Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 117

117 Tamandani Yehova, inu anthu a mitundu yonse;
    mulemekezeni Iye, inu mitundu ya anthu.
Pakuti chikondi chake pa ife ndi chachikulu,
    ndipo kukhulupirika kwa Yehova nʼkosatha.

Tamandani Yehova.

Yeremiya 31:1-6

31 “Pa nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “Ndidzakhala Mulungu wa mafuko onse a Israeli, ndipo iwo adzakhala anthu anga.”

Yehova akuti,

“Anthu amene anapulumuka ku nkhondo
    ndinawakomera mtima mʼchipululu;
    pamene Aisraeli ankafuna kupumula.”

Ine ndinawaonekera ndili chapatali ndipo ndinati,

“Ine ndakukondani ndi chikondi chopanda malire.
    Nʼchifukwa chake ndipitiriza kukukondani.
Ndidzakusamaliraninso, inu anthu a Israeli;
    mudzasangalala poyimba tizitoliro tanu,
ndipo mudzapita kukavina nawo
    anthu ovina mwachimwemwe.
Mudzalimanso minda ya mpesa
    pa mapiri a Samariya;
alimi adzadzala mphesa
    ndipo adzadya zipatso zake.
Lidzafika tsiku pamene alonda adzafuwula
    pa mapiri a Efereimu nati,
‘Tiyeni tipite ku Ziyoni,
    kwa Yehova Mulungu wathu.’ ”

Luka 1:1-4

Mawu Oyamba

Ambiri anayesa kufotokoza nkhani ya zimene zinakwaniritsidwa pakati pathu, monga mmene zinaperekedwera kwa ife ndi iwo amene anaona poyambirira ndi atumiki a mawu. Popeza inenso ndafufuza mosamalitsa chilichonse kuyambira pachiyambi, zandikomera kukulemberani mwatsatanetsatane inu wolemekezeka Tiofilo, kuti mudziwe bwinobwino zoona za zinthu zimene mwaphunzitsidwa.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.