Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 11

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

11 Mwa Yehova ine ndimathawiramo.
    Nanga mungathe bwanji kunena kwa ine kuti,
    “Thawira ku phiri lako ngati mbalame.
Pakuti taona oyipa akunga mauta awo;
    ayika bwino mivi yawo pa zingwe za uta,
pobisala pawo kuti alase
    olungama mtima.
Tsono ngati maziko awonongeka,
    olungama angachite chiyani?”

Yehova ali mʼNyumba yake yoyera;
    Yehova ali pa mpando wake waufumu kumwamba.
Iye amayangʼanitsitsa ana a anthu;
    maso ake amawayesa.
Yehova amayesa olungama,
    koma moyo wake umadana ndi oyipa,
    amene amakonda zachiwawa.
Iye adzakhuthulira pa oyipa
    makala amoto ndi sulufule woyaka;
    mphepo yotentha idzakhala yowayenera.

Pakuti Yehova ndi wolungama,
    Iye amakonda chilungamo;
    ndipo anthu olungama adzaona nkhope yake.

Yesaya 24:1-13

Chilango cha Yehova pa Dziko Lapansi

24 Taonani, Yehova adzawononga dziko lapansi
    ndi kulisandutsa chipululu;
Iye adzasakaza maonekedwe ake
    ndi kumwaza anthu ake onse.
Aliyense zidzamuchitikira mofanana:
    wansembe chimodzimodzi munthu wamba,
    antchito aamuna mofanananso ndi ambuye awo aamuna,
    antchito aakazi chimodzimodzi ambuye awo aakazi,
    wogula chimodzimodzi wogulitsa,
    wobwereka chimodzimodzi wobwereketsa,
    okongola chimodzimodzi okongoza.
Dziko lapansi lidzawonongedwa kwathunthu
    ndi kusakazikiratu.
            Yehova wanena mawu awa.

Dziko lapansi likulira ndipo likufota,
    dziko lonse likuvutika ndipo likuwuma,
    anthu omveka a dziko lapansi akuvutika.
Anthu ayipitsa dziko lapansi;
    posamvera malangizo ake;
pophwanya mawu ake
    ndi pangano lake lamuyaya.
Nʼchifukwa chake matemberero akuwononga dziko lapansi;
    anthu a mʼdzikomo akuzunzika chifukwa cha kulakwa kwawo,
iwo asakazika
    ndipo atsala ochepa okha.
Vinyo watsopano watha ndipo mphesa zikufota;
    onse okonda zosangalatsa ali ndi chisoni.
Kulira kokometsera kwa matambolini kwatha,
    phokoso la anthu osangalala latha,
    zeze wosangalatsa wati zii.
Anthu sadzayimbanso akumwa vinyo;
    akadzamwa zaukali zidzakhala zowawa mʼkamwa mwawo.
10 Mzinda wachisokonezo uja wawonongeka;
    nyumba iliyonse yatsekedwa.
11 Anthu akulira mʼmisewu kufuna vinyo;
    chimwemwe chonse chatheratu,
    palibenso chisangalalo pa dziko lapansi.
12 Mzinda wasanduka bwinja
    zipata zake zagumuka.
13 Zimenezi ndizo zidzachitikire mitundu yonse ya dziko lapansi
    ndiponso pakati pa mitundu ya anthu.
Zidzakhala ngati pamene mitengo ya olivi yayoyoledwa,
    kapena ngati nthawi ya kunkha la mphesa atatsiriza kukolola.

Ahebri 11:17-28

17 Ndi chikhulupiriro Abrahamu, Mulungu atamuyesa, anapereka Isake ngati nsembe. Ngakhale anali munthu woti Mulungu anamulonjeza, anakhala wokonzeka kupereka nsembe mwana wake mmodzi yekhayo. 18 Za mwana ameneyu Mulungu anamuwuza iye kuti, “Zidzukulu zako zidzachokera mwa Isake.” 19 Abrahamu amazindikira kuti Mulungu angathe kuukitsa akufa, ndipo tingathe kunena mofanizira kuti iye analandiranso Isake ngati wouka kwa akufa.

20 Ndi chikhulupiriro Isake anadalitsa Yakobo ndi Esau pa zatsogolo lawo.

21 Ndi chikhulupiriro, pamene Yakobo ankamwalira anadalitsa ana awiri a Yosefe, ndipo anapembedza Mulungu atatsamira ndodo yake.

22 Ndi chikhulupiriro Yosefe ali pafupi kumwalira anayankhula za kutuluka kwa Aisraeli mu Igupto ndipo anawawuza zoti adzachite ndi mafupa ake.

23 Ndi chikhulupiriro Mose atabadwa makolo ake anamubisa miyezi itatu, chifukwa iwo anaona kuti mwanayo anali wokongola ndipo sanaope konse lamulo la mfumu.

24 Ndi chikhulupiriro Mose atakula, anakana kutchedwa mwana wa mwana wamkazi wa Farao. 25 Iye anasankha kuzunzika nawo limodzi anthu a Mulungu kuposa kusangalala ndi zokondweretsa za uchimo kwa nthawi yochepa. 26 Anaona kuti kuzunzika chifukwa cha Khristu kunali kwa mtengowapatali kuposa chuma cha ku Igupto, chifukwa amaona mphotho ya mʼtsogolo. 27 Ndi chikhulupiriro anachoka ku Igupto wosaopa ukali wa mfumu. Iye anapirira chifukwa anamuona Mulungu amene ndi wosaonekayo. 28 Ndi chikhulupiriro anachita Paska ndi kuwaza magazi, kuti mngelo wowononga ana oyamba kubadwa asaphe ana oyamba kubadwa a Aisraeli.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.