Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 119:137-144

Tsade

137 Yehova ndinu wolungama,
    ndipo malamulo anu ndi abwino.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama;
    ndi odalirika ndithu.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga
    chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri
    nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka,
    sindiyiwala malangizo anu.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya,
    ndipo malamulo anu nʼchoona.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera,
    koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse;
    patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.

Habakuku 2:5-11

Ndithu, wasokonezeka ndi vinyo;
    ndi wodzitama ndiponso wosakhazikika.
Pakuti ngodzikonda ngati manda,
    ngosakhutitsidwa ngati imfa,
wadzisonkhanitsira mitundu yonse ya anthu
    ndipo wagwira ukapolo anthu a mitundu yonse.

“Kodi onse ogwidwawo sadzamunyoza ndi kumunyogodola ponena kuti,

“Tsoka kwa amene amadzikundikira katundu amene si wake
    ndipo amadzilemeretsa ndi chuma cholanda!
    Kodi izi zidzachitika mpaka liti?
Kodi angongole ako sadzakuwukira mwadzidzidzi?
    Kodi sadzadzuka ndi kukuchititsa mantha?
    Pamenepo iwe udzalandidwa kalikonse.
Pakuti unafunkha mitundu yambiri ya anthu,
    mitundu ina imene inatsala idzakufunkha iweyo.
Pakuti wakhetsa magazi a anthu;
    wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.

“Tsoka kwa amene amalemera ndi chuma chochipeza mwachinyengo,
    kukweza malo ake okhalapo,
    kuthawa mavuto!
10 Wakonzekera kuwononga mitundu yambiri ya anthu,
    kuchititsa manyazi nyumba yako yomwe ndi kuwononga moyo wako.
11 Mwala pa khoma udzafuwula,
    ndipo mitanda ya matabwa idzavomereza zimenezi.

Yohane 8:39-47

39 Iwo anayankha kuti, “Ife abambo athu ndi Abrahamu.”

Yesu anati, “Inu mukanakhala ana a Abrahamu, bwenzi mukuchita zinthu zimene Abrahamuyo ankachita. 40 Koma mmene zililimu, inu mwatsimikiza kundipha Ine, munthu amene ndinakuwuzani choonadi chimene Ine ndinachimva kuchokera kwa Mulungu. Abrahamu sanachite zinthu zoterezi. 41 Inu mukuchita zinthu zimene abambo anu amachita.”

Iwo anatsutsa kuti, “Ife si ana amʼchigololo, Atate amene tili nawo ndi Mulungu yekha.”

Ana a Mdierekezi

42 Yesu anawawuza kuti, “Mulungu akanakhala Atate anu, inu mukanandikonda Ine, pakuti Ine ndinachokera kwa Mulungu ndipo tsopano ndili pano. Ine sindinabwere mwa Ine ndekha. 43 Nʼchifukwa chiyani simukumvetsetsa mawu anga? Chifukwa chake nʼchakuti simungathe kumva zoyankhula zanga. 44 Inu ndinu ana a mdierekezi. Iye ndiye abambo anu ndipo mukufuna kuchita zimene abambo anuwo amakhumba. Iye anali wakupha kuyambira pachiyambi, sanasunge choonadi, pakuti mwa iye mulibe choonadi. Pamene Iye anena bodza, amayankhula chiyankhulo chobadwa nacho, popeza ndi wabodza ndipo ndi bambo wa mabodza. 45 Koma chifukwa ndikuwuzani choonadi, inu simukundikhulupirira Ine! 46 Ndani mwa inu angatsimikize kuti ndine wochimwa? Ngati Ine ndikunena choonadi, nʼchifukwa chiyani simukundikhulupirira? 47 Munthu wochokera kwa Mulungu amamva zimene Mulungu amanena. Chifukwa chimene simumvera nʼchakuti, inuyo sindinu ochokera kwa Mulungu.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.