Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 139:1-6

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

139 Inu Yehova, mwandisanthula
    ndipo mukundidziwa.
Inu mumadziwa pamene ndikhala pansi ndi pamene ndidzuka;
    mumazindikira maganizo anga muli kutali.
Mumapenyetsetsa pamene ndikutuluka ndi kugona kwanga;
    mumadziwa njira zanga zonse.
Mawu asanatuluke pa lilime langa
    mumawadziwa bwinobwino, Inu Yehova.

Mumandizinga kumbuyo ndi kutsogolo komwe;
    mwasanjika dzanja lanu pa ine.
Nzeru zimenezi ndi zopitirira nzeru zanga,
    ndi zapamwamba kuti ine ndizipeze.

Masalimo 139:13-18

13 Pakuti Inu munalenga za mʼkati mwanga;
    munandiwumba pamodzi mʼmimba mwa amayi anga.
14 Ndimakuyamikani chifukwa ndinapangidwa mochititsa mantha ndi modabwitsa;
    ntchito zanu ndi zodabwitsa,
    zimenezi ndimazidziwa bwino lomwe.
15 Mapangidwe anga sanabisike pamaso panu
    pamene ndimapangidwa mʼmalo achinsinsi,
pamene ndinkawumbidwa mwaluso mʼmimba ya amayi anga.
16 Maso anu anaona thupi langa lisanawumbidwe.
    Masiku onse amene anapatsidwa kwa ine, analembedwa mʼbuku lanu
    asanayambe nʼkuwerengedwa komwe.

17 Zolingalira zanu pa ine ndi zamtengowapatali, Inu Mulungu,
    ndi zosawerengeka ndithu!
18 Ndikanaziwerenga,
    zikanakhala zochuluka kuposa mchenga;
    pamene ndadzuka, ndili nanube.

Yeremiya 15:10-21

10 Kalanga ine, amayi pakuti munandibereka ine,
    munthu amene ndikutsutsana ndi kulimbana ndi anthu pa dziko lonse!
Ine sindinakongoze kapena kukongola kanthu,
    komatu aliyense akunditemberera.

11 Yehova anati,

“Ndithudi, Ine ndidzakulanditsa kuti upeze bwino.
    Ndithudi, adani ako adzakupempha pa nthawi ya tsoka
    ndi ya mavuto awo.

12 “Palibe munthu amene angathe kudula chitsulo,
    makamaka chitsulo chochokera kumpoto chosakaniza ndi mkuwa.
13 Anthu ako ndi chuma chako
    ndidzazipereka kwa ofunkha popanda malipiro,
chifukwa cha machimo anu onse
    a mʼdziko lanu lonse.
14 Ndidzakusandutsani akapolo a adani anu
    mʼdziko limene inu simulidziwa,
chifukwa mkwiyo wanga wayaka ngati moto
    umene udzakutenthani.”

15 Ine ndinati, “Inu Yehova, mumadziwa zonse;
    kumbukireni ndi kundisamalira.
    Ndilipsireni anthu ondizunza.
Ndilezereni mtima musandilande moyo wanga.
    Onani momwe ndi kuvutikira chifukwa cha Inu.
16 Munandiyankhula ndipo mawu anu ndinawalandira bwino.
    Mawu anu anandipatsa chimwemwe ndipo mtima wanga unasangalala.
Paja ine, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse,
    ndimadziwika ndi dzina lanu.
17 Sindinakhale nawo mʼgulu la anthu amadyera,
    sindinasangalale nawo anthu amenewo.
Ndinakhala ndekha chifukwa choti dzanja lanu linali pa ine
    ndipo munadzaza mu mtima mwanga ndi mkwiyo.
18 Nanga nʼchifukwa chiyani mavuto anga sakutha?
    Bwanji chilonda changa sichikupola?
Kodi inu mudzakhala ngati mtsinje wowuma nthawi yachilimwe,
    kapena ngati kasupe wopanda madzi?”

19 Tsono Yehova anandiyankha kuti,

“Ukabwerera kwa Ine, ndidzakulandiranso
    ndipo udzakhalanso mtumiki wanga.
Ngati udzayankhula mawu oyenera osati achabechabe,
    udzakhalanso mneneri wanga.
Anthu adzabwera kwa iwe
    ndipo sipadzafunika kuti iwe upite kwa iwo.
20 Ndidzakusandutsa ngati khoma lolimba
    ngati mkuwa kwa anthu awa.
Adzalimbana nawe
    koma sadzakugonjetsa,
pakuti Ine ndili nawe
    kukulanditsa ndi kukupulumutsa,”
            akutero Yehova.
21 “Ndidzakupulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa
    ndipo ndidzakuwombola kwa anthu ankhanza.”

Afilipi 2:25-30

25 Koma ndikuganiza kuti nʼkofunika kuti ndikutumizireni mʼbale wanga Epafrodito, mtumiki mnzanga ndi msilikali mnzanga, amenenso ndi mtumiki wanu amene munamutumiza kuti adzandithandize pa zosowa zanga. 26 Pakuti akukulakalakani nonsenu ndipo akusauka mu mtima chifukwa munamva kuti akudwala. 27 Zoonadi ankadwala ndipo anatsala pangʼono kumwalira. Koma Mulungu anamuchitira chifundo, ndipo sanangomuchitira chifundo iye yekhayu komanso ine, kuti chisoni changa chisachuluke. 28 Choncho khumbo langa lofulumiza kumutumiza lakula, kuti pamene mumuonenso musangalale komanso kuti nkhawa yanga ichepe. 29 Mulandireni mwa Ambuye ndi chimwemwe chachikulu, ndipo anthu onga iyeyu muziwachitira ulemu. 30 Iyeyu anatsala pangʼono kufa chifukwa cha ntchito ya Khristu, anayika moyo pa chiswe kuti akwaniritse thandizo limene inu simukanatha.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.