Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
BUKU LACHISANU
Masalimo 107–150
107 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;
pakuti chikondi chake ndi chosatha.
2 Owomboledwa a Yehova anene zimenezi
amene Iyeyo anawawombola mʼdzanja la mdani,
3 iwo amene anawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko,
kuchokera kumadzulo ndi kummawa, kuchokera kumpoto ndi kummwera.
4 Ena anayendayenda mʼchipululu mopanda kanthu,
osapeza njira yopitira ku mzinda kumene akanakakhazikikako.
5 Iwo anamva njala ndi ludzu,
ndipo miyoyo yawo inafowokeratu.
6 Pamenepo analirira Yehova mʼmavuto awo
ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.
7 Iye anawatsogolera mʼnjira yowongoka
kupita ku mzinda umene anakakhazikikako.
8 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
ndi chifukwa cha machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,
9 pakuti Iye wapha ludzu la munthu womva ludzu
ndipo wakhutitsa wanjala ndi zinthu zabwino.
43 Aliyense wanzeru asamalitse zinthu zimenezi
ndi kuganizira za chikondi chachikulu cha Yehova.
Chilango cha Israeli
9 Iwe Israeli, usakondwere;
monga imachitira mitundu ina.
Pakuti wakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wako;
umakonda malipiro a chiwerewere
pa malo aliwonse opunthira tirigu.
2 Malo opunthira tirigu ndi malo opsinyira mphesa sadzadyetsa anthu;
adzasowa vinyo watsopano.
3 Sadzakhalanso mʼdziko la Yehova.
Efereimu adzabwerera ku Igupto
ndipo mudzadya chakudya chodetsedwa ku Asiriya.
4 Iwo sadzaperekanso chopereka cha chakumwa kwa Yehova,
kapena nsembe zawo kuti akondweretse Yehovayo.
Nsembe zotere zidzakhala kwa iwo ngati chakudya cha anamfedwa;
onse akudya chakudya chimenechi adzakhala odetsedwa.
Chakudya ichi chidzakhala chodya okha,
sichidzalowa mʼnyumba ya Yehova.
5 Kodi mudzachita chiyani pa tsiku la maphwando anu oyikika;
pa masiku a zikondwerero za Yehova?
6 Ngakhale iwo atathawa chiwonongeko,
Igupto adzawasonkhanitsa,
ndipo Mefisi adzawayika mʼmanda.
Khwisa adzamera pa ziwiya zawo zasiliva,
ndipo minga idzamera mʼmatenti awo.
7 Masiku achilango akubwera,
masiku obwezera ali pafupi.
Israeli adziwe zimenezi.
Chifukwa machimo anu ndi ochuluka kwambiri
ndipo udani wanu pa Mulungu ndi waukulu kwambiri.
Mneneri amamuyesa chitsiru,
munthu wanzeru za kwa Mulungu ngati wamisala.
8 Mneneri pamodzi ndi Mulungu wanga
ndiwo alonda a Efereimu,
koma mneneri amutchera misampha mʼnjira zake zonse,
ndipo udani ukumudikira mʼnyumba ya Mulungu wake.
9 Iwo azama mu zachinyengo
monga masiku a Gibeya.
Mulungu adzakumbukira zolakwa zawo
ndipo adzawalanga chifukwa cha machimo awo.
10 “Pamene ndinamupeza Israeli
zinali ngati kupeza mphesa mʼchipululu.
Nditaona makolo anu,
zinali ngati ndikuona nkhuyu zoyambirira kupsa.
Koma atafika ku Baala Peori,
anadzipereka ku fano lija lochititsa manyazi
ndipo anakhala onyansa ngati chinthu chimene anachikondacho.
11 Ulemerero wa Efereimu udzawuluka ngati mbalame.
Sipadzakhalanso kubereka ana, kuyembekezera kapena kutenga pathupi.
12 Ngakhale atalera ana
ndidzachititsa kuti mwana aliyense amwalire.
Tsoka kwa anthuwo
pamene Ine ndidzawafulatira!
13 Ndaona Efereimu ngati Turo,
atadzalidwa pa nthaka ya chonde.
Koma Efereimu adzatsogolera
ana ake kuti akaphedwe.”
14 Inu Yehova, muwapatse.
Kodi mudzawapatsa chiyani?
Apatseni mimba yomangopita padera
ndi mawere owuma.
15 “Chifukwa cha zoyipa zawo zonse ku Giligala,
Ine ndinawada kumeneko.
Chifukwa cha machitidwe awo auchimo,
ndidzawapirikitsa mʼnyumba yanga.
Sindidzawakondanso;
atsogoleri awo onse ndi owukira.
16 Efereimu wathedwa,
mizu yake yauma
sakubalanso zipatso.
Ngakhale atabereka ana,
Ine ndidzapha ana awo okondedwawo.”
17 Mulungu wanga adzawakana
chifukwa sanamumvere Iye;
adzakhala oyendayenda pakati pa anthu a mitundu ina.
Malangizo pa Makhalidwe a Chikhristu
17 Tsono ine ndikukuwuzani izi, ndipo ndikunenetsa mwa Ambuye, kuti musayendenso monga amachitira anthu a mitundu ina potsata maganizo awo opanda pake. 18 Maganizo awo ndi odetsedwa, ndi osiyanitsidwa ndi moyo wa Mulungu chifukwa cha umbuli umene uli mwa iwo chifukwa cha kuwuma mtima kwawo. 19 Popeza sazindikiranso kanthu kalikonse, adzipereka okha kuti akhumbe zonyansa, kuti achite mtundu uliwonse wa zoyipa ndi zilakolako zosatha.
20 Koma inu simunadziwe Khristu mʼnjira yotere. 21 Zoonadi munamva za Iye ndipo munaphunzitsidwa mwa Iye molingana ndi choonadi chimene chili mwa Yesu. 22 Inu munaphunzitsidwa molingana ndi moyo wanu wakale, kuchotsa umunthu wakale, umene ukupitirira kuwonongeka ndi zilakolako zachinyengo; 23 kuti mukonzedwe mwatsopano mʼmitima mwanu; 24 ndi kuti muvale umunthu watsopano, wolengedwa kuti ufanane ndi Mulungu mu chilungamo chenicheni ndi chiyero.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.