangizo.
32 Ngodala munthu
amene zolakwa zake zakhululukidwa;
amene machimo ake aphimbidwa.
2 Ngodala munthu
amene machimo ake Yehova sawawerengeranso pa iye
ndipo mu mzimu mwake mulibe chinyengo.
3 Pamene ndinali chete,
mafupa anga anakalamba
chifukwa cha kubuwula kwanga tsiku lonse.
4 Pakuti usana ndi usiku
dzanja lanu linandipsinja;
mphamvu zanga zinatha
monga nthawi yotentha yachilimwe.
Sela
5 Kotero ine ndinavomereza tchimo langa kwa Inu,
sindinabise mphulupulu zanga.
Ndinati, “Ine ndidzawulula
zolakwa zanga kwa Yehova,
ndipo Inu munandikhululukira
mlandu wa machimo anga.”
Sela
6 Choncho aliyense okhulupirika apemphere kwa Inuyo
pomwe mukupezeka;
ndithu pamene madzi amphamvu auka,
sadzamupeza.
7 Inu ndi malo anga obisala;
muzinditeteza ku mavuto ndipo muzindizinga
ndi nyimbo zachipulumutso.
Sela
8 Ndidzakulangiza ndi kukuphunzitsa njira imene udzayendamo;
ndidzakupatsa uphungu ndi kukuyangʼanira.
9 Usakhale ngati kavalo kapena bulu,
zimene zilibe nzeru,
koma ziyenera kuwongoleredwa ndi zitsulo za mʼkamwa ndi pamutu,
ukapanda kutero sizibwera kwa iwe.
10 Zowawa ndi zambiri za anthu oyipa
koma chikondi chosatha cha Yehova
chimamuzinga munthu amene amadalira Iye.
11 Kondwerani mwa Yehova inu olungama;
imbani, inu nonse amene muli owongoka mtima!
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.