Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere.
60 Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza.
Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
2 Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba,
konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
3 Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto;
inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.
4 Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera
kuti tisonkhanireko pothawa uta.
5 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja,
kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
6 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika:
“Mwakupambana ndidzagawa Sekemu
ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
7 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso;
Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera,
Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
8 Mowabu ndi mbale yanga yosambira,
pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga,
pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”
9 Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa?
Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
10 Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife
ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
11 Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu,
pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
12 Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano
ndipo tidzapondaponda adani athu.
Tchimo la Israeli
12 Efereimu wandizungulira ndi mabodza,
nyumba ya Israeli yandizungulira ndi chinyengo.
Ndipo Yuda wawukira Mulungu,
wawukira ngakhale Woyerayo amene ndi wokhulupirika.
12 Efereimu amadya mpweya;
tsiku lonse amasaka mphepo ya kummawa
ndipo amachulukitsa mabodza ndi chiwawa.
Amachita mgwirizano ndi Asiriya
ndipo amatumiza mphatso za mafuta a olivi ku Igupto.
2 Yehova akuyimba mlandu Yuda;
Iye adzalanga Yakobo molingana ndi makhalidwe ake,
adzamulanga molingana ndi ntchito zake.
3 Akali mʼmimba mwa amayi ake, Yakobo anagwira chidendene cha mʼbale wake;
iye atakula analimbana ndi Mulungu.
4 Yakobo analimbana ndi mngelo ndipo anapambana;
analira napempha kuti amukomere mtima.
Mulungu anakumana naye ku Beteli
ndipo anayankhula naye kumeneko,
5 Yehova Mulungu Wamphamvuzonse,
Yehova ndiye dzina lake lotchuka!
6 Koma inu muyenera kubwerera kwa Mulungu wanu;
pitirizani chikondi ndi chiweruzo cholungama,
ndipo muzidikira Mulungu wanu nthawi zonse.
7 Munthu wamalonda amagwiritsa ntchito masikelo achinyengo;
iyeyo amakonda kubera anthu.
8 Efereimu amadzitama ponena kuti,
“Ndine wolemera kwambiri; ndili ndi chuma chambiri.
Palibe amene angandiloze chala
chifukwa cha kulemera kwanga.”
9 “Ine ndine Yehova Mulungu wako
amene ndinakutulutsa mu Igupto.
Ndidzakukhazikaninso mʼmatenti,
monga munkachitira masiku aja pa nthawi ya zikondwerero zanu.
10 Ndinayankhula ndi aneneri,
ndinawaonetsa masomphenya ambiri,
ndipo ndinawawuza mafanizo kudzera mwa iwo.”
11 Kodi Giliyadi ndi woyipa?
Anthu ake ndi achabechabe!
Kodi amapereka nsembe za ngʼombe zazimuna ku Giligala?
Maguwa awo ansembe adzakhala ngati milu ya miyala
mʼmunda molimidwa.
12 Yakobo anathawira ku dziko la Aramu,
Israeli anagwira ntchito kuti apeze mkazi,
ndipo anaweta nkhosa kuti akwatire mkaziyo.
13 Yehova anagwiritsa ntchito mneneri kuti atulutse Israeli mu Igupto;
kudzera mwa mneneriyo Iye anawasamalira.
14 Koma Efereimu wamukwiyitsa kwambiri.
Nʼchifukwa chake Yehova adzawalanga ndi imfa.
Adzawalanga chifukwa anamuchititsa manyazi kwambiri.
Malangizo a Moyo wa Mʼbanja la Chikhristu
18 Inu akazi, gonjerani amuna anu, monga kuyenera mwa Ambuye.
19 Inu amuna, kondani akazi anu ndipo musawapsere mtima.
20 Inu ana, mverani makolo anu mu zonse pakuti izi zimakondweretsa Ambuye.
21 Inu abambo, musakwiyitse ana anu, kuti angataye mtima.
22 Inu antchito, mverani mabwana anu mu zonse, ndipo muzichita zimenezi osati nthawi yokhayo imene akukuonani kuti akukondeni, koma muzichite moona mtima ndi mopereka ulemu kwa Ambuye. 23 Chilichonse mungachite, muchite ndi mtima wanu onse, monga mmene mungagwirire ntchito ya Ambuye osati ya anthu. 24 Inu mukudziwa kuti mudzalandira mphotho monga cholowa kuchokera kwa Ambuye. Ndi Ambuye Khristu amene mukumutumikira. 25 Aliyense amene amachita zolakwa adzalandira malipiro molingana ndi kulakwa kwake, ndipo palibe tsankho.
4 Mabwana, antchito anu muzikhala nawo mwachilungamo ndi moyenera, podziwa kuti nanunso muli nawo Ambuye anu mmwamba.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.