Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
11 Mwa Yehova ine ndimathawiramo.
Nanga mungathe bwanji kunena kwa ine kuti,
“Thawira ku phiri lako ngati mbalame.
2 Pakuti taona oyipa akunga mauta awo;
ayika bwino mivi yawo pa zingwe za uta,
pobisala pawo kuti alase
olungama mtima.
3 Tsono ngati maziko awonongeka,
olungama angachite chiyani?”
4 Yehova ali mʼNyumba yake yoyera;
Yehova ali pa mpando wake waufumu kumwamba.
Iye amayangʼanitsitsa ana a anthu;
maso ake amawayesa.
5 Yehova amayesa olungama,
koma moyo wake umadana ndi oyipa,
amene amakonda zachiwawa.
6 Iye adzakhuthulira pa oyipa
makala amoto ndi sulufule woyaka;
mphepo yotentha idzakhala yowayenera.
7 Pakuti Yehova ndi wolungama,
Iye amakonda chilungamo;
ndipo anthu olungama adzaona nkhope yake.
14 Koma otsala onse akufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe;
anthu akumadzulo akutamanda ukulu wa Yehova.
15 Nʼchifukwa chake inu akummawa, tamandani Yehova;
ndi inu okhala mʼmphepete mwa nyanja kwezani dzina la Yehova, Mulungu wa Israeli.
16 Kuchokera kumalekezero a dziko lapansi tikumva kuyimba kotamanda
“Wolungamayo.”
Koma ine ndinati, “Ndatheratu, ndatheratu!
Tsoka kwa ine!
Anthu achinyengo akupitirizabe kuchita zachinyengo,
inde chinyengo chawo chikunkerankera mʼtsogolo.”
17 Inu anthu adziko lapansi, zoopsa, dzenje
ndi msampha zikukudikirani.
18 Aliyense wothawa phokoso la zoopsa
adzagwa mʼdzenje;
ndipo aliyense wotuluka mʼdzenjemo
adzakodwa ndi msampha.
Zitseko zakumwamba zatsekulidwa,
ndipo maziko a dziko lapansi agwedezeka.
19 Dziko lapansi lathyokathyoka,
ndipo lagawika pakati,
dziko lapansi lagwedezeka kotheratu.
20 Dziko lapansi likudzandira ngati munthu woledzera
likugwedezeka ndi mphepo ngati chisimba;
lalemedwa ndi machimo ake.
Lidzagwa ndipo silidzadzukanso.
21 Tsiku limenelo Yehova adzalanga
amphamvu a kumwamba
ndiponso mafumu apansi pano.
22 Mulungu adzawasonkhanitsa pamodzi
ngati amʼndende amene ali mʼdzenje.
Adzawatsekera mʼndende
ndipo adzalangidwa patapita nthawi yayitali.
23 Mwezi udzanyazitsidwa, dzuwa lidzachita manyazi;
pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzakhala mfumu ndipo adzalamulira;
pa Phiri la Ziyoni ndi ku Yerusalemu,
ndipo adzaonetsa ulemerero wake pamaso pa akuluakulu.
Wantchito Wokhulupirika ndi Wosakhulupirika
41 Petro anafunsa kuti, “Kodi mukunena fanizoli kwa ife, kapena kwa aliyense?”
42 Ambuye anayankha kuti, “Kodi tsono woyangʼanira wokhulupirika ndi wanzeru ndani? Kodi ndi amene mbuye wake wamuyika kukhala oyangʼanira antchito ake kuti aziwapatsa ndalama yachakudya pa nthawi yake yoyenera? 43 Zidzamukhalira bwino wantchito amene mbuye wake adzamupeza akuchita zimene pamene iye abwera. 44 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti adzamuyika kukhala woyangʼanira katundu wake yense. 45 Koma tiyerekeze kuti wantchitoyo aziganiza mu mtima mwake kuti, ‘Bwana wanga akuchedwa kwambiri kubwera,’ ndipo kenaka ndi kuyamba kumenya antchito aamuna ndi aakazi ndi kudya, kumwa ndi kuledzera. 46 Mbuye wake adzabwera tsiku limene iye sakumuyembekezera ndi ora limene iye sakudziwa. Iye adzamulanga ndi kumusiya kumalo kumene kuli osakhulupirira.
47 “Wantchito amene amadziwa chifuniro cha mbuye wake koma wosakonzeka kapena wosachita chimene mbuye wake akufuna adzakwapulidwa zikwapu zambiri. 48 Koma wantchito amene sadziwa koma nʼkuchita zinthu zoyenera chilango, adzakwapulidwa zikwapu zochepa. Aliyense amene anapatsidwa zambiri, adzayenera kubwezanso zambiri; ndipo amene anamusungitsa zambiri, adzamulamula kuti abweze zambirinso.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.