Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 44

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora.

44 Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu;
    makolo athu atiwuza
zimene munachita mʼmasiku awo,
    masiku akalekalewo.
Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena
    ndi kudzala makolo athu;
Inu munakantha mitundu ya anthu,
    koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
Sanalande dziko ndi lupanga lawo,
    si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso,
koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu,
    pakuti munawakonda.

Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga
    amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu;
    kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
Sindidalira uta wanga,
    lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
koma Inu mumatigonjetsera adani athu,
    mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse,
    ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.

Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa;
    Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
10 Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani
    ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
11 Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa
    ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
12 Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika,
    osapindulapo kanthu pa malondawo.

13 Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina,
    chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
14 Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina;
    anthu amapukusa mitu yawo akationa.
15 Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse
    ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
16 chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe,
    chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.

17 Zonsezi zinatichitikira
    ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu
    kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
18 Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo;
    mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
19 Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe
    ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.

20 Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu
    kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
21 kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi,
    pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
22 Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse,
    tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.

23 Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona!
    Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
24 Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu,
    ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?

25 Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi;
    matupi athu amatirira pa dothi.
26 Imirirani ndi kutithandiza,
    tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.

Hoseya 2:14-3:5

14 “Koma tsopano ndidzamukopa mkaziyo;
    ndidzapita naye ku chipululu
    ndipo ndidzamuyankhula mwachikondi.
15 Kumeneko ndidzamubwezera minda yake ya mpesa,
    ndipo ndidzasandutsa Chigwa cha Akori kukhala khomo la chiyembekezo.
Kumeneko iye adzayimba nyimbo monga mʼmasiku a ubwana wake,
    monga tsiku limene anatuluka ku Igupto.

16 “Tsiku limeneli,” Yehova akuti,
    “udzandiyitana kuti, ‘Amuna anga;’
    sudzandiyitananso kuti, ‘Mbuye wanga.’
17 Ndidzachotsa mayina a Abaala pakamwa pake;
    sadzatchulanso mayina awo popemphera.
18 Tsiku limenelo ndidzachita pangano
    ndi zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga
    ndiponso zolengedwa zokwawa pansi kuti ziyanjane ndi anthu anga.
Ndidzachotsa mʼdzikomo uta,
    lupanga ndi zida zonse zankhondo,
    kuti onse apumule mwamtendere.
19 Ndidzakutomera kuti ukhale mkazi wanga mpaka muyaya;
    ndidzakutomera mwachilungamo, mwaungwiro,
    mwachikondi ndi mwachifundo.
20 Ndidzakutomera mokhulupirika
    ndipo udzadziwa Yehova.

21 “Tsiku limenelo Ine ndidzayankha,”
    akutero Yehova.
“Ndidzayankha mlengalenga pempho lake lofuna mitambo
    ndipo mvula idzagwa pa dziko lapansi;
22 ndipo nthaka idzamvera kupempha kwa tirigu,
    vinyo ndi mafuta,
    ndipo zidzamvera Yezireeli.
23 Ndidzadzala Israeli mʼdziko kuti akhale wanga:
    ndidzaonetsa chikondi changa kwa anthu amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Sakondedwa.’
Ndidzawawuza amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Si anthu anga,’ kuti, ‘Ndinu anthu wanga;’
    ndipo adzanena kuti, ‘ndinu Mulungu wathu,’ ”

Hoseya Ayanjana ndi Mkazi Wake

Yehova anati kwa ine, “Pita kamukondenso mkazi wako, ngakhale ali pa chibwenzi ndi wina ndi kuti ndi wachigololo. Mukonde iyeyo monga momwe Yehova amakondera Aisraeli, ngakhale iwo amapita kukapembedza milungu ina ndi kukonda nsembe za keke zamphesa zowuma.”

Motero ndinamukwatira popereka ndalama khumi ndi zisanu zasiliva, ndiponso mitanga isanu ndi iwiri ya barele. Kenaka ndinamuwuza mkaziyo kuti, “Ukhale nane masiku ambiri; usachitenso zachiwerewere kapena chigololo ndi munthu wina, ndipo ine ndidzakhala nawe.”

Pakuti Aisraeli adzakhala masiku ambiri opanda mfumu kapena kalonga, osapereka nsembe kapena kuyimika miyala yachipembedzo, wopanda efodi kapena fano. Pambuyo pake Aisraeli adzabwerera ndi kufunafuna Yehova Mulungu wawo ndi Davide mfumu yawo. Adzabwera kwa Yehova akunjenjemera ndipo adzalandira madalitso mʼmasiku awo otsiriza.

Akolose 2:16-3:1

Ufulu Wathu

16 Nʼchifukwa chake musalole wina aliyense kukuzengani mlandu chifukwa cha zimene mumadya kapena kumwa, kapena za masiku achikondwerero cha chipembedzo, za chikondwerero cha mwezi watsopano, kapena za tsiku la Sabata. 17 Zimenezi ndi chithunzithunzi chabe cha zinthu zimene zikubwera, koma choonadi chenicheni chikupezeka mwa Khristu. 18 Musalole kuti wina aliyense amene amakonda kudzichepetsa mwachiphamaso ndi kumapembedza angelo akulepheretseni kukalandira mphotho. Munthu woteroyu amayankhulanso mwatsatanetsatane zinthu zimene akuti anaziona mʼmasomphenya. Anthuwa ndi odzitukumula ndi fundo zopanda pake zochokera mʼmaganizo mwawo amene si auzimu. 19 Iwo sakulumikizananso ndi mutu, kumene kumachokera thupi lonse, logwirizidwa ndi kumangiriridwa pamodzi ndi mʼmitsempha yake ndi mnofu, limene limakula monga mmene Mulungu afunira kuti likulire.

20 Popeza munafa pamodzi ndi Khristu kusiyana nayo miyambo ya dziko lapansi lino, nʼchifukwa chiyani mukukhalanso ngati a dziko lapansi lino? Bwanji mukumvera malamulo monga awa: 21 “Usagwire chakuti,” “Usalawe chakuti,” “Usakhudze chakuti?” 22 Malamulo amenewa amakhudza zinthu zimene zimatha zikamagwiritsidwa ntchito, ndipo malamulo ndi zophunzitsa za anthu chabe. 23 Ndithu malamulo oterewa amaoneka ngati anzeru, pakuti amalamulira anthu ambiri pa zachipembedzo ndi pa zakudzichepetsa kwa chiphamaso, ndi pa zakuzunza thupi lawo, koma alibe mphamvu zoletsa kuchita zofuna za thupilo.

Moyo Watsopano

Tsono popeza munaukitsidwa pamodzi ndi Khristu, ikani mitima yanu pa zinthu za kumwamba, kumene Khristu akukhala ku dzanja lamanja la Mulungu.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.