Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 81:1

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu.

81 Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu;
    Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!

Masalimo 81:10-16

10 Ine ndine Yehova Mulungu wanu,
    amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto.
    Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.

11 “Koma anthu anga sanandimvere;
    Israeli sanandigonjere.
12 Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo
    kuti atsate zimene ankafuna.

13 “Anthu anga akanangondimvera,
    Israeli akanatsatira njira zanga,
14 nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo
    ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
15 Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake,
    ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
16 Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri;
    ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”

Yeremiya 2:1-3

Aisraeli Asiya Mulungu

Yehova anandiwuza kuti, “Pita ukalengeze kwa anthu a ku Yerusalemu kuti Yehova akuti,

“ ‘Ine ndikukumbukira mmene umakhulupirikira pa unyamata wako,
    mmene unkandikondera ngati momwe amachitira mkwatibwi,
mmene unkanditsata mʼchipululu muja;
    mʼdziko losadzalamo kanthu.
Israeli anali wopatulika wa Yehova,
    anali ngati zipatso zake zoyamba kucha pa nthawi yokolola;
onse amene anamuzunza anapezeka kuti ndi olakwa
    ndipo mavuto anawagwera,’ ”
            akutero Yehova.

Yeremiya 2:14-22

14 Israeli si wantchito kapena kapolo wobadwira mʼnyumba, ayi.
    Nanga nʼchifukwa chiyani amuwononga chotere?
15 Adani ake abangulira
    ndi kumuopseza ngati mikango.
Dziko lake analisandutsa bwinja;
    mizinda yake anayitentha popanda wokhalamo.
16 Ndiponso Aigupto a ku Mefisi ndi a ku Tapanesi
    akuphwanyani mitu.
17 Zimenezitu zakuchitikirani
    chifukwa munasiya Yehova Mulungu wanu
    pamene Iye ankakutsogolerani pa njira yanu?
18 Tsopano mudzapindula chiyani mukapita ku Igupto,
    kukamwa madzi a mu Sihori?
Ndipo mudzapindulanji mukapita ku Asiriya,
    kukamwa madzi a mu mtsinje wa Yufurate?
19 Kuyipa kwanuko kudzakulangani;
    kubwerera mʼmbuyo kwanuko kudzakutsutsani.
Tsono ganizirani bwino,
    popeza ndi chinthu choyipa
kundisiya Ine Yehova Mulungu wanu;
    ndi chinthu chowawa ndithu kusandiopa Ine Mulungu wanu.
            Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.

20 “Kuyambira kalekale inu munathyola goli lanu
    ndi kudula msinga zanu;
    munanena kuti, ‘Sitidzakutumikirani!’
Ndithudi, inu mwakhala ngati mkazi wachiwerewere.
    Mukupembedza milungu ina pa phiri lililonse lalitali
    ndiponso pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
21 Ine ndinakudzala iwe ngati mtengo wampesa wosankhika;
    unali mpesa wabwino kwambiri ndi wodalirika.
Nanga nʼchifukwa chiyani wasanduka mpesa
    wachabechabe wonga wa kutchire?
22 Ngakhale utasamba ndi soda
    kapena kusambira sopo wambiri,
    kuthimbirira kwa machimo ako kumaonekabe pamaso panga,”
            akutero Ambuye Yehova.

Mateyu 20:20-28

Pempho la Mkazi wa Zebedayo

20 Amayi a ana a Zebedayo anabwera ndi ana ake kwa Yesu, nagwada pansi namupempha Iye.

21 Yesu anawafunsa kuti, “Mukufuna chiyani?”

Amayiwo anati, “Lolani kuti ana anga awiriwa adzakhale mmodzi ku dzanja lanu lamanja ndi wina ku dzanja lanu lamazere mu ufumu wanu.”

22 Yesu anawawuza kuti, “Simukudziwa chimene mukupempha. Kodi mungathe kumwera chikho chimene ndidzamwera Ine?”

Iwo anayankha nati, “Inde tingathe.”

23 Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi mudzamwera chikho changa, koma kuti mudzakhale ku dzanja langa lamanja kapena lamazere si kwa Ine kupereka. Malo awa ndi a iwo amene anakonzeredweratu ndi Atate anga.”

24 Ophunzira khumi aja, anawapsera mtima abale awiriwo. 25 Yesu anawayitana onse pamodzi nati, “Mukudziwa kuti olamulira a mitundu ina ali ndi mphamvu pa iwo, ndipo akuluakulu awo amawalamulira. 26 Siziyenera kutero ndi inu. Mʼmalo mwake, aliyense amene akufuna kukhala wamkulu pakati panu akhale wotumikira wanu. 27 Ndipo aliyense amene akufuna kukhala woyamba akhale kapolo wanu. 28 Momwenso Mwana wa Munthu sanabwere kudzatumikiridwa, koma kudzatumikira, ndi kupereka moyo wake kukhala dipo la anthu ambiri.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.