Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Salimo la Asafu.
82 Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu;
Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
2 “Mudzateteza osalungama mpaka liti,
ndi kukondera anthu oyipa?
3 Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye;
mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
4 Landitsani anthu ofowoka ndi osowa;
apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
5 “Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse.
Amayendayenda mu mdima;
maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
6 “Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu,
nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
7 Koma mudzafa ngati anthu wamba;
mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
8 Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi,
pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.
1 Mawu a Amosi, mmodzi mwa anthu oweta nkhosa ku Tekowa. Zimene iye anaona mʼmasomphenya zokhudza Israeli patatsala zaka ziwiri kuti chivomerezi chichitike, nthawi imene Uziya anali mfumu ya Yuda ndipo Yeroboamu mwana wa Yowasi anali mfumu ya Israeli.
2 Amosi anati:
“Yehova akubangula mu Ziyoni
ndipo akumveka ngati bingu mu Yerusalemu;
msipu wa abusa ukulira,
ndipo pamwamba pa Karimeli pakuwuma.”
Chiweruzo pa Anthu Oyandikana ndi Israeli
3 Yehova akuti,
“Chifukwa anthu a ku Damasiko akunka nachimwirachimwira,
Ine sindileka kuwalanga.
Popeza anapuntha Giliyadi
ndi zopunthira za mano achitsulo,
4 Ine ndidzatumiza moto pa nyumba ya Hazaeli
umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.
5 Ndidzathyola chipata cha Damasiko;
ndidzawononga mfumu yokhala ku Chigwa cha Aveni,
ndiponso iye amene akugwira ndodo yaufumu mu Beti-Edeni.
Anthu a ku Aramu adzapita ku ukapolo ku Kiri,”
akutero Yehova.
6 Yehova akuti,
“Chifukwa anthu a ku Gaza akunka nachimwirachimwira,
Ine sindileka kuwalanga.
Popeza anatenga ukapolo mtundu wathunthu
ndi kuwugulitsa ku Edomu,
7 ndidzatumiza moto pa makoma a Gaza
umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.
8 Ndidzawononga mfumu ya ku Asidodi
komanso amene akugwira ndodo yaufumu ku Asikeloni.
Ndidzalanga Ekroni,
mpaka wotsala mwa Afilisti atafa,”
akutero Ambuye Yehova.
9 Yehova akuti,
“Chifukwa anthu a ku Turo akunka nachimwirachimwira,
Ine sindileka kuwalanga.
Popeza iwo anagulitsa mtundu wathunthu ku ukapolo ku Edomu,
osasunga pangano laubale lija,
10 Ine ndidzatumiza moto pa makoma a Turo
umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.”
11 Yehova akuti,
“Chifukwa anthu a ku Edomu akunka nachimwirachimwira,
Ine sindileka kuwalanga.
Popeza anathamangitsa mʼbale wake ndi lupanga,
popanda nʼchifundo chomwe.
Popeza mkwiyo wake unakulabe
ndipo ukali wake sunatonthozeke,
12 Ine ndidzatumiza moto pa Temani
umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Bozira.”
13 Yehova akuti,
“Chifukwa anthu a ku Amoni akunka nachimwirachimwira,
Ine sindileka kuwalanga.
Popeza anatumbula akazi oyembekezera a ku Giliyadi
nʼcholinga choti akuze malire awo,
14 Ine ndidzayatsa moto pa makoma a ku Raba
umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.
Padzakhala kulira kwakukulu pa tsiku la nkhondoyo,
kumenyana kudzakhala kwafumbi ngati mkuntho wa kamvuluvulu.
15 Mfumu yawo idzatengedwa kupita ku ukapolo,
iyo pamodzi ndi akuluakulu ake,”
akutero Yehova.
2 Yehova akuti,
“Chifukwa anthu a ku Mowabu akunka nachimwirachimwira,
Ine sindileka kuwalanga.
Popeza anatentha mafupa a mfumu ya ku Edomu,
mpaka kuwasandutsa phulusa,
2 Ine ndidzatumiza moto pa Mowabu,
umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Keriyoti.
Mowabu adzafera pakati pa nkhondo yoopsa,
mʼkati mwa mfuwu wa nkhondo ndi kuliza malipenga.
3 Ndidzawononga wolamulira wake
ndi kupha akuluakulu onse amene ali pamodzi ndi iye,”
akutero Yehova.
Chikhulupiriro ndi Ntchito Zabwino
14 Abale anga, phindu lake nʼchiyani ngati munthu anena kuti ali ndi chikhulupiriro koma chopanda ntchito zabwino? Kodi chikhulupiriro choterechi chingamupulumutse? 15 Tangoganizirani, mʼbale kapena mlongo amene ali ndi usiwa, ndipo alibe chakudya cha tsiku ndi tsiku. 16 Ngati mmodzi wa inu amuwuza kuti, “Pita ndi mtendere, ukafundidwe ndipo ukakhute,” koma osamupatsa zimene akuzisowa, phindu lake nʼchiyani pamenepa? 17 Chomwechonso, chikhulupiriro chokha chopanda ntchito zabwino ndi chakufa.
18 Koma wina anganene kuti, “Inuyo muli ndi chikhulupiriro koma ine ndili ndi ntchito zabwino.”
Onetsani chikhulupiriro chanu chopanda ntchito zabwino ndipo ineyo ndidzakuonetsani chikhulupiriro changa pochita ntchito zabwino. 19 Mumakhulupirira kuti kuli Mulungu mmodzi yekha. Mumachita bwino. Komatu ngakhale ziwanda zimakhulupirira zimenezi ndipo zimanjenjemera ndi mantha.
20 Munthu wopusa iwe, kodi ukufuna umboni woti chikhulupiriro chopanda ntchito zabwino nʼchakufa? 21 Kodi Abrahamu kholo lathu sanatengedwe kukhala wolungama chifukwa cha zimene anachita pamene anapereka mwana wake Isake pa guwa lansembe? 22 Tsono mukuona kuti chikhulupiriro chake ndi ntchito zabwino zinkachitika pamodzi, ndipo chikhulupiriro chake chinasanduka chenicheni chifukwa cha ntchito zake zabwino. 23 Ndipo Malemba akunena kuti, “Abrahamu anakhulupirira Mulungu ndipo anatengedwa kukhala wolungama,” ndipo anatchedwa bwenzi la Mulungu. 24 Tsono mukuona kuti munthu amasanduka wolungama ndi ntchito zabwino osati ndi chikhulupiriro chokha ayi.
25 Nʼchimodzimodzinso, kodi wadama uja, Rahabe, sanasanduke wolungama chifukwa cha zomwe anachita pamene anapereka malo ogona kwa azondi aja ndi kuwathawitsira mbali ina? 26 Monga thupi lopanda mzimu ndi lakufa, chomwechonso chikhulupiriro chopanda ntchito zabwino ndi chakufa.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.