Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 91:1-6

91 Iye amene amakhala mu mthunzi wa Wammwambamwamba
    adzapuma mu mthunzi wa Wamphamvuzonse.
Ndidzanena za Yehova, “Iye ndiye pothawira panga ndi linga langa,
    Mulungu wanga amene ndimadalira.”

Ndithu, Iye adzakupulumutsa ku msampha wa mlenje
    ndi ku mliri woopsa;
Adzakuphimba ndi nthenga zake,
    ndipo udzapeza malo othawira mʼmapikomo;
    kukhulupirika kwake kudzakhala chishango chako ndi lihawo.
Sudzachita mantha ndi zoopsa za usiku,
    kapena muvi wowuluka masana,
kapena mliri umene umayenda mu mdima,
    kapena zowononga za pa nthawi ya masana.

Masalimo 91:14-16

14 “Chifukwa iye amandikonda,” akutero Yehova, “Ndidzamulanditsa;
    ndidzamuteteza pakuti wavomereza dzina langa.
15 Adzandiyitana, ndipo ndidzamuyankha;
    ndidzakhala naye pa mavuto,
    ndidzamupulumutsa ndi kumulemekeza.
16 Ndidzamupatsa moyo wautali
    ndi kumupulumutsa.”

Yeremiya 23:9-22

Aneneri Onyenga

Kunena za aneneri awa:

Mtima wanga wasweka;
    mʼnkhongono mwati zii.
Ndakhala ngati munthu woledzera,
    ngati munthu amene wasokonezeka ndi vinyo,
chifukwa cha Yehova
    ndi mawu ake opatulika.
10 Dziko ladzaza ndi anthu achigololo;
    lili pansi pa matemberero.
    Dziko lasanduka chipululu ndipo msipu wawuma.
Aneneri akuchita zoyipa
    ndipo akugwiritsa ntchito mphamvu zawo molakwika.

11 “Mneneri ngakhale wansembe onse sapembedza Yehova.
    Amachita zoyipa ngakhale mʼnyumba yanga,”
            akutero Yehova.
12 “Nʼchifukwa chake njira zawo zidzakhala zoterera;
    adzawapirikitsira ku mdima
    ndipo adzagwera kumeneko.
Adzaona zosaona
    mʼnthawi ya chilango chawo,”
            akutero Yehova.

13 “Pakati pa aneneri a ku Samariya
    ndinaona chonyansa ichi:
Ankanenera mʼdzina la Baala
    ndipo anasocheretsa anthu anga, Aisraeli.
14 Ndipo pakati pa aneneri a ku Yerusalemu
    ndaonapo chinthu choopsa kwambiri:
    amachita chigololo, amanena bodza
ndipo amalimbitsa mtima anthu ochita zoyipa.
    Choncho palibe amene amasiya zoyipa zake.
Kwa Ine anthu onsewa
    ali ngati a ku Sodomu ndi Gomora.”

15 Choncho ponena za aneneriwa Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Ndidzawadyetsa zakudya zowawa
    ndi kuwamwetsa madzi a ndulu,
chifukwa uchimo umene wafalikira mʼdziko lonse
    ndi wochokera kwa aneneri a ku Yerusalemuwa.”

16 Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Musamvere zimene aneneri amenewa akulosera kwa inu;
    zomwe aloserazo nʼzachabechabe.
Iwo akungoyankhula za masomphenya a mʼmitima mwawo basi,
    osati zochokera kwa Yehova.
17 Iwo amapita ndi kumakawuza amene amandinyoza Ine kuti,
    ‘zinthu zidzakuyenderani bwino.’
Kwa iwo amene amawumirira kutsata zofuna za mitima yawo amakawawuza kuti,
    ‘palibe choyipa chimene chidzakugwereni.’ ”
18 Ine ndikuti, “Koma ndani wa iwo amene anakhalapo mu msonkhano wa Yehova?
    Ndani anaonapo kapena kumvapo mawu ake?
    Ndani mwa iwo analabadirako za mawu ake ndi kuwamvera?
19 Taonani ukali wa Yehova
    uli ngati chimphepo chamkuntho,
inde ngati namondwe.
    Ndipo adzakantha mitu ya anthu oyipa.
20 Mkwiyo wa Yehova sudzaleka
    mpaka atachita zonse zimene
    anatsimikiza mu mtima mwake.
Mudzazizindikira bwino zimenezi
    masiku akubwerawa.”
21 Yehova anati, “Ine sindinatume aneneri amenewa,
    komabe iwo athamanga uku ndi uku kulalikira uthenga wawo;
Ine sindinawayankhule,
    komabe iwo ananenera.
22 Iwo akanakhala pa msonkhano wanga
    ndiye kuti akanamayankhula mawu anga kwa anthu anga.
Komanso bwenzi atawachotsa anthu anga mʼnjira zawo zoyipa
    kuti aleke machimo awo.”

2 Akorinto 8:8-15

Sindikukulamulirani, koma ndikufuna kuona ngati chikondi chanu nʼchoona pofananitsa ndi changu cha anthu ena. Pakuti mukudziwa chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu, kuti ngakhale anali wolemera, koma chifukwa cha inuyo anasanduka wosauka, kuti umphawi wakewo, inuyo mulemere.

10 Ndipo nawa malangizo anga pa zoyenera inu kuchita pa nkhaniyi. Chaka chatha munali oyamba, osati ongofuna kupereka kokha komanso okhala ndi mtima ofuna kupereka. 11 Tsopano tsirizani ntchitoyi, ndipo changu chanu chofunitsitsa kugwira ntchitoyi ndi kuyitsiriza chichitike molingana ndi zimene muli nazo. 12 Ndipo ngati mtima ofunitsitsa ulipo, mphatsoyo imalandiridwa molingana ndi zimene munthuyo ali nazo, osati zimene alibe.

13 Cholinga chathu sikuti tipeputse ena pamene inuyo mukuvutika, koma kuti pakhale kufanana. 14 Zambiri zimene muli nazo pakati panu muthandize nazo osowa, kuti nawonso akadzakhala nazo zambiri adzakuthandizeni pa zosowa zanu. Cholinga nʼkuchita mofanana, 15 monga kwalembedwa kuti, “Iye amene anatola zambiri sizinamutsalireko ndipo amene anatola pangʼono sizinamuchepere.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.