Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 71:1-6

71 Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo;
    musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu,
    mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.
Mukhale thanthwe langa lothawirapo,
    kumene ine nditha kupita nthawi zonse;
lamulani kuti ndipulumuke,
    pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.
Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa,
    kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.

Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse,
    chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.
Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu;
    Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga,
    ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.

Yeremiya 6:1-19

Kuzingidwa kwa Yerusalemu

“Thawani, inu anthu a ku Benjamini!
    Tulukani mu Yerusalemu!
Lizani lipenga ku Tekowa!
    Kwezani mbendera ku Beti-Hakeremu!
Pakuti tsoka lalikulu likubwera kuchokera kumpoto,
    ndipo chiwonongekocho nʼchachikulu.
Kodi mzinda wa Ziyoni suli ngati msipu wokongola kwambiri,
    kumene abusa amafikako ndi ziweto zawo?
Abusa ndi nkhosa zawo adzabwera kudzalimbana nawo;
    adzamanga matenti awo mowuzinga,
    ndipo aliyense adzakhazika anthu ake pamalo pake.”

Adzanena kuti, “Konzekani kuwuthira nkhondo mzindawo!
    Nyamukani, kuti tiwuthire nkhondo mzindawu masana ano.
Koma tili ndi tsoka, dzuwa lapendeka,
    ndipo zithunzithunzi za kumadzulo zikunka zitalika.
Tsono nyamukani kuti tiwuthire nkhondo mzindawu usiku uno
    ndi kuwononga malinga ake!”

Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Dulani mitengo
    ndipo mumange mitumbira yankhondo kulimbana ndi Yerusalemu.
Mzinda umenewu uyenera kulangidwa;
    wadzaza ndi kuponderezana.
Monga momwe chitsime chimatulutsira madzi
    ndi mmenenso Yerusalemu amatulutsira zoyipa zake.
Chiwawa ndi chiwonongeko ndi zomwe zimamveka mu mzindamo;
    nthenda yake ndi mabala ake ndimaziona nthawi zonse.
Iwe Yerusalemu, tengapo phunziro,
    kuopa kuti chikondi changa pa iwe chingakuchokere
ndi kusandutsa dziko lako kukhala bwinja
    mopanda munthu wokhalamo.”

Yehova Wamphamvuzonse anandiwuza kuti,

“Adani adzawakunkha ndithu anthu otsala a Israeli,
    monga momwe amachitira populula mphesa.
Tsono iwe yesetsa kupulumutsa amene ungathe
    monga mmene amachitira munthu wokolola mphesa.”

10 Kodi ndiyankhule ndi yani ndi kumuchenjeza?
    Ndinene mawu ochenjeza kwa yani kuti amve?
Makutu awo ndi otsekeka
    kotero kuti sangathe kumva.
Mawu a Yehova ndi onyansa kwa iwo;
    sasangalatsidwa nawo.
11 Koma ine ndadzazidwa ndi mkwiyo wa Yehova,
    ndipo ndatopa ndi kusunga mkwiyo wa Yehova.

Yehova anandiwuza kuti, “Tsono ndidzawutulutsira mkwiyo umenewu pa ana oyenda mʼmisewu
    ndi pa achinyamata amene asonkhana pamodzi;
pakutinso mwamuna ndi mkazi wake adzatengedwa,
    pamodzi ndi okalamba amene ali ndi zaka zochuluka.
12 Nyumba zawo adzazipereka kwa ena,
    pamodzi ndi minda yawo ndi akazi awo.
Ndidzatambasula dzanja langa kukantha
    anthu okhala mʼdzikomo,”
            akutero Yehova.
13 “Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu,
    onse ali ndi dyera lofuna kupeza phindu mwa kuba;
aneneri pamodzi ndi ansembe omwe,
    onse amachita zachinyengo.
14 Amapoletsa zilonda za anthu anga
    pamwamba pokha.
Iwo amanena kuti, ‘Mtendere, mtendere,’
    pamene palibe mtendere.
15 Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazo?
    Ayi, sachita manyazi ndi pangʼono pomwe;
    sadziwa ndi kugwetsa nkhope komwe.
Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale;
    adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalange,”
            akutero Yehova.

