Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
18 Ndadzazidwa ndi chisoni kwambiri,
mtima wanga walefukiratu.
19 Imvani kulira kwa anthu anga
kuchokera ku dziko lakutali:
akuti, “Kodi Yehova sali ku Ziyoni?
Kodi mfumu yake sili kumeneko?”
“Chifukwa chiyani akundiputa ndi mafano awo osema,
ndi milungu yawo yachilendo?”
20 “Nthawi yokolola yapita,
chilimwe chapita,
koma sitinapulumuke.”
21 Chifukwa cha mavuto a anthu anga, ine ndikumva kuwawa;
ndikungolira ndipo mantha aakulu andigwira.
22 Kodi ku Giliyadi kulibe mankhwala ochiritsa?
Kodi kumeneko kulibe singʼanga?
Nanga chifukwa chiyani mabala
a anthu anga sanapole?
9 Aa, ndikanakonda kuti mutu wanga ukanakhala chitsime cha madzi,
ndi maso anga ngati kasupe wa misozi!
Ndikanalira usana ndi usiku
kulirira anthu anga amene aphedwa.
Salimo la Asafu.
79 Inu Mulungu, anthu a mitundu ina alowerera mʼcholowa chanu;
ayipitsa Nyumba yanu yoyera,
asandutsa Yerusalemu kukhala bwinja.
2 Iwo anapereka mitembo ya atumiki anu
kwa mbalame zamlengalenga ngati chakudya,
matupi a oyera mtima anu kwa zirombo za dziko lapansi.
3 Akhetsa magazi monga madzi
kuzungulira Yerusalemu yense,
ndipo palibe wina woti ayike mʼmanda anthu akufa.
4 Ife ndife chinthu chonyozeka kwa anansi athu,
choseketsa ndi cholalatiridwa kwa iwo amene atizungulira.
5 Mpaka liti Inu Yehova? Kodi mudzakwiya mpaka muyaya?
Kodi mpaka liti nsanje yanu idzayaka ngati moto?
6 Khuthulirani ukali wanu pa anthu a mitundu ina
amene sakudziwani Inu,
pa maufumu
amene sayitana pa dzina lanu;
7 pakuti iwo ameza Yakobo
ndi kuwononga dziko lawo.
8 Musatilange chifukwa cha machimo a makolo athu
chifundo chanu chibwere msanga kukumana nafe,
pakuti tili ndi chosowa chachikulu.
9 Tithandizeni Inu Mulungu Mpulumutsi wathu,
chifukwa cha ulemerero wa dzina lanu;
tipulumutseni ndi kutikhululukira machimo athu
chifukwa cha dzina lanu.
Malangizo Achipembedzo
2 Tsono choyamba ndikukupemphani kuti mupempherere anthu onse. Mapemphero anu akhale opemba, opempha, opempherera ena ndi oyamika. 2 Mupempherere mafumu ndi onse aulamuliro, kuti tikhale moyo wamtendere ndi bata, woopa Mulungu ndi oyera mtima. 3 Izi ndi zabwino ndipo zimakondweretsa Mulungu Mpulumutsi wathu, 4 amene amafuna kuti anthu onse apulumutsidwe ndipo kuti adziwe choonadi. 5 Pakuti pali Mulungu mmodzi yekha ndi Mʼkhalapakati mmodzi yekha pakati pa Mulungu ndi anthu, munthu uja Khristu Yesu. 6 Iyeyu anadzipereka kukhala dipo lowombolera anthu onse. Umenewu ndi umboni umene waperekedwa mu nthawi yake yoyenera. 7 Nʼchifukwa chake anandisankha kukhala mlaliki ndiponso mtumwi wophunzitsa anthu a mitundu ina mawu achikhulupiriro choona. Sindikunama ayi, ndikunena zoona.
Fanizo la Kapitawo Wosakhulupirika
16 Yesu anawuza ophunzira ake kuti, “Panali munthu wina wachuma amene kapitawo wake anzake anamuneneza kuti amawononga chuma chakecho. 2 Choncho anamuyitana ndi kumufunsa kuti, ‘Kodi nʼchiyani chimene ndikumva za iwe? Pereka tsatanetsatane wa ntchito yako, pakuti supitirizanso kukhala kapitawo wanga.’
3 “Kapitawoyo analingalira kuti, ‘Kodi tsopano ndidzachita chiyani? Bwana wanga andichotsa ntchito. Ine ndilibe mphamvu zokwanira zolimira, komanso ine ndimachita manyazi kupempha. 4 Ine ndikudziwa chimene ndidzachita kotero kuti, pamene ntchito yanga yatha pano, anthu adzandilandire mʼnyumba zawo.’
5 “Choncho iye anayitana aliyense amene anali ndi ngongole kwa bwana wake. Iye anafunsa woyamba, ‘Kodi uli ndi ngongole yotani kwa bwana wanga?’
6 “Iye anayankha kuti, ‘Migolo yamafuta a olivi 800.’
“Kapitawo uja anamuwuza iye, ‘Tenga pamene unalemba ngongole yakoyo, khala pansi msanga ndipo lemba kuti ndi migolo 400.’
7 “Kenaka iye anafunsa wachiwiri kuti, ‘Nanga iwe uli ndi ngongole yotani?’
“Iye ayankha kuti madengu a tirigu 1,000.
“Iye anati, ‘Tenga pamene unalemba ngongole yakoyo ndipo ulembepo 800.’
8 “Bwana anayamikira kapitawo wosakhulupirikayo popeza anachita mochenjera. Pakuti anthu a dziko lino lapansi ndi ochenjera kwambiri akamachita zinthu ndi anthu ofanana nawo kuposa anthu a kuwunika. 9 Ine ndikukuwuzani inu, gwiritsani ntchito chuma cha dziko lapansi kuti mudzipezere nokha abwenzi, kuti pamene chatha mudzalandiridwe mʼmalo okhala amuyaya.
10 “Amene akhulupirika pa zinthu zochepa akhoza kukhulupirikanso pa zinthu zambiri, ndipo amene sakhulupirika pa zinthu zochepa adzakhala wosakhulupirika pa zinthu zambiri. 11 Ndipo ngati simunakhale okhulupirika pogwiritsa ntchito chuma cha dziko lapansi, ndani amene adzakusungitsani chuma chenicheni? 12 Ndipo ngati simunakhale okhulupirika ndi chuma cha mwini wake, ndani amene adzakupatsani katundu wanuwanu?
13 “Palibe wantchito amene angatumikire mabwana awiri. Mwina iye adzadana ndi wina ndi kukonda winayo, kapena adzakhala wodzipereka kwa wina ndi kumunyoza winayo. Inu simungathe kutumikira Mulungu komanso ndalama nthawi imodzi.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.