Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 71:1-6

71 Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo;
    musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu,
    mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.
Mukhale thanthwe langa lothawirapo,
    kumene ine nditha kupita nthawi zonse;
lamulani kuti ndipulumuke,
    pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.
Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa,
    kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.

Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse,
    chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.
Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu;
    Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga,
    ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.

Yeremiya 6:20-30

20 Kodi pali phindu lanji ngakhale mubwere ndi lubani kuchokera ku Seba,
    kapena zonunkhira zina kuchokera ku dziko lakutali?
Nsembe zanu zopsereza Ine sindidzalandira;
    nsembe zanu sizindikondweretsa.”

21 Choncho Yehova akuti,

“Ndidzayika zokhumudwitsa pamaso pa anthu awa.
    Abambo ndi ana awo aamuna onse adzapunthwa ndi kugwa;
    anansi awo ndi abwenzi awo adzawonongeka.”

22 Yehova akunena kuti,

“Taonani, gulu lankhondo likubwera
    kuchokera kumpoto;
mtundu wa anthu amphamvu wanyamuka
    kuchokera kumathero a dziko lapansi.
23 Atenga mauta ndi mikondo;
    ndi anthu ankhanza ndi opanda chifundo.
Phokoso lawo lili ngati mkokomo wa nyanja.
    Akwera pa akavalo awo
ndipo akonzekera ngati anthu ankhondo,
    kudzakuthirani nkhondo anthu a ku Ziyoni.”

24 A ku Ziyoni akuti “Ife tamva mbiri yawo,
    ndipo manja anthu alefukiratu.
Nkhawa yatigwira,
    ndipo tikumva ululu ngati mayi pa nthawi yake yochira.
25 Musapite ku minda
    kapena kuyenda mʼmisewu,
pakuti mdani ali ndi lupanga,
    ndipo ponseponse anthu akuchita mantha.
26 Inu anthu anga, valani ziguduli
    ndipo gubudukani pa phulusa;
lirani mwamphamvu
    ngati munthu wolirira mwana wake mmodzi yekha,
pakuti mwadzidzidzi wowonongayo
    adzabwera kudzatipha.

27 “Iwe Yeremiya, ndakuyika kuti ukhale choyesera zitsulo.
    Uwayese anthu anga
monga ungayesere chitsulo
    kuti uwone makhalidwe awo.
28 Onsewo ali ndi khalidwe lokanika ndi lowukira
    ndipo akunka nanena zamiseche.
Iwo ndi olimba ngati mkuwa ndi chitsulo.
    Onse amangochita zoyipa zokhazokha.
29 Moto mu mvukuto ukuyaka kwambiri;
    mtovu watha kusungunuka ndi moto.
Koma ntchito yosungunulayo sikupindula
    chifukwa zoyipa sizikuchokapo.
30 Iwo ali ngati siliva wotayidwa,
    chifukwa Yehova wawakana.”

Machitidwe a Atumwi 17:1-9

Paulo ku Tesalonika

17 Atadutsa ku Amfipoli ndi Apoloniya, anafika ku Tesalonika, kumene kunali sunagoge ya Ayuda. Paulo, monga mwachizolowezi chake, analowa mʼsunagoge, ndipo anakambirana nawo Mawu a Mulungu kwa masabata atatu, kuwafotokozera ndi kuwatsimikizira kuti Khristu anayenera kufa ndi kuuka. Iye anati, “Yesu amene ndikukulalikirani ndiye Khristu.” Ena mwa Ayuda anakopeka mtima ndipo anatsatira Paulo ndi Sila, monganso linachitira gulu lalikulu la Agriki woopa Mulungu, pamodzi ndi amayi odziwika ambiri.

Koma Ayuda ena anachita nsanje; kotero anasonkhanitsa anthu akhalidwe loyipa ochokera pa msika ndipo napanga gulu nayambitsa chipolowe mu mzindawo. Anathamangira ku nyumba ya Yasoni kukafuna Paulo ndi Sila kuti awabweretse pa gulu la anthu. Koma atalephera kuwapeza, anakokera Yasoniyo ndi abale ena ku bwalo la akulu a mzindawo akufuwula kuti, “Anthu awa, Paulo ndi Sila, amene akhala akusokoneza dziko lonse lapansi, tsopano afikanso kuno. Yasoni ndiye anawalandira mʼnyumba mwake. Onsewa akuchita zotsutsana ndi malamulo a Kaisara pomanena kuti palinso mfumu ina, yotchedwa Yesu.” Atamva zimenezi, gulu la anthu ndi akulu a mzinda anavutika mu mtima. Iwo analipiritsa Yasoni ndi anzakewo ndipo anawamasula.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.