Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 52

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, ndakatulo ya Davide; pamene Doegi Mwedomu anapita kwa Sauli ndi kunena kuti “Davide wapita ku nyumba ya Ahimeleki.”

52 Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira ndi zoyipa, iwe munthu wamphamvu?
    Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira tsiku lonse,
    iwe munthu wochititsa manyazi pamaso pa Mulungu?
Tsiku lonse umakhalira kuganizira za kuwononga ena;
    lilime lako lili ngati lumo lakuthwa,
    ntchito yako nʼkunyenga.
Iwe umakonda choyipa mʼmalo mwa kuyankhula choonadi.
    Umakonda kunama kupambana kuyankhula zoona.
            Sela
Umakonda mawu onse opweteka,
    iwe lilime lachinyengo!

Zoonadi Mulungu adzakutsitsa kupita ku chiwonongeko chamuyaya:
    iye adzakukwatula ndi kukuchotsa mʼtenti yako;
    iye adzakuzula kuchoka mʼdziko la amoyo.
Olungama adzaona zimenezi ndi kuchita mantha;
    adzamuseka nʼkumanena kuti,
“Pano tsopano pali munthu
    amene sanayese Mulungu linga lake,
koma anakhulupirira chuma chake chambiri
    nalimbika kuchita zoyipa!”

Koma ine ndili ngati mtengo wa olivi
    wobiriwira bwino mʼnyumba ya Mulungu;
ndimadalira chikondi chosatha cha Mulungu
    kwa nthawi za nthawi.
Ine ndidzakutamandani kwamuyaya chifukwa cha zimene mwachita;
    chifukwa cha zimene mwachita; mʼdzina lanu ndidzayembekezera
    pakuti dzina lanulo ndi labwino. Ndidzakutamandani pamaso pa oyera mtima anu.

Amosi 5:10-17

10 inu mumadana ndi amene amadzudzula mʼbwalo la milandu
    ndi kunyoza amene amanena zoona.

11 Mumapondereza munthu wosauka
    ndi kumukakamiza kuti akupatseni tirigu.
Nʼchifukwa chake, ngakhale mwamanga nyumba zamiyala yosema,
    inuyo simudzakhalamo.
Ngakhale mwalima minda yabwino ya mphesa,
    inu simudzamwa vinyo wake.
12 Pakuti Ine ndikudziwa kuchuluka kwa zolakwa zanu
    ndi kukula kwa machimo anu.

Inu mumapondereza anthu olungama ndi kulandira ziphuphu
    ndipo anthu osauka simuwaweruza mwachilungamo mʼmabwalo anu amilandu.
13 Nʼchifukwa chake pa nthawi yotere munthu wanzeru sayankhulapo kanthu,
    popeza ndi nthawi yoyipa.

14 Muyike mtima wanu pa zabwino osati pa zoyipa,
    kuti mukhale ndi moyo.
Mukatero Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzakhala nanu,
    monga mmene mumanenera kuti ali nanu.
15 Mudane ndi zoyipa, mukonde zabwino;
    mukhazikitse chiweruzo cholungama mʼmabwalo anu amilandu.
Mwina mwake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzachitira chifundo
    anthu otsala a mʼbanja la Yosefe.

16 Choncho izi ndi zimene Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, akunena:

“Mʼmisewu monse mudzakhala kulira mofuwula,
    ndi kulira chifukwa cha kuwawa kwa masautso kudzakhala paliponse.
Adzayitana alimi kuti adzalire,
    ndipo anthu odziwa maliridwe anthetemya adzalira mofuwula.
17 Mʼminda yonse ya mpesa mudzakhala kulira kokhakokha,
    pakuti Ine ndidzadutsa pakati panu,”
            akutero Yehova.

Ahebri 5:1-6

Mkulu wa ansembe aliyense amasankhidwa kuchokera pakati pa anthu ndipo amayikidwa kuti aziwayimirira pamaso pa Mulungu, kuti azipereka mphatso ndi nsembe chifukwa cha machimo. Popeza kuti iye mwini ali ndi zofowoka zake, amatha kuwalezera mtima amene ali osadziwa ndi osochera. Chifukwa cha ichi, iye amadziperekera nsembe chifukwa cha machimo ake omwe ndiponso chifukwa cha machimo a anthu ena.

Palibe amene amadzipatsa yekha ulemu wotere, koma amachita kuyitanidwa ndi Mulungu monga momwe anayitanidwira Aaroni. Nʼchifukwa chake Khristu sanadzipatse yekha ulemu wokhala Mkulu wa ansembe. Koma Mulungu anamuwuza kuti,

“Iwe ndiwe Mwana wanga;
    Ine lero ndakhala Atate ako.”

Ndipo penanso anati,

“Iwe ndiwe wansembe mpaka muyaya,
    monga mwa unsembe wa Melikizedeki.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.