Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora.
44 Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu;
makolo athu atiwuza
zimene munachita mʼmasiku awo,
masiku akalekalewo.
2 Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena
ndi kudzala makolo athu;
Inu munakantha mitundu ya anthu,
koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
3 Sanalande dziko ndi lupanga lawo,
si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso,
koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu,
pakuti munawakonda.
4 Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga
amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
5 Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu;
kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
6 Sindidalira uta wanga,
lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
7 koma Inu mumatigonjetsera adani athu,
mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
8 Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse,
ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
9 Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa;
Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
10 Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani
ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
11 Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa
ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
12 Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika,
osapindulapo kanthu pa malondawo.
13 Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina,
chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
14 Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina;
anthu amapukusa mitu yawo akationa.
15 Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse
ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
16 chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe,
chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
17 Zonsezi zinatichitikira
ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu
kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
18 Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo;
mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
19 Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe
ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
20 Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu
kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
21 kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi,
pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
22 Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse,
tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
23 Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona!
Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
24 Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu,
ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
25 Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi;
matupi athu amatirira pa dothi.
26 Imirirani ndi kutithandiza,
tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
11 “Kunenanso za iwe Yuda,
udzakolola chilango.
“Pamene ndiwabwezere anthu anga zinthu zabwino.”
7 Pamene ndichiritsa Israeli,
machimo a Efereimu amaonekera poyera
ndiponso milandu ya Samariya sibisika.
Iwo amachita zachinyengo,
mbala zimathyola nyumba,
achifwamba amalanda anthu katundu mʼmisewu.
2 Koma sazindikira kuti Ine
ndimakumbukira zoyipa zawo zonse.
Azunguliridwa ndi zolakwa zawo;
ndipo sizichoka mʼmaso mwanga.
3 “Anthuwa amasangalatsa mfumu ndi zoyipa zawozo,
akalonga amasekerera mabodza awo.
4 Onsewa ndi anthu azigololo,
otentha ngati moto wa mu uvuni,
umene wophika buledi sasonkhezera
kuyambira pamene akukanda buledi mpaka atafufuma.
5 Pa tsiku la chikondwerero cha mfumu yathu
akalonga amaledzera ndi vinyo,
ndipo amalowa mʼgulu la anthu achipongwe.
6 Mitima yawo ili ngati uvuni;
amayandikira Mulungu mwachiwembu.
Ukali wawo umanyeka usiku wonse,
mmawa umayaka ngati malawi a moto.
7 Onsewa ndi otentha ngati uvuni,
amapha olamulira awo.
Mafumu awo onse amagwa,
ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amandiyitana Ine.
8 “Efereimu wasakanikirana ndi mitundu ya anthu ena;
Efereimu ndi buledi amene wapsa mbali imodzi.
9 Alendo atha mphamvu zake,
koma iye sakuzindikira.
Tsitsi lake layamba imvi
koma iye sakudziwa.
10 Kunyada kwake Israeli kukumutsutsa,
koma pa zonsezi
iye sakubwerera kwa Yehova Mulungu wake
kapena kumufunafuna.
11 “Efereimu ali ngati nkhunda
yopusa yopanda nzeru.
Amayitana Igupto
namapita ku Asiriya.
12 Akamadzapita, ndidzawakola ndi ukonde wanga;
ndidzawagwetsa pansi ngati mbalame zamumlengalenga.
Ndikadzamva kuti asonkhana pamodzi
ndidzawakola.
13 Tsoka kwa iwo,
chifukwa andisiya Ine!
Chiwonongeko kwa iwo,
chifukwa andiwukira!
Ndimafunitsitsa kuwapulumutsa
koma amayankhula za Ine monama.
14 Iwo salirira kwa Ine kuchokera pansi pa mtima,
koma amalira mofuwula ali pa bedi pawo.
Amadzichekacheka chifukwa chofuna tirigu ndi vinyo watsopano,
koma amandifulatira.
15 Ine ndinawaphunzitsa ndikuwalimbitsa,
koma amandikonzera chiwembu.
16 Iwo satembenukira kwa Wammwambamwamba;
ali ngati uta woonongeka.
Atsogoleri awo adzaphedwa ndi lupanga
chifukwa cha mawu awo achipongwe.
Motero iwo adzasekedwa
mʼdziko la Igupto.
Kukonda Adani
43 “Munamva kuti, ‘Konda mnansi wako ndi kudana ndi mdani wako.’ 44 Koma Ine ndikuwuzani kuti, ‘Kondani adani anu ndi kuwapempherera okuzunzani 45 kuti mukhale ana a Atate anu akumwamba, amene awalitsa dzuwa lake pa oyipa ndi pa abwino, nagwetsa mvula pa olungama ndi pa osalungama.’ 46 Ngati mukonda amene akukondani inu, mudzapeza mphotho yanji? Kodi ngakhale amisonkho sachita chimodzimodzi? 47 Ndipo ngati inu mupatsa moni abale anu okhaokha mukuchita chiyani choposa ena? Kodi ngakhale akunja sachita chimodzimodzi? 48 Nʼchifukwa chake, inu khalani angwiro monga Atate anu akumwamba ali wangwiro.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.