Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 50:1-8

Salimo la Asafu.

50 Wamphamvuyo, Yehova Mulungu,
    akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi
    kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri
    Mulungu akuwala.
Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete;
    moto ukunyeketsa patsogolo pake,
    ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
Iye akuyitanitsa zamumlengalenga
    ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
Mundisonkhanitsire okhulupirika anga,
    amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake,
    pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.

Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula,
    iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa;
    ndine Mulungu, Mulungu wako.
Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako,
    kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.

Masalimo 50:22-23

22 “Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu
    kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
23 Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza,
    ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse
    chipulumutso cha Mulungu.”

Yesaya 9:8-17

Mkwiyo wa Yehova pa Israeli

Ambuye atumiza mawu otsutsa Yakobo;
    ndipo mawuwo agwera pa Israeli.
Anthu onse okhala mu
    Efereimu ndi okhala mu Samariya,
adzadziwa zimenezi.
    Iwo amayankhula modzikuza kuti,
10 “Ngakhale njerwa zagumuka,
    koma ife tidzamanga ndi miyala yosema.
Mitanda ya mkuyu yagwetsedwa,
    koma ife tidzayika mitanda ya mkungudza mʼmalo mwake.”
11 Koma Yehova wadzutsa adani kuti alimbane nawo
    ndipo wawafulumiza adani awo kuti amenyane nawo.
12 Asiriya ochokera kummawa ndi Afilisti ochokera kumadzulo ndipo
    ayasama pakamwa kuti adye a Israeli.

Komabe, mkwiyo wake sunawachokere,
    mkono wake uli chitambasulire.

13 Koma anthu sanabwerere kwa amene anawakantha uja,
    ngakhale kufunafuna Yehova Wamphamvuzonse.
14 Choncho Yehova adzadula mutu wa Israeli pamodzi ndi mchira womwe,
    nthambi ya kanjedza ndi bango lomwe tsiku limodzi;
15 mutuwo ndiye akuluakulu ndi olemekezeka,
    mchira ndiye aneneri ophunzitsa zabodza.
16 Amene amatsogolera anthuwa ndiwo amawasocheretsa,
    ndipo otsogoleredwa amatayika.
17 Nʼchifukwa chake Ambuye adzakondwera nawo achinyamata,
    ngakhale kuwachitira chifundo ana amasiye ndi akazi amasiye,
pakuti aliyense ndi wosapembedza Mulungu ndiponso ndi wochimwa ndipo
    aliyense amayankhula zopusa.

Komabe, mkwiyo wake sunawachokere,
    mkono wake uli chitambasulire.

Aroma 9:1-9

Chisankho Chopambana cha Mulungu

Ine ndikunena zoona mwa Khristu. Sindikunama ndipo chikumbumtima changa kudzera mwa Mzimu Woyera chikundichitira umboni. Ndili ndi chisoni chachikulu ndipo ndikumva kupwetekeka kosalekeza mu mtima mwanga. Pakuti ndikanafuna ine mwini nditatembereredwa ndi kuchotsedwa mwa Khristu chifukwa cha abale anga, amene ndi a mtundu wanga, anthu Aisraeli. Iwo anasankhidwa kukhala ana. Mulungu anawapatsa ulemerero, anachita nawo mapangano, kuwapatsa Malamulo, Nyumba yopembedzeramo ndi malonjezano ake. Awo ndi makolo athu. Kuchokera kwa iwo mʼthupi ndi kumene kunachokera makolo a Khristu Yesu amene ndi Mulungu wolamulira zinthu zonse, alemekezeke mpaka muyaya! Ameni.

Sikuti mawu a Mulungu analephera. Pakuti si onse obadwa mwa Israeli amene ndi Israeli. Kapena kuti ana ake chifukwa anachokera mwa Abrahamu. Koma zidzukulu zako zidzachokera mwa Isake. Kutanthauza kuti, si ana obadwa mʼthupi amene ndi ana a Mulungu koma ndi ana a lonjezano amene amatengedwa kukhala zidzukulu za Abrahamu. Pakuti Mulungu analonjeza ponena kuti, “Pa nthawi yake ngati yomwe ino chaka chamawa ndidzabweranso, ndipo Sara adzakhala ndi mwana wamwamuna.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.