Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
BUKU LACHISANU
Masalimo 107–150
107 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;
pakuti chikondi chake ndi chosatha.
2 Owomboledwa a Yehova anene zimenezi
amene Iyeyo anawawombola mʼdzanja la mdani,
3 iwo amene anawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko,
kuchokera kumadzulo ndi kummawa, kuchokera kumpoto ndi kummwera.
4 Ena anayendayenda mʼchipululu mopanda kanthu,
osapeza njira yopitira ku mzinda kumene akanakakhazikikako.
5 Iwo anamva njala ndi ludzu,
ndipo miyoyo yawo inafowokeratu.
6 Pamenepo analirira Yehova mʼmavuto awo
ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.
7 Iye anawatsogolera mʼnjira yowongoka
kupita ku mzinda umene anakakhazikikako.
8 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
ndi chifukwa cha machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,
9 pakuti Iye wapha ludzu la munthu womva ludzu
ndipo wakhutitsa wanjala ndi zinthu zabwino.
43 Aliyense wanzeru asamalitse zinthu zimenezi
ndi kuganizira za chikondi chachikulu cha Yehova.
Israeli Akolola Kamvuluvulu
8 “Ika lipenga pakamwa pako.
Ngati chiwombankhanga, kutsutsana ndi nyumba ya Yehova
chifukwa anthu aphwanya pangano langa
ndiponso agalukira lamulo langa.
2 Israeli akulirira kwa Ine kuti,
‘Inu Mulungu wathu, ife timakudziwani!’
3 Koma Israeli wakana zabwino;
mdani adzamuthamangitsa.
4 Amalonga mafumu mosatsata kufuna kwanga.
Amasankha akalonga popanda chilolezo changa.
Amadzipangira mafano
asiliva ndi agolide
koma adzawonongeka nawo.
5 Iwe Samariya, taya fano lako la mwana wangʼombe!
Mkwiyo wanga wayakira anthuwo.
Padzapita nthawi yayitali chotani asanasinthike kukhala oyera mtima?
6 Mafanowa ndi ochokera ku Israeli!
Mwana wa ngʼombe uyu anapangidwa ndi munthu waluso;
si Mulungu amene anamupanga.
Adzaphwanyidwa nʼkukhala zidutswa,
mwana wangʼombe wa ku Samariya.
7 “Aisraeli amadzala mphepo
ndipo amakolola kamvuluvulu.
Tirigu alibe ngala;
sadzabala chakudya.
Akanabala chakudya
alendo akanadya chakudyacho.
8 Israeli wamezedwa,
tsopano ali pakati pa anthu a mitundu ina
ngati chinthu cha chabechabe.
9 Pakuti iwo anapita ku Asiriya
ngati mbidzi yongodziyendera pa yokha.
Efereimu wadzigulitsa kwa zibwenzi zake.
10 Ngakhale wadzigulitsa pakati pa mitundu ya anthu,
Ine ndidzawasonkhanitsa pamodzi.
Iwo adzayamba kuzunzika pansi pa
ulamuliro wankhanza wa mfumu yamphamvu.
11 “Ngakhale Efereimu anamanga maguwa ambiri a nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo,
maguwa amenewa akhala malo ochimwirapo.
12 Ndinawalembera zinthu zambiri za malamulo anga,
koma iwo anaziyesa ngati zinthu zachilendo.
13 Amapereka nsembe za nyama kwa Ine
ndipo iwo amadya nyamayo,
koma Yehova sakondwera nazo.
Tsopano Iye adzakumbukira zoyipa zawo
ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo:
iwowo adzabwerera ku Igupto.
14 Israeli wayiwala Mlengi wake
ndipo wamanga nyumba zaufumu;
Yuda wachulukitsa mizinda ya malinga.
Koma Ine ndidzaponya moto pa mizinda yawoyo,
moto umene udzatenthe malinga awo.”
Kulemekeza Mulungu
33 Aa! Nzeru za Mulungu ndi chidziwitso chake ndi zozama kwambiri!
Ndani angazindikire maweruzidwe ake,
ndipo njira zake angazitulukire ndani?
34 “Kodi wadziwa ndani maganizo a Ambuye?
Kapena ndani anakhalapo mlangizi wake?”
35 “Kodi ndani anapereka mphatso kwa Mulungu,
kuti Mulunguyo amubwezere iye?”
36 Pakuti zinthu zonse nʼzochokera kwa Iye, nʼzolengedwa ndi Iye ndipo zimabweretsa ulemerero kwa Iye.
Kwa Iye kukhale ulemerero mpaka muyaya! Ameni.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.