Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 142

Ndakatulo ya Davide, pamene iyeyo anali mʼphanga. Pemphero.

142 Ndikulirira Yehova mofuwula;
    ndikukweza mawu anga kwa Yehova kupempha chifundo.
Ndikukhuthula madandawulo anga pamaso pake;
    ndikufotokoza za masautso anga pamaso pake.

Pamene mzimu wanga walefuka mʼkati mwanga,
    ndinu amene mudziwa njira yanga.
Mʼnjira imene ndimayendamo
    anthu anditchera msampha mobisa.
Yangʼanani kumanja kwanga ndipo onani;
    palibe amene akukhudzika nane.
Ndilibe pothawira;
    palibe amene amasamala za moyo wanga.

Ndilirira Inu Yehova;
    ndikuti, “Ndinu pothawirapo panga,
    gawo langa mʼdziko la anthu amoyo.”
Mverani kulira kwanga
    pakuti ndathedwa nzeru;
pulumutseni kwa amene akundithamangitsa
    pakuti ndi amphamvu kuposa ine.
Tulutseni mʼndende yanga
    kuti nditamande dzina lanu.

Ndipo anthu olungama adzandizungulira
    chifukwa cha zabwino zanu pa ine.

Habakuku 2:12-20

12 “Tsoka kwa amene amanga mzinda pokhetsa magazi
    ndi kukhazikitsa mzinda pochita zoyipa!
13 Kodi Yehova Wamphamvuzonse sanatsimikize
    kuti ntchito za anthu zili ngati nkhuni pa moto,
    ndi kuti mitundu ya anthu imadzitopetsa popanda phindu?
14 Pakuti dziko lapansi lidzadzaza ndi chidziwitso cha ulemerero wa Yehova,
    monga momwe madzi amadzazira nyanja.

15 “Tsoka kwa amene amamwetsa anzake zakumwa zoledzeretsa,
    kutsanula mʼbotolo mpaka ataledzera,
    kuti aone umaliseche wawo.
16 Udzachita manyazi mʼmalo mokhala ndi ulemerero.
    Tsopano ino ndi nthawi yako! Imwa mpaka umaliseche wako uwonekere!
Chikho chochokera mʼdzanja lamanja la Yehova chikubwera kwa iwe,
    ndipo manyazi adzaphimba ulemerero wako.
17 Udzathedwa nzeru ndi chiwawa chimene unachita ku Lebanoni,
    ndiponso udzachita mantha ndi nyama zimene unaziwononga.
Pakuti wakhetsa magazi a anthu;
    wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.

18 “Kodi fano lili ndi phindu lanji, poti analisema ndi munthu,
    kapena chifanizo chimene chimaphunzitsa mabodza?
Pakuti munthu amene walipanga amakhulupirira ntchito ya manja ake;
    amapanga mafano amene samatha kuyankhula.
19 Tsoka kwa amene amawuza mtengo kuti, ‘Khala wamoyo!’
    Kapena mwala wopanda moyo kuti, ‘Dzuka!’
Kodi zimenezi zingathe kulangiza?
    Ndi zokutidwa ndi golide ndi siliva;
    mʼkati mwake mulibe mpweya.
20 Koma Yehova ali mʼNyumba yake yopatulika;
    dziko lonse lapansi likhale chete pamaso pake.”

1 Akorinto 5:9-13

Ndakulemberani mʼkalata yanga kuti musayanjane nawo anthu achigololo. 10 Pamenepatu sindikutanthauzatu anthu a dziko lapansi lino amene ndi achigololo, kapena aumbombo, kapena opeza ndalama mwachinyengo, kapena opembedza mafano. Kukanatero mukanangochoka mʼdziko lapansi lino. 11 Koma tsopano ndikukulemberani kuti musayanjane ndi aliyense amene adzitcha mʼbale koma ndi wachigololo, kapena waumbombo, kapena wopembedza mafano, kapena wonamizira anzake, woledzera kapena wopeza ndalama mwachinyengo. Munthu wotere ngakhale kudya, osadya naye pamodzi.

12 Kodi ndipindulanji kuti ndiweruze anthu amene si a mu mpingo? Kodi simuyenera kuweruza iwo amene ali mu mpingo? 13 Mulungu adzaweruza akunja. “Chotsani woyipayo pakati panu.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.