Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini.
7 Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu;
pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,
2 mwina angandikadzule ngati mkango,
ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.
3 Inu Yehova Mulungu wanga,
ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,
4 ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere,
kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,
5 pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira,
lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi
ndipo mundigoneke pa fumbi.
Sela
6 Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu;
nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga.
Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.
7 Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani.
Alamulireni muli kumwambako;
8 Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo.
Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa,
monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.
9 Inu Mulungu wolungama,
amene mumasanthula maganizo ndi mitima,
thetsani chiwawa cha anthu oyipa
ndipo wolungama akhale motetezedwa.
10 Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba,
amene amapulumutsa olungama mtima.
11 Mulungu amaweruza molungama,
Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.
12 Ngati munthu satembenuka,
Mulungu adzanola lupanga lake,
Iye adzawerama ndi kukoka uta.
13 Mulungu wakonza zida zake zoopsa;
Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.
14 Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse.
Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.
15 Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa
amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.
16 Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini;
chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.
17 Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake;
ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.
6 “Ndine amene ndinakusendetsani milomo mʼmizinda yanu yonse,
ndipo munasowa chakudya mʼmizinda yanu.
Komatu inu simunabwerere kwa Ine,”
akutero Yehova.
7 “Ndinenso amene ndinamanga mvula
patangotsala miyezi itatu kuti mukolole.
Ndinagwetsa mvula pa mzinda wina,
koma pa mzinda wina ayi,
mvula inkagwa pa munda wina;
koma sinagwe pa munda wina ndipo mbewu zinawuma.
8 Anthu ankayenda mzinda ndi mzinda kufuna madzi,
koma sanapeze madzi okwanira kumwa.
Komabe inu simunabwerere kwa Ine,”
akutero Yehova.
9 “Nthawi zambiri ndinakantha mbewu zanu ndiponso minda ya mpesa,
ndinayikantha ndi chinsikwi ndiponso ndi chiwawu.
Dzombe linawononga mikuyu yanu ndi mitengo ya olivi.
Komabe inu simunabwerere kwa Ine,”
akutero Yehova.
10 “Ine ndinabweretsa miliri pakati panu
monga ndinachitira ku Igupto.
Ndinapha anyamata anu ndi lupanga,
ndinapereka akavalo anu kwa adani.
Ndinakununkhitsani fungo la mitembo lochokera mʼmisasa yanu ya nkhondo.
Komatu inu simunabwerere kwa Ine,”
akutero Yehova.
11 “Ndinawononga ena mwa inu
monga ndinawonongera Sodomu ndi Gomora.
Inu munali ngati chikuni choyaka chimene chafumulidwa pa moto.
Komabe inu simunabwerere kwa Ine,”
akutero Yehova.
12 “Choncho izi ndi zimene ndidzakuchitire iwe Israeli,
chifukwa ndidzakuchitira zimenezi,
konzekera kukumana ndi Mulungu wako, iwe Israeli.”
13 Iye amene amawumba mapiri,
amalenga mphepo,
ndipo amawululira munthu za mʼmaganizo ake,
Iye amene amasandutsa usana kuti ukhale mdima,
ndipo amayenda pa zitunda za dziko lapansi,
dzina lake ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
Kukondana Wina ndi Mnzake
11 Uthenga umene munawumva kuyambira pachiyambi ndi uwu: Tizikondana wina ndi mnzake. 12 Musakhale ngati Kaini, amene anali wa woyipayo ndipo anapha mʼbale wake. Nanga anamupha chifukwa chiyani? Chifukwa zochita zake zinali zoyipa ndipo zochita za mʼbale wake zinali zolungama. 13 Abale anga, musadabwe ngati dziko lapansi lidana nanu. 14 Ife tikudziwa kuti tinatuluka mu imfa ndi kulowa mʼmoyo, chifukwa timakonda abale athu. Aliyense amene sakonda mʼbale wake akanali mu imfa. 15 Aliyense amene amadana ndi mʼbale wake ndi wakupha, ndipo inu mukudziwa kuti wopha anthu mwa iye mulibe moyo wosatha.
16 Mmene timadziwira chikondi chenicheni ndi umu: Yesu anapereka moyo wake chifukwa cha ife. Ndipo nafenso tiyenera kupereka miyoyo yathu chifukwa cha abale athu. 17 Ngati wina ali ndi chuma ndipo nʼkuona mʼbale wake akusowa, koma wosamvera chisoni, kodi mwa iyeyo muli chikondi cha Mulungu?
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.