Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 20

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

20 Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso;
    dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.
Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika;
    akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.
Iye akumbukire nsembe zako zonse
    ndipo alandire nsembe zako zopsereza.
            Sela
Akupatse chokhumba cha mtima wako
    ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.
Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana
    ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu,
Yehova ayankhe zopempha zako zonse.

Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake;
    Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika
    ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.
Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo
    koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.
Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa,
    koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.

Inu Yehova, pulumutsani mfumu!
    Tiyankheni pamene tikuyitanani!

Yesaya 26:1-9

Nyimbo ya Matamando

26 Tsiku limenelo anthu a mʼdziko la Yuda adzayimba nyimbo iyi.

Tili ndi mzinda wolimba.
    Mulungu amawuteteza ndi zipupa
    ndi malinga.
Tsekulani zipata za mzinda
    kuti mtundu wolungama
    ndi wokhulupirika ulowemo.
Inu mudzamupatsa munthu
    wa mtima wokhazikika
    mtendere weniweni.
Mudalireni Yehova mpaka muyaya,
    chifukwa Yehova Mulungu ndiye Thanthwe losatha.
Iye amatsitsa anthu amene amadziyika pamwamba,
    iye amagwetsa pansi mzinda wodzitukumula,
amagumula makoma ake
    ndi kuwagwetsa pansi pa fumbi penipeni.
Mapazi a anthu akuwupondereza,
    mapazi a anthu oponderezedwa,
    mapazi anthu osauka.

Njira ya munthu wolungama ndi yosalaza,
    Inu Wolungamayo, mumasalaza njira ya wolungama.
Inde Yehova, timayenda mʼnjira zanu zolungama,
    ife timayembekezera Inu;
mitima yathu imakhumba kukumbukira
    ndi kulemekeza dzina lanu.
Moyo wanga umalakalaka Inu usiku wonse;
    nthawi yammawa ndimafunafuna Inu.
Pamene muweruza dziko lapansi
    anthu amaphunzira kuchita chilungamo.

2 Akorinto 4:16-18

16 Nʼchifukwa chake ife sititaya mtima. Ngakhale thupi lathu likunka lifowokerafowokera, koma mʼkatimu tikulimbikitsidwa mwatsopano tsiku ndi tsiku. 17 Pakuti masautso athu ndi opepuka ndi a kanthawi, koma akutitengera ulemerero wamuyaya umene ndi wopambana kwambiri. 18 Motero sitiyangʼana zinthu zimene ndi zooneka ndi maso, koma zinthu zimene ndi zosaoneka. Pakuti zimene zimaoneka ndi zosakhalitsa, koma zimene sizioneka ndi zamuyaya.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.