Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
40 Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake
ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
41 Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina,
ndipo adani awo anawalamulira.
42 Adani awo anawazunza
ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
43 Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri,
koma iwo ankatsimikiza za kuwukira
ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
44 Koma Iye anaona kuzunzika kwawo
pamene anamva kulira kwawo;
45 Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake
ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
46 Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo
awamvere chisoni.
47 Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu,
ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina
kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera
ndi kunyadira mʼmatamando anu.
48 Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli,
Kuyambira muyaya mpaka muyaya.
Anthu onse anene kuti, “Ameni!”
Tamandani Yehova.
Chiwonongeko Chikubwera
17 Sonkhanitsani katundu wanu,
inu amene mukukhala mʼlinga la ankhondo.
18 Pakuti Yehova akuti,
“Tsopano Ine ndidzachotsa anthu onse
amene akukhala mʼdziko lino;
adzakhala pa mavuto
mpaka adzamvetsa.”
19 Aliyense ankangoti, “Mayo ine, chifukwa cha kupweteka kwanga!
Chilonda changa nʼchachikulu!”
Koma ine ndinkaganiza kuti, “Ndithu, ili ndi vuto langa basi,
choncho ndingolipirira.”
20 Tenti yanga yawonongeka,
zingwe zake zonse zaduka.
Ana anga andisiya ndipo kulibenso.
Palibenso amene adzandimangire tenti,
kapena kufunyulula nsalu yake.
21 Abusa ndi opusa
ndipo sanapemphe nzeru kwa Yehova;
choncho palibe chimene anapindula
ndipo nkhosa zawo zonse zabalalika.
22 Tamvani! kukubwera mphekesera,
phokoso lalikulu la gulu la a ankhondo likumveka kuchokera kumpoto!
Lidzasandutsa bwinja mizinda ya ku Yuda,
malo okhala nkhandwe.
Pemphero la Yeremiya
23 Inu Yehova, ndikudziwa kuti moyo umene munthu ali nawo si wake;
munthuyo sangathe kuwongolera mayendedwe ake.
24 Inu Yehova, langizeni, komatu mwachilungamo,
osati ndi mkwiyo wanu,
mungandiwononge kotheratu.
25 Tsanulirani ukali wanu pa mitundu ya anthu amene sakudziwani,
ndiye kuti mitundu ya anthu amene satama pa dzina lanu mopemba.
Iwo aja anasakaza Yakobo;
amusakaza kotheratu
ndipo awononga dziko lake.
Achenjeza za Aphunzitsi Amalamulo
45 Pamene anthu onse ankamvetsera, Yesu anati kwa ophunzira ake, 46 “Chenjerani ndi aphunzitsi amalamulo. Iwo amakonda kuyenda atavala mikanjo ndipo amakonda kulonjeredwa mʼmisika ndipo amakhala mʼmipando yofunika mʼmasunagoge ndi mʼmalo aulemu mʼmaphwando. 47 Amawadyera akazi amasiye chuma chawo ndi kuchita mapemphero aatali kuti awaone. Anthu oterewa adzalangidwa kwambiri.”
Chopereka cha Mayi Wamasiye
21 Yesu atayangʼana, anaona olemera akuyika mphatso zawo mu chosungira ndalama za mʼNyumba ya Mulungu. 2 Iye anaonanso mkazi wamasiye wosauka akuyikamo timakopala tiwiri. 3 Iye anati, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mkazi wamasiye wosaukayu wapereka zambiri kuposa ena onsewa. 4 Anthu onsewa atapa mphatso zawo kuchokera pa zochuluka zimene ali nazo; koma uyu, mwa umphawi wake, wapereka zonse zimene ali nazo.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.