Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
4 Imvani mawu a Yehova, inu zidzukulu za Yakobo,
inu mafuko onse a Israeli.
5 Yehova akuti,
“Kodi makolo anu anandipeza nʼcholakwa chanji,
kuti andithawe?
Iwo anatsata milungu yachabechabe,
nawonso nʼkusanduka achabechabe.
6 Iwo sanafunse nʼkomwe kuti, ‘Kodi Yehova ali kuti,
amene anatitulutsa mʼdziko la Igupto
natitsogolera mʼchipululu mʼdziko lowuma
ndi lokumbikakumbika,
mʼdziko lopanda mvula ndi la mdima,
dziko limene munthu sadutsamo ndipo simukhala munthu aliyense?’
7 Ndinakufikitsani ku dziko lachonde
kuti mudye zipatso zake ndi zabwino zake zina.
Koma inu mutafika munaliyipitsa dziko langa
ndi kusandutsa cholowa changa kukhala chonyansa.
8 Ansembe nawonso sanafunse kuti,
‘Yehova ali kuti?’
Iwo amene amaphunzitsa malamulo sanandidziwe;
atsogoleri anandiwukira.
Aneneri ankanenera mʼdzina la Baala,
ndi kutsatira mafano achabechabe.
9 “Chifukwa chake Ine ndidzakuyimbaninso mlandu,”
akutero Yehova.
“Ndipo ndidzayimbanso mlandu zidzukulu zanu.
10 Pitani kumadzulo ku chilumba cha Kitimu, ndipo mukaone,
tumizani anthu ku Kedara kuti akafufuze bwino;
ndipo muona kuti zinthu zoterezi sizinachitikepo nʼkale lomwe:
11 Kodi ulipo mtundu wa anthu uliwonse umene unasinthapo milungu yake?
(Ngakhale kuti si milungu nʼkomwe).
Koma anthu anga asinthitsa Mulungu wawo waulemerero
ndi mafano achabechabe.
12 Inu mayiko akumwamba, dabwani ndi zimenezi,
ndipo njenjemerani ndi mantha aakulu,”
akutero Yehova.
13 “Popeza anthu anga achita machimo awiri:
Andisiya Ine
kasupe wa madzi a moyo,
ndi kukadzikumbira zitsime zawo,
zitsime zongʼaluka, zomwe sizingathe kusunga madzi.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu.
81 Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu;
Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
10 Ine ndine Yehova Mulungu wanu,
amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto.
Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.
11 “Koma anthu anga sanandimvere;
Israeli sanandigonjere.
12 Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo
kuti atsate zimene ankafuna.
13 “Anthu anga akanangondimvera,
Israeli akanatsatira njira zanga,
14 nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo
ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
15 Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake,
ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
16 Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri;
ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”
Mawu Achilimbikitso Otsiriza
13 Pitirizani kukondana monga abale. 2 Musayiwale kusamalira alendo, pakuti pochita zimenezi anthu ena anasamalira angelo amene samawadziwa. 3 Muzikumbukira amene ali mʼndende ngati kuti inunso ndi omangidwa, ndiponso amene akusautsidwa ngati inunso mukuvutika.
4 Ukwati muziwulemekeza nonse, ndipo mwamuna ndi mkazi azikhala wokhulupirika, pakuti anthu adama ndi achigololo Mulungu adzawalanga. 5 Mtima wanu usakonde ndalama koma mukhutitsidwe ndi zimene muli nazo, chifukwa Mulungu anati,
“Sadzakusiyani,
kapena kukutayani konse.”
6 Kotero ife tikunena molimba mtima kuti,
“Ambuye ndiye mthandizi wanga;
sindidzachita mantha. Munthu angandichitenji ine?”
7 Muzikumbukira atsogoleri anu, amene amakulalikirani Mawu a Mulungu. Ganizirani zamoyo wawo ndipo tsatirani chikhulupiriro chawo. 8 Yesu Khristu ndi yemweyo dzulo, lero ndi kunthawi zonse.
15 Tsono, tiyeni kudzera mwa Yesu tipereke nsembe zachiyamiko kwa Mulungu osalekeza, chipatso cha milomo imene imavomereza dzina lake. 16 Ndipo musayiwale kumachita zabwino ndi kuthandiza ena, pakuti Mulungu amakondwera ndi nsembe zotere.
Yesu Mʼnyumba ya Mfarisi
14 Pa tsiku lina la Sabata, Yesu atapita kukadya ku nyumba ya Mfarisi wodziwika, Afarisi anamulonda mosamalitsa.
Kudzichepetsa ndi Kulandira Ulemu
7 Iye ataona momwe alendo amasankhira malo aulemu pa tebulo, Iye anawawuza fanizo ili: 8 “Pamene wina wakuyitanani ku phwando la ukwati, musakhale pa malo aulemu ayi, chifukwa mwina anayitananso munthu wina wolemekezeka kuposa inu. 9 Ngati zitatero, ndiye kuti munthu uja amene anakuyitani inu nonse awiri adzakuwuzani kuti, ‘Mupatseni munthu uyu malo anu.’ Pamenepo inu mudzachita manyazi, pokakhala malo wotsika. 10 Koma akakuyitanani, khalani pa malo otsika, kuti amene anakuyitanani uja adzakuwuzeni kuti, ‘Bwenzi, bwera udzakhale pa malo aulemu pano.’ Pamenepo inu mudzalandira ulemu pamaso pa alendo anzanu onse. 11 Pakuti aliyense wodzikuza adzamuchepetsa, ndipo aliyense wodzichepetsa adzamukweza.”
12 Kenaka Yesu anati kwa mwini malo uja, “Ukakonza chakudya chamasana kapena chamadzulo, usamayitane abwenzi ako, abale ako, anthu afuko lako kapena anzako achuma; ngati iwe utero, iwo adzakuyitananso, choncho udzalandiriratu mphotho yako. 13 Koma ukakonza phwando, itana anthu osauka, ofa ziwalo, olumala ndi osaona. 14 Pamenepo udzakhala wodala, chifukwa iwo sangakubwezere kanthu, koma Mulungu ndiye adzakubwezera pa chiukitso cha olungama.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.