Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 79:1-9

Salimo la Asafu.

79 Inu Mulungu, anthu a mitundu ina alowerera mʼcholowa chanu;
    ayipitsa Nyumba yanu yoyera,
    asandutsa Yerusalemu kukhala bwinja.
Iwo anapereka mitembo ya atumiki anu
    kwa mbalame zamlengalenga ngati chakudya,
    matupi a oyera mtima anu kwa zirombo za dziko lapansi.
Akhetsa magazi monga madzi
    kuzungulira Yerusalemu yense,
    ndipo palibe wina woti ayike mʼmanda anthu akufa.
Ife ndife chinthu chonyozeka kwa anansi athu,
    choseketsa ndi cholalatiridwa kwa iwo amene atizungulira.

Mpaka liti Inu Yehova? Kodi mudzakwiya mpaka muyaya?
    Kodi mpaka liti nsanje yanu idzayaka ngati moto?
Khuthulirani ukali wanu pa anthu a mitundu ina
    amene sakudziwani Inu,
pa maufumu
    amene sayitana pa dzina lanu;
pakuti iwo ameza Yakobo
    ndi kuwononga dziko lawo.
Musatilange chifukwa cha machimo a makolo athu
    chifundo chanu chibwere msanga kukumana nafe,
    pakuti tili ndi chosowa chachikulu.

Tithandizeni Inu Mulungu Mpulumutsi wathu,
    chifukwa cha ulemerero wa dzina lanu;
tipulumutseni ndi kutikhululukira machimo athu
    chifukwa cha dzina lanu.

Yeremiya 8:14-17

14 Koma amati, “Tikukhala pano chifukwa chiyani?
    Tiyeni tonse pamodzi
tithawire ku mizinda yotetezedwa
    ndi kukafera kumeneko.
Pakuti Yehova Mulungu wathu watsimikiza kuti tiyenera kufa.
    Watipatsa madzi aululu kuti timwe,
    chifukwa tamuchimwira.
15 Tinkayembekezera mtendere
    koma palibe chabwino chomwe chinachitika,
tinkayembekezera kuchira
    koma tinakumana ndi zoopsa zokhazokha.
16 Kulira kwa ngʼombe zazimuna za mdani
    kukumveka kuchokera ku Dani;
dziko lonse likunjenjemera
    chifukwa cha kulira kwa akavalowo.
Akubwera kudzawononga dziko
    ndi zonse zimene zili mʼmenemo.
    Adzawononga mzinda ndi onse okhalamo.”

17 Yehova akuti, “Onani, ndikukutumizirani njoka zaululu,
    mphiri zimene munthu sangathe kuzilodza,
    ndipo zidzakulumani,”

Yeremiya 9:2-11

Ndani adzandipatsa malo
    ogona mʼchipululu
kuti ndiwasiye anthu anga
    ndi kuwachokera kupita kutali;
pakuti onse ndi achigololo,
    ndiponso gulu la anthu onyenga.

“Amapinda lilime lawo ngati uta.
    Mʼdzikomo mwadzaza
ndi mabodza okhaokha
    osati zoonadi.
Amapitirirabe kuchita zoyipa;
    ndipo sandidziwa Ine.”
            Akutero Yehova.
“Aliyense achenjere ndi abwenzi ake;
    asadalire ngakhale abale ake.
Aliyense amafuna kumudyera mʼbale wake masuku pa mutu.
    Choncho aliyense amachitira bwenzi lake ugogodi.
Aliyense amamunamiza mʼbale wake
    ndipo palibe amene amayankhula choonadi.
Anapazoloweza pakamwa pawo kunena zabodza;
    amalimbika kuchita machimo.
Iwe wakhalira mʼchinyengo
    ndipo ukukana kundidziwa Ine,”
            akutero Yehova.

Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Taonani, Ine ndidzawasungunula ngati chitsulo ndi kuwayesa.
    Kodi ndingachite nawonso
    bwanji chifukwa cha machimo awo?
Lilime lawo lili ngati muvi wakuthwa;
    limayankhula zachinyengo.
Aliyense ndi pakamwa pake amayankhula mawu achikondi kwa mnansi wake,
    koma mu mtima mwake amakonzekera zomuchita chiwembu.
Kodi ndilekerenji kuwalanga chifukwa cha zimenezi?
    akutero Yehova.
‘Kodi ndisawulipsire
    mtundu wotere wa anthu?’ ”

10 Ndidzakhetsa misozi ndi kulira kwamphamvu chifukwa cha mapiri
    ndipo ndidzadandaula chifukwa cha msipu wa ku chipululu.
Malo onsewo awonongeka ndipo palibe amene amapitako,
    ndipo sikumveka kulira kwa ngʼombe.
Mbalame zamlengalenga zathawa
    ndipo nyama zakuthengo zachokako.

11 Ndipo Yehova anati, “Ndidzasandutsa Yerusalemu kukhala bwinja,
    malo okhalamo ankhandwe;
ndipo ndidzawononga mizinda ya Yuda
    kotero kuti palibe munthu amene adzakhalemo.”

Marko 12:41-44

Chopereka cha Mayi Wamasiye

41 Yesu anakhala pansi moyangʼanana ndi pamene amaperekera zopereka ndipo amaona anthu akupereka ndalama zawo mʼthumba la Nyumba ya Mulungu. Anthu ambiri olemera anaponya ndalama zambiri. 42 Koma mkazi wamasiye, wosauka anabwera ndi kuyikamo tindalama tiwiri ta kopala, tongokwanira theka la ndalama.

43 Yesu anayitana ophunzira ake nati, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti mayi wosauka wamasiyeyu waponya zambiri mʼthumbali kuposa ena onsewa. 44 Iwo apereka molingana ndi chuma chawo; koma iye, mwaumphawi wake, wapereka zonse anali nazo ngakhale zoti akanagulira chakudya.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.