Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
91 Iye amene amakhala mu mthunzi wa Wammwambamwamba
adzapuma mu mthunzi wa Wamphamvuzonse.
2 Ndidzanena za Yehova, “Iye ndiye pothawira panga ndi linga langa,
Mulungu wanga amene ndimadalira.”
3 Ndithu, Iye adzakupulumutsa ku msampha wa mlenje
ndi ku mliri woopsa;
4 Adzakuphimba ndi nthenga zake,
ndipo udzapeza malo othawira mʼmapikomo;
kukhulupirika kwake kudzakhala chishango chako ndi lihawo.
5 Sudzachita mantha ndi zoopsa za usiku,
kapena muvi wowuluka masana,
6 kapena mliri umene umayenda mu mdima,
kapena zowononga za pa nthawi ya masana.
14 “Chifukwa iye amandikonda,” akutero Yehova, “Ndidzamulanditsa;
ndidzamuteteza pakuti wavomereza dzina langa.
15 Adzandiyitana, ndipo ndidzamuyankha;
ndidzakhala naye pa mavuto,
ndidzamupulumutsa ndi kumulemekeza.
16 Ndidzamupatsa moyo wautali
ndi kumupulumutsa.”
Aneneri Onyenga
9 Kunena za aneneri awa:
Mtima wanga wasweka;
mʼnkhongono mwati zii.
Ndakhala ngati munthu woledzera,
ngati munthu amene wasokonezeka ndi vinyo,
chifukwa cha Yehova
ndi mawu ake opatulika.
10 Dziko ladzaza ndi anthu achigololo;
lili pansi pa matemberero.
Dziko lasanduka chipululu ndipo msipu wawuma.
Aneneri akuchita zoyipa
ndipo akugwiritsa ntchito mphamvu zawo molakwika.
11 “Mneneri ngakhale wansembe onse sapembedza Yehova.
Amachita zoyipa ngakhale mʼnyumba yanga,”
akutero Yehova.
12 “Nʼchifukwa chake njira zawo zidzakhala zoterera;
adzawapirikitsira ku mdima
ndipo adzagwera kumeneko.
Adzaona zosaona
mʼnthawi ya chilango chawo,”
akutero Yehova.
13 “Pakati pa aneneri a ku Samariya
ndinaona chonyansa ichi:
Ankanenera mʼdzina la Baala
ndipo anasocheretsa anthu anga, Aisraeli.
14 Ndipo pakati pa aneneri a ku Yerusalemu
ndaonapo chinthu choopsa kwambiri:
amachita chigololo, amanena bodza
ndipo amalimbitsa mtima anthu ochita zoyipa.
Choncho palibe amene amasiya zoyipa zake.
Kwa Ine anthu onsewa
ali ngati a ku Sodomu ndi Gomora.”
15 Choncho ponena za aneneriwa Yehova Wamphamvuzonse akuti,
“Ndidzawadyetsa zakudya zowawa
ndi kuwamwetsa madzi a ndulu,
chifukwa uchimo umene wafalikira mʼdziko lonse
ndi wochokera kwa aneneri a ku Yerusalemuwa.”
16 Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti,
“Musamvere zimene aneneri amenewa akulosera kwa inu;
zomwe aloserazo nʼzachabechabe.
Iwo akungoyankhula za masomphenya a mʼmitima mwawo basi,
osati zochokera kwa Yehova.
17 Iwo amapita ndi kumakawuza amene amandinyoza Ine kuti,
‘zinthu zidzakuyenderani bwino.’
Kwa iwo amene amawumirira kutsata zofuna za mitima yawo amakawawuza kuti,
‘palibe choyipa chimene chidzakugwereni.’ ”
18 Ine ndikuti, “Koma ndani wa iwo amene anakhalapo mu msonkhano wa Yehova?
Ndani anaonapo kapena kumvapo mawu ake?
Ndani mwa iwo analabadirako za mawu ake ndi kuwamvera?
19 Taonani ukali wa Yehova
uli ngati chimphepo chamkuntho,
inde ngati namondwe.
Ndipo adzakantha mitu ya anthu oyipa.
20 Mkwiyo wa Yehova sudzaleka
mpaka atachita zonse zimene
anatsimikiza mu mtima mwake.
Mudzazizindikira bwino zimenezi
masiku akubwerawa.”
21 Yehova anati, “Ine sindinatume aneneri amenewa,
komabe iwo athamanga uku ndi uku kulalikira uthenga wawo;
Ine sindinawayankhule,
komabe iwo ananenera.
22 Iwo akanakhala pa msonkhano wanga
ndiye kuti akanamayankhula mawu anga kwa anthu anga.
Komanso bwenzi atawachotsa anthu anga mʼnjira zawo zoyipa
kuti aleke machimo awo.”
8 Sindikukulamulirani, koma ndikufuna kuona ngati chikondi chanu nʼchoona pofananitsa ndi changu cha anthu ena. 9 Pakuti mukudziwa chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu, kuti ngakhale anali wolemera, koma chifukwa cha inuyo anasanduka wosauka, kuti umphawi wakewo, inuyo mulemere.
10 Ndipo nawa malangizo anga pa zoyenera inu kuchita pa nkhaniyi. Chaka chatha munali oyamba, osati ongofuna kupereka kokha komanso okhala ndi mtima ofuna kupereka. 11 Tsopano tsirizani ntchitoyi, ndipo changu chanu chofunitsitsa kugwira ntchitoyi ndi kuyitsiriza chichitike molingana ndi zimene muli nazo. 12 Ndipo ngati mtima ofunitsitsa ulipo, mphatsoyo imalandiridwa molingana ndi zimene munthuyo ali nazo, osati zimene alibe.
13 Cholinga chathu sikuti tipeputse ena pamene inuyo mukuvutika, koma kuti pakhale kufanana. 14 Zambiri zimene muli nazo pakati panu muthandize nazo osowa, kuti nawonso akadzakhala nazo zambiri adzakuthandizeni pa zosowa zanu. Cholinga nʼkuchita mofanana, 15 monga kwalembedwa kuti, “Iye amene anatola zambiri sizinamutsalireko ndipo amene anatola pangʼono sizinamuchepere.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.