Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
124 Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,
anene tsono Israeli,
2 akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,
potiwukira anthuwo,
3 iwo atatipsera mtima,
akanatimeza amoyo;
4 chigumula chikanatimiza,
mtsinje ukanatikokolola,
5 madzi a mkokomo
akanatikokolola.
6 Atamandike Yehova,
amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo.
7 Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame
yokodwa mu msampha wa mlenje;
msampha wathyoka,
ndipo ife tapulumuka.
8 Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova
wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Ulemerero Wamʼtsogolo wa Ziyoni
54 “Sangalala, iwe mayi wosabala,
iwe amene sunabalepo mwana;
imba nyimbo, ndi kufuwula mwachimwemwe,
iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka;
chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri
kuposa mkazi wokwatiwa,”
akutero Yehova.
2 Kulitsa malo omangapo tenti yako,
tambasula kwambiri nsalu zake,
usaleke;
talikitsa zingwe zako,
limbitsa zikhomo zako.
3 Pakuti udzasendeza malire ako kumanja ndi kumanzere;
ndipo zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina
ndipo zidzakhala mʼmizinda yawo yosiyidwa.
4 “Usachite mantha; sadzakunyozanso.
Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso.
Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako
ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.
5 Pakuti Mlengi wako ali ngati mwamuna wako,
dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wanu;
dzina lake ndi Mulungu wa dziko lonse lapansi.
6 Yehova wakuyitananso,
uli ngati mkazi wosiyidwa ndi wodzaza ndi chisoni mu mtima,
mkazi amene anakwatiwa pa unyamata wake kenaka nʼkukanidwa,”
akutero Mulungu wako.
7 “Kwa kanthawi kochepa, Ine ndinakusiya,
koma ndidzakutenganso chifukwa ndimakukonda kwambiri.
8 Ndinakufulatira kwa kanthawi kochepa
ndili wokwiya kwambiri.
Koma ndi kukoma mtima kwanga kwa muyaya,
ndidzakuchitira chifundo,”
akutero Yehova Mpulumutsi wako.
9 “Kwa ine zimenezi zili ngati mmene zinalili mʼnthawi ya Nowa.
Monga ndinalumbira nthawi imeneyo kuti sindidzawononganso dziko lapansi ndi madzi.
Kotero tsopano ndalumbira kuti sindidzakupseraninso mtima,
sindidzakudzudzulaninso.
10 Ngakhale mapiri atagwedezeka
ndi zitunda kusunthidwa,
koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha.
Pangano langa lamtendere silidzasintha,”
akutero Yehova amene amakuchitira chifundo.
23 Pa nthawi imeneyo ngati wina adzati kwa inu, ‘Onani, Khristu ali pano!’ Kapena, ‘Uyo ali ukoyo!’ Musakhulupirire. 24 Chifukwa akhristu onama ndi aneneri onama adzaoneka ndipo adzachita zizindikiro zazikulu ndi zodabwitsa kuti akanyenge ngakhale osankhidwawo ngati kukanakhala kotheka kutero. 25 Onani, ndakuwuzani izi nthawi isanafike.
26 “Ndiye ngati wina akuwuzani inu kuti, ‘Uyo ali ku chipululu,’ inu musapiteko; kapena akati, ‘Uyu ali kuno mʼchipinda chamʼkati,’ musakhulupirire. 27 Monga momwe mphenzi ingʼanima kuchokera kummawa kupita kumadzulo, momwemonso kudzakhala kubwera kwa Mwana wa Munthu. 28 Kulikonse kuli chinthu cha kufa, makwangwala adzasonkhanako.
29 “Akadzangotha mavuto a masiku amenewo,
“ ‘dzuwa lidzadetsedwa,
ndipo mwezi sudzawala;
nyenyezi zidzagwa kuchokera kumwamba,
ndipo mphamvu za mmwamba zidzagwedezeka.’
30 “Pa nthawi imeneyo chizindikiro cha Mwana wa Munthu chidzaoneka mlengalenga, ndipo mitundu yonse ya pa dziko lapansi idzalira. Idzaona Mwana wa Munthu akubwera ndi mitambo, mphamvu ndi ulemerero waukulu. 31 Ndipo adzatuma angelo ake, ndi kulira kwa lipenga kwakukulu, nadzasonkhanitsa osankhidwa ake kuchokera ku mphepo zinayi, ndi kuchokera kumathero a thambo kufika mbali ina.
32 “Tsopano kuchokera ku mtengo wamkuyu phunzirani ichi: Pamene uyamba kuphukira, masamba ake akatuluka, mumadziwa kuti dzinja layandikira. 33 Momwemonso, pamene mudzaona zinthu zonsezi mudzadziwe kuti ali pafupi pa khomo penipeni. 34 Zoonadi, ndikuwuzani kuti mʼbado uwu sudzatha mpaka zinthu zonse zitachitika. 35 Kumwamba ndi dziko lapansi zidzatha, koma mawu anga sadzatha.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.