Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Nyimbo ya Mariya
46 Ndipo Mariya anati:
“Moyo wanga ulemekeza Ambuye.
47 Ndipo mzimu wanga ukondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,
48 pakuti wakumbukira
kudzichepetsa kwa mtumiki wake.
Kuyambira tsopano mibado yonse idzanditcha wodala,
49 pakuti Wamkuluyo wandichitira ine zinthu zazikulu,
dzina lake ndi loyera.
50 Chifundo chake chifikira kwa iwo amene amuopa Iye
kufikira mibadomibado.
51 Iye wachita zamphamvu ndi dzanja lake;
Iye anabalalitsa iwo amene ali onyada mʼmaganizo awo.
52 Iye anachotsa olamulira pa mipando yawo yaufumu,
koma wakweza odzichepetsa.
53 Iye wakhutitsa a njala ndi zinthu zabwino
koma anachotsa olemera wopanda kanthu.
54 Iye anathandiza mtumiki wake Israeli,
pokumbukira chifundo chake.
55 Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse
monga ananena kwa makolo athu.”
Ulemerero wa Ziyoni
60 “Dzuka, wala, pakuti kuwala kwako kwafika,
ndipo ulemerero wa Yehova wakuwalira.
2 Taona, mdima waphimba dziko lapansi
ndipo mdima wandiweyani wagwa pa anthu a mitundu ina,
koma Yehova adzakuwalira iwe,
ndipo ulemerero wake udzaoneka pa iwe.
3 Mitundu ya anthu idzatsata kuwunika kwako
ndipo mafumu adzalondola kunyezimira kwa mʼbandakucha wako.
4 “Tukula maso ako, yangʼanayangʼana ndipo ona zimene zikuchitika.
Onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe;
ana ako a amuna akubwera kuchokera kutali
ndipo ana ako aakazi anyamulidwa mʼmanja.
5 Ukadzaona zimenezi udzasangalala kwambiri,
mtima wako udzalumpha ndi kudzaza ndi chimwemwe;
chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe
chuma cha mitundu ya anthu chidzabwera kwa iwe.
6 Gulu la ngamira lidzaphimba dziko lako,
ngamira zingʼonozingʼono zidzachokera ku Midiyani ndi ku Efai.
Ndipo onse a ku Seba adzabwera
atanyamula golide ndi lubani
uku akutamanda Yehova.
Nyimbo ya Zakariya
67 Abambo ake, Zakariya, anadzazidwa ndi Mzimu Woyera ndipo ananenera kuti,
68 “Alemekezeke Ambuye, Mulungu wa Israeli
chifukwa wabwera ndi kuwombola anthu ake.
69 Iye wakweza nyanga yachipulumutso kwa ife
mu nyumba ya mtumiki wake Davide.
70 (Monga mmene ananenera kudzera mwa aneneri oyera),
71 chipulumutso kuchoka kwa adani athu
ndi kuchoka mʼdzanja la onse otida,
72 kuonetsa chifundo kwa makolo athu
ndi kukumbukira pangano lake loyera,
73 lumbiro limene analumbira kwa kholo lathu Abrahamu:
74 kutilanditsa ife mʼdzanja la adani athu,
ndi kutipanga ife timutumikire Iye mopanda mantha,
75 mʼchiyero ndi mʼchilungamo masiku athu onse.
76 “Ndipo iwe mwana wanga udzatchedwa mneneri wa Wammwambamwamba;
pakuti udzapita patsogolo pa Ambuye kukonza njira yake,
77 kupatsa anthu ake chidziwitso cha chipulumutso
kudzera mwa chikhululukiro cha machimo awo,
78 chifukwa cha chifundo chachikulu cha Mulungu wathu,
ndipo kuwala kwa dzuwa kudzafikira ife kuchokera kumwamba,
79 kuwalira iwo okhala mu mdima
ndi mu mthunzi wa imfa,
kutsogolera mapazi athu mu njira yamtendere.”
80 Ndipo mwanayo anakula nakhala wamphamvu mu mzimu; ndipo anakhala ku chipululu mpaka pamene anaonekera poyera mu Israeli.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.