16 Yehova akuti,

“Imani pa mphambano ndipo mupenye;
    kumeneko ndiye kuli njira zakale,
funsani kumene kuli njira yabwino. Yendani mʼmenemo,
    ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu.
    Koma inu munati, ‘Ife sitidzayenda njira imeneyo.’
17 Ine ndinakupatsani alonda oti akuyangʼanireni
    ndipo ndinati, ‘Imvani kulira kwa lipenga!’
    koma inu munati, ‘Sitidzamvera.’
18 Nʼchifukwa chake imvani, inu anthu a mitundu ina;
    yangʼanitsitsani, inu amene mwasonkhana pano,
    chimene chidzawachitikire anthuwo.
19 Imvani, inu anthu okhala pa dziko lapansi,
ndikubweretsa masautso pa anthu awa.
    Zimenezi ndi mphotho ya ntchito zawo.
Iwowa sanamvere mawu anga
    ndipo anakana lamulo langa.

Ahebri 12:3-17

Muzilingalira za Iye amene anapirira udani waukulu chotere wochokera kwa anthu ochimwa, kuti musafowoke ndi kutaya mtima. Polimbana ndi uchimo, simunafike mpaka pokhetsa magazi.

Mulungu Amalanga Ana ake

Kodi mwayiwala mawu olimbitsa mtima aja, amene Mulungu anayankhula kwa inu ngati ana ake? Mawuwo ndi awa:

“Mwana wanga, usapeputse kulanga kwa Ambuye
    ndipo usataye mtima pamene akukudzudzula.
Chifukwa Ambuye amadzudzula amene amawakonda
    ndipo amalanga aliyense amene amamulandira.”

Pamene mukupirira masautso monga chilango, Mulungu achitira inu monga ana ake. Kodi ndi mwana wotani amene abambo ake samulanga? Ngati inu simulangidwa, komatu aliyense amalangidwa, ndiye kuti sindinu ana enieni koma amʼchigololo. Komanso, tonsefe tinali ndi abambo athu otibala amene amatilanga ndipo timawapatsa ulemu. Nanga kodi sitidzagonjera Atate a mizimu yathu kuti tikhale ndi moyo? 10 Abambo athu ankatilanga kwa kanthawi kochepa monga amaonera kufunika kwake, koma Mulungu amatilanga kuti tipindule, kuti tikhale oyera mtima. 11 Palibe chilango chimene chimaoneka kuti ndi chabwino pa nthawiyo, komatu chowawa. Koma pambuyo pake, chimabweretsa chipatso chachilungamo ndi mtendere kwa iwo amene aleredwa mwa njira imeneyi.

12 Nʼchifukwa chake limbitsani manja anu otopa ndi mawondo anu ogowoka. 13 Muziyenda mʼnjira zowongoka, kuti iwo amene akukutsatirani ngakhale ndi olumala ndi ofowoka asapunthwe ndi kugwa koma adzilimbikitsidwa.

Chenjezo kwa Okana Mulungu

14 Yesetsani kukhala pa mtendere ndi anthu onse ndi kukhala oyera mtima, pakuti popanda chiyero palibe ndi mmodzi yemwe adzaona Ambuye. 15 Yangʼanitsitsani kuti wina aliyense asachiphonye chisomo cha Mulungu ndiponso kuti pasaphuke muzu wamkwiyo umene udzabweretsa mavuto ndi kudetsa ambiri. 16 Yangʼanitsitsani kuti pasakhale wina wachigololo. Kapena wosapembedza ngati Esau, amene chifukwa cha chakudya cha kamodzi kokha anagulitsa ukulu wake. 17 Monga inu mukudziwa, pambuyo pake pamene anafuna kuti adalitsidwe anakanidwa. Sanapezenso mpata woti asinthe maganizo, ngakhale anafuna madalitsowo ndi misozi.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.