Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
BUKU LACHISANU
Masalimo 107–150
107 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;
pakuti chikondi chake ndi chosatha.
2 Owomboledwa a Yehova anene zimenezi
amene Iyeyo anawawombola mʼdzanja la mdani,
3 iwo amene anawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko,
kuchokera kumadzulo ndi kummawa, kuchokera kumpoto ndi kummwera.
4 Ena anayendayenda mʼchipululu mopanda kanthu,
osapeza njira yopitira ku mzinda kumene akanakakhazikikako.
5 Iwo anamva njala ndi ludzu,
ndipo miyoyo yawo inafowokeratu.
6 Pamenepo analirira Yehova mʼmavuto awo
ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.
7 Iye anawatsogolera mʼnjira yowongoka
kupita ku mzinda umene anakakhazikikako.
8 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
ndi chifukwa cha machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,
9 pakuti Iye wapha ludzu la munthu womva ludzu
ndipo wakhutitsa wanjala ndi zinthu zabwino.
43 Aliyense wanzeru asamalitse zinthu zimenezi
ndi kuganizira za chikondi chachikulu cha Yehova.
10 Israeli anali mpesa wotambalala;
anabereka zipatso zambiri.
Pamene zipatso zawo zinanka zichuluka,
anawonjezera kumanga maguwa ansembe.
Pamene dziko lake linkatukuka,
anakongoletsa miyala yake yopatulika.
2 Mtima wawo ndi wonyenga
ndipo tsopano ayenera kulangidwa chifukwa cha kulakwa kwawo.
Yehova adzagumula maguwa awo ansembe
ndi kuwononga miyala yawo yopatulika.
3 Pamenepo anthuwo adzanena kuti, “Ife tilibe mfumu
chifukwa sitinaope Yehova.
Koma ngakhale tikanakhala ndi mfumu,
kodi mfumuyo ikanatichitira chiyani?”
4 Mafumu amalonjeza zambiri,
amalumbira zabodza
pochita mapangano.
Kotero maweruzo amaphuka
ngati zitsamba zakupha mʼmunda umene walimidwa.
5 Anthu amene amakhala mu Samariya akuchita mantha
chifukwa cha fano la mwana wangʼombe ku Beti-Aveni.
Anthu ake adzalirira fanolo,
chimodzimodzinso ansembe ake adamawo,
amene anakondwera ndi kukongola kwake,
chifukwa lachotsedwa pakati pawo ndi kupita ku ukapolo.
6 Fanolo lidzatengedwa kupita ku Asiriya
ngati mphatso kwa mfumu yayikulu.
Efereimu adzachititsidwa manyazi
chifukwa cha mafano ake amitengo.
7 Samariya ndi mfumu yake adzatengedwa kupita kutali
ngati kanthambi koyenda pa madzi.
8 Malo opembedzerako mafano a ku Aveni adzawonongedwa.
Ili ndiye tchimo la Israeli.
Minga ndi mitungwi zidzamera
ndi kuphimba maguwa awo ansembe.
Kenaka anthu adzawuza mapiri kuti, “Tiphimbeni!”
ndipo adzawuza zitunda kuti, “Tigwereni!”
9 “Iwe Israeli, wachimwa kuyambira mʼmasiku a Gibeya,
ndipo wakhala uli pomwepo.
Kodi nkhondo sinagonjetse anthu
ochita zoyipa ku Gibeya?
10 Pamene ndifunire, ndidzalanga anthuwo;
mitundu ya anthu idzasonkhanitsidwa kudzalimbana nawo,
kuwayika mʼndende chifukwa cha uchimo wawo waukulu.
11 Efereimu ndi mwana wangʼombe wamkazi wophunzitsidwa
amene amakonda kupuntha tirigu,
choncho Ine ndidzayika goli
mʼkhosi lake lokongolalo.
Ndidzasenzetsa Efereimu goli,
Yuda ayenera kulima,
ndipo Yakobo ayenera kutipula.
12 Mufese nokha chilungamo
ndipo mudzakolola chipatso cha chikondi changa chosasinthika.
Ndipo tipulani munda wanu wosalimidwawo;
pakuti ino ndi nthawi yofunafuna Yehova,
mpaka Iye atabwera
kudzakugwetserani mivumbi ya chilungamo.
13 Koma inu munadzala zolakwa,
mwakolola zoyipa;
mwadya chipatso cha chinyengo.
Chifukwa mumadalira mphamvu zanu
ndiponso ankhondo anu ochulukawo,
14 phokoso lankhondo lidzamveka pakati pa anthu anga
kotero kuti malinga anu onse adzawonongeka,
monga momwe Salimani anawonongera Beti-Aribeli pa nthawi ya nkhondo;
pamene anapha amayi pamodzi ndi ana awo omwe.
15 Momwemonso zidzakuchitikira, iwe Beteli
chifukwa kuyipa kwako ndi kwakukulu.
Tsiku limeneli likadzafika,
mfumu ya Israeli idzawonongedwa kwathunthu.
Munthu Wachuma ndi Ufumu wa Mulungu
17 Yesu atanyamuka, munthu wina anamuthamangira nagwa mogwada pamaso pake. Iye anafunsa kuti, “Aphunzitsi abwino, ndichite chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?”
18 Yesu anamufunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani ukunditchula wabwino? Palibe wabwino koma Mulungu yekha. 19 Iwe umadziwa malamulo: ‘Usaphe, usachite chigololo, usabe, usapereke umboni wonama, usachite chinyengo, lemekeza abambo ndi amayi ako.’ ”
20 Iye anati, “Aphunzitsi zonsezi ndinazisunga kuyambira ndili mnyamata.”
21 Yesu anamuyangʼana ndi kumukonda nati, “Ukusowa chinthu chimodzi. Pita, kagulitse zonse zimene uli nazo ndipo kapereke kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Ndipo ukabwere ndi kunditsata Ine.”
22 Pa chifukwa ichi nkhope yake inagwa. Anachoka ali wachisoni, chifukwa anali ndi chuma chambiri.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.