Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
21 Inu Yehova, mfumu ikusangalala mu mphamvu yanu,
chimwemwe chake nʼchachikuludi pa kupambana kumene mumapereka!
2 Inu mwayipatsa zokhumba za mtima wake
ndipo simunayimane zopempha za pa milomo yake.
Sela
3 Inu munayilandira ndi madalitso ochuluka
ndipo munayiveka chipewa chaufumu chagolide weniweni pa mutu wake.
4 Iye anakupemphani moyo, ndipo munamupatsa
masiku ochuluka kwamuyaya.
5 Kudzera mʼzigonjetso zimene munapereka, ulemerero wake ndi waukulu;
Inu mwapereka pa iyo ulemerero ndi ufumu.
6 Zoonadi Inu mwayipatsa madalitso amuyaya,
Inu mwayipatsa chisangalalo ndi chimwemwe chimene chili pamaso panu.
7 Pakuti mfumu imadalira Yehova;
kudzera mʼchikondi chake chosatha cha Wammwambamwamba,
iyo sidzagwedezeka.
8 Dzanja lanu lidzayimitsa adani anu onse;
dzanja lanu lamanja lidzagwira adani anu.
9 Pa nthawi ya kuonekera kwanu
mudzawasandutsa ngʼanjo yamoto yotentha.
Mu ukali wake Yehova adzawameza,
ndipo moto wake udzawatha.
10 Inu mudzawononga ana awo pa dziko lapansi,
zidzukulu zawo pakati pa anthu.
11 Ngakhale iwo akukonzereni chiwembu mwa kuchenjera kwawo
sadzapambana;
12 pakuti mudzawapirikitsa ndipo adzaonetsa misana yawo
pamene mudzawaloza ndi mivi yanu.
13 Mukwezeke Inu Yehova mʼmphamvu yanu,
ife tidzayimba nyimbo ndi kutamanda mphamvu yanu.
Chilango cha Yehova pa Dziko Lapansi
24 Taonani, Yehova adzawononga dziko lapansi
ndi kulisandutsa chipululu;
Iye adzasakaza maonekedwe ake
ndi kumwaza anthu ake onse.
2 Aliyense zidzamuchitikira mofanana:
wansembe chimodzimodzi munthu wamba,
antchito aamuna mofanananso ndi ambuye awo aamuna,
antchito aakazi chimodzimodzi ambuye awo aakazi,
wogula chimodzimodzi wogulitsa,
wobwereka chimodzimodzi wobwereketsa,
okongola chimodzimodzi okongoza.
3 Dziko lapansi lidzawonongedwa kwathunthu
ndi kusakazikiratu.
Yehova wanena mawu awa.
4 Dziko lapansi likulira ndipo likufota,
dziko lonse likuvutika ndipo likuwuma,
anthu omveka a dziko lapansi akuvutika.
5 Anthu ayipitsa dziko lapansi;
posamvera malangizo ake;
pophwanya mawu ake
ndi pangano lake lamuyaya.
6 Nʼchifukwa chake matemberero akuwononga dziko lapansi;
anthu a mʼdzikomo akuzunzika chifukwa cha kulakwa kwawo,
iwo asakazika
ndipo atsala ochepa okha.
7 Vinyo watsopano watha ndipo mphesa zikufota;
onse okonda zosangalatsa ali ndi chisoni.
8 Kulira kokometsera kwa matambolini kwatha,
phokoso la anthu osangalala latha,
zeze wosangalatsa wati zii.
9 Anthu sadzayimbanso akumwa vinyo;
akadzamwa zaukali zidzakhala zowawa mʼkamwa mwawo.
10 Mzinda wachisokonezo uja wawonongeka;
nyumba iliyonse yatsekedwa.
11 Anthu akulira mʼmisewu kufuna vinyo;
chimwemwe chonse chatheratu,
palibenso chisangalalo pa dziko lapansi.
12 Mzinda wasanduka bwinja
zipata zake zagumuka.
13 Zimenezi ndizo zidzachitikire mitundu yonse ya dziko lapansi
ndiponso pakati pa mitundu ya anthu.
Zidzakhala ngati pamene mitengo ya olivi yayoyoledwa,
kapena ngati nthawi ya kunkha la mphesa atatsiriza kukolola.
14 Koma otsala onse akufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe;
anthu akumadzulo akutamanda ukulu wa Yehova.
15 Nʼchifukwa chake inu akummawa, tamandani Yehova;
ndi inu okhala mʼmphepete mwa nyanja kwezani dzina la Yehova, Mulungu wa Israeli.
16 Kuchokera kumalekezero a dziko lapansi tikumva kuyimba kotamanda
“Wolungamayo.”
Koma ine ndinati, “Ndatheratu, ndatheratu!
Tsoka kwa ine!
Anthu achinyengo akupitirizabe kuchita zachinyengo,
inde chinyengo chawo chikunkerankera mʼtsogolo.”
Moyo Wokondweretsa Mulungu
4 Potsiriza, abale, tinakulangizani kale momwe mukuyenera kukhalira kuti mukondweretse Mulungu, monga momwe mukukhaliramo. Tsopano tikukupemphani ndi kukulimbikitsani mwa Ambuye Yesu kuti muchite zimenezi koposa kale. 2 Inu mukudziwa malangizo amene tinakupatsani mwa ulamuliro wa Ambuye Yesu.
3 Ndi chifuniro cha Mulungu kuti muyeretsedwe: kuti mupewe dama; 4 aliyense wa inu aphunzire kulamulira thupi lake mʼnjira yoyera ndi yaulemu, 5 osati yotsata chilakolako chonyansa monga amachitira akunja, amene sadziwa Mulungu. 6 Pa zimenezi munthu asachimwire mʼbale wake kapena kumuonerera. Ambuye adzalanga anthu onse amene amachita machimo amenewa, monga tinakuwuzani kale ndi kukuchenjezani. 7 Pakuti Mulungu sanatiyitane kuti tizichita zonyansa, koma kuti tikhale oyera mtima. 8 Choncho, aliyense amene akukana malangizo awa sakukana munthu koma Mulungu, Mulungu weniweniyo amene amakupatsani Mzimu Woyera.
9 Tsono kunena za kukondana wina ndi mnzake, nʼkosafunikira kuti tikulembereni, popeza ndi Mulungu amene anakuphunzitsani za kukondana wina ndi mnzake. 10 Ndipo kunena zoona, mumakonda abale onse a mʼbanja la Mulungu a ku Makedoniya. Komabe, abale tikukulimbikitsani kuti muzichita zimenezi koposa kale.
11 Yesetsani kuti mukhale moyo wofatsa. Aliyense asamale ntchito yakeyake ndi kugwira ntchito ndi manja ake. 12 Mukatero akunja adzalemekeza makhalidwe anu a tsiku ndi tsiku, ndi kuti inuyo mukhale osadalira wina aliyense.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.