Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 119:17-32

Gimeli

17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo;
    kuti tsono ndisunge mawu anu.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona
    zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi;
    musandibisire malamulo anu.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka
    malamulo anu nthawi zonse.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa,
    amene achoka pa malamulo anu.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo
    pakuti ndimasunga malamulo anu.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza,
    mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24 Malamulo anu amandikondweretsa;
    ndiwo amene amandilangiza.

Daleti

25 Moyo wanga wakangamira fumbi;
    tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha;
    phunzitseni malamulo anu.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu;
    pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni;
    limbikitseni monga mwa mawu anu.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo;
    mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30 Ndasankha njira ya choonadi;
    ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova;
    musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu,
    pakuti Inu mwamasula mtima wanga.

Amosi 9:5-15

Ambuye Yehova Wamphamvuzonse
    amene amakhudza dziko lapansi ndipo dzikolo limasungunuka,
    onse amene amakhala mʼmenemo amalira.
Dziko lonse lidzadzaza ngati mtsinje wa Nailo,
    kenaka nʼkuphwera ngati mtsinje wa ku Igupto.
Iye amene amamanga malo ake okhalamo kumwamba,
    ndi kuyika maziko ake pa dziko lapansi,
Iye amene amayitana madzi a ku nyanja
    ndikuwakhuthulira pa dziko lapansi,
    dzina lake ndiye Yehova.

“Kodi kwa Ine, inu Aisraeli, simuli
    chimodzimodzi ndi Akusi?”
            Akutero Yehova.
“Kodi sindine amene ndinatulutsa Israeli ku Igupto,
    Afilisti ku Kafitori
    ndi Aaramu ku Kiri?

“Taonani, maso a Ambuye Yehova
    ali pa ufumu wochimwawu.
Ndidzawufafaniza
    pa dziko lapansi.
Komabe sindidzawononga kotheratu
    nyumba ya Yakobo,”
            akutero Yehova.
“Pakuti ndidzalamula,
    ndipo ndidzagwedeza nyumba ya Israeli
    pakati pa mitundu yonse ya anthu
monga momwe amasefera ufa mʼsefa,
    koma palibe nʼkamwala kamodzi komwe kamene kadzagwe pansi.
10 Anthu onse ochimwa pakati pa anthu anga
    adzaphedwa ndi lupanga,
onse amene amanena kuti,
    ‘Tsoka silidzatigwera ife kapena kutiwononga.’

Kubwezeretsedwa kwa Israeli

11 “Tsiku limenelo ndidzabwezeretsa
    nyumba ya Davide imene inagwa.
Ndidzakonzanso malo amene anagumuka,
    ndi kuyimanganso
    monga inalili poyamba,
12 kuti adzatengenso otsala a Edomu
    ndi mitundu yonse imene imatchedwa ndi dzina langa,”
            akutero Yehova amene adzachita zinthu izi.

13 Yehova akunena kuti

“Nthawi ikubwera pamene mlimi wotipula adzapyola wokolola
    ndipo woponda mphesa adzapyola wodzala mbewu.
Mapiri adzachucha vinyo watsopano
    ndi kuyenderera pa zitunda zonse.
14 Ndidzawabwezeranso pabwino anthu anga Aisraeli;
    mizinda imene inali mabwinja idzamangidwanso ndipo azidzakhalamo.
Adzalima minda ya mpesa ndipo adzamwa vinyo wake;
    adzalima minda ndipo adzadya zipatso zake.
15 Ndidzakhazika Aisraeli mʼdziko mwawo,
    ndipo sadzachotsedwamonso mʼdziko
    limene Ine ndawapatsa,”

            akutero Yehova Mulungu wako.

Yohane 6:41-51

41 Pamenepo Ayuda anayamba kungʼungʼudza chifukwa anati, “Ine ndine chakudya chotsika kuchokera kumwamba.” 42 Iwo anati, “Kodi uyu si Yesu, mwana wa Yosefe, amene abambo ake ndi amayi ake timawadziwa? Nanga Iyeyu akunena bwanji kuti, ‘Ine ndinatsika kuchokera kumwamba?’ ”

43 Yesu anayankha kuti, “Musangʼungʼudze pakati panu.” 44 Palibe munthu amene angabwere kwa Ine, ngati Atate amene anandituma Ine samubweretsa. Ndipo Ine ndidzamuukitsa kwa akufa pa tsiku lomaliza. 45 Aneneri analemba kuti, “Onse adzaphunzitsidwa ndi Mulungu! Aliyense amene amamva Atate ndi kuphunzira kwa Iye amabwera kwa Ine. 46 Palibe amene anaona Atate koma yekhayo amene achokera kwa Mulungu; yekhayo ndiye anaona Atate. 47 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti Iye amene akhulupirira ali nawo moyo wosatha. 48 Ine ndine chakudya chamoyo. 49 Makolo anu akale anadya mana mʼchipululu, komabe anafa. 50 Koma pano pali chakudya chochokera kumwamba, chimene munthu akadya sangafe. 51 Ine ndine chakudya chamoyo chochokera kumwamba. Ngati munthu adya chakudya ichi, adzakhala ndi moyo nthawi zonse. Chakudya chimenechi ndi thupi langa, limene Ine ndidzalipereka kuti anthu pa dziko lapansi akhale ndi moyo.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.