Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Nyimbo za Mayamiko
12 Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati:
“Ndikukuyamikani, Inu Yehova;
chifukwa ngakhale munandipsera mtima,
mkwiyo wanu wachoka,
ndipo mwanditonthoza.
2 Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga;
ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;
Iye wakhala chipulumutso changa.”
3 Mudzakondwera popeza Yehova
ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.
4 Tsiku limenelo mudzati:
“Yamikani Yehova, tamandani dzina lake;
mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu,
ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.
5 Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu;
zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.
6 Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni;
pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”
Tchimo, Kuvomereza ndi Chipulumutso
59 Taonani, mkono wa Yehova si waufupi kuti sungathe kupulumutsa,
kapena khutu lake kuti ndilogontha kuti sangamve.
2 Koma zoyipa zanu zakulekanitsani
ndi Mulungu wanu;
ndipo wakufulatirani chifukwa cha machimo anu,
kotero Iye sadzamva.
3 Pakuti manja anu ali psuu ndi magazi.
Munayipitsa zala zanu ndi zamphulupulu.
Pakamwa panu payankhula zabodza,
ndipo lilime lanu lanena zinthu zoyipa.
4 Palibe amene akuyimba mnzake mlandu molungama,
palibe amene akupita ku mlandu moona mtima.
Iwo amadalira mawu opanda pake ndipo amayankhula mabodza;
amalingalira za mphulupulu ndipo amachita zoyipa.
5 Iwo amayikira mazira a mamba
ndipo amaluka ukonde wakangawude.
Aliyense amene adzadya mazira awo adzafa,
ndipo ngati dzira limodzi lasweka limatulutsa mphiri.
6 Ukonde wawo wa kangawude sangawuvale ngati chovala;
ndipo chimene apangacho sangachifunde.
Ntchito zawo ndi zoyipa,
ndipo amakonda kuchita zandewu ndi manja awo.
7 Amathamangira kukachita zoyipa;
sachedwa kupha anthu osalakwa.
Maganizo awo ndi maganizo oyipa;
kulikonse kumene amapita amasiyako bwinja ndi chiwonongeko.
8 Iwo sadziwa kuchita za mtendere;
zonse zimene amachita nʼzopanda chilungamo.
Njira zawo zonse nʼzokhotakhota;
aliyense oyenda mʼnjira zimenezo sadzapeza mtendere.
9 Anthu akuti, “Chifukwa cha zimenezi chilungamo chatitalikira;
ndipo chipulumutso sichitifikira.
Timafunafuna kuwala koma timangopeza mdima okhaokha;
tinayembekezera kuyera koma timayenda mu mdima wandiweyani.
10 Timapapasapapasa khoma ngati munthu wosaona,
kuyangʼanayangʼana njira ngati anthu opanda maso.
Timapunthwa dzuwa lili paliwombo ngati kuti ndi usiku;
timakhala pansi mu mdima ngati anthu akufa.
11 Tonse timabangula ngati zimbalangondo:
Timalira modandaula ngati nkhunda.
Tinayembekezera kuweruza kolungama; koma sitikupeza.
Timayembekezera chipulumutso koma chimakhala nafe kutali.”
12 Pakuti zolakwa zathu nʼzochuluka pamaso panu,
ndipo machimo athu akutsutsana nafe.
Zolakwa zathu zili ndi ife nthawi zonse
ndipo tikuvomereza machimo athu:
13 Tawukira ndi kumukana Yehova.
Tafulatira Mulungu wathu,
pa kupondereza anzathu ndi kupandukira Yehova,
ndi pa kuyankhula mabodza amene tawaganiza mʼmitima mwathu.
14 Motero kuweruza kolungama kwalekeka
ndipo choonadi chili kutali ndi ife;
kukhulupirika sikukupezekanso mʼmabwalo a milandu,
ndipo kuona mtima sikukupezekanso mʼmenemo.
15 Choonadi sichikupezeka kumeneko,
ndipo wina akakana kuchita nawo zoyipa amapeza mavuto.
Yehova anaziona zimenezi ndipo zinamunyansa
kuti panalibe chiweruzo cholungama.
Kuyamika ndi Pemphero
3 Ife tiyenera kuyamika Mulungu nthawi zonse chifukwa cha inu abale. Ndipo tiyenera kutero chifukwa chikhulupiriro chanu chikukulirakulirabe, ndiponso chikondi chimene aliyense wa inu ali nacho pa mnzake chikuchulukirachulukirabe. 4 Nʼchifukwa chake, timayankhula monyadira mʼmipingo yonse ya Mulungu za kupirira kwanu ndi chikhulupiriro chanu pakati pa masautso onse ndi mayesero amene mukudutsamo.
5 Zonsezi zikutsimikiza kuti Mulungu amaweruza molungama. Zotsatira zake ndi zakuti mudzatengedwa kukhala oyenera kulowa mu ufumu wa Mulungu umene mukuwuvutikira. 6 Mulungu ndi wolungama ndipo adzalanga amene amakusautsaniwo 7 ndikukupatsani mpumulo amene mukusautsidwa, pamodzi ndi ifenso. Izi zidzachitika Ambuye Yesu akadzaoneka mʼmalawi amoto kuchokera kumwamba pamodzi ndi angelo ake amphamvu. 8 Iye adzalanga amene sadziwa Mulungu ndi amene samvera Uthenga Wabwino wa Ambuye athu Yesu. 9 Adzalangidwa ndi chiwonongeko chamuyaya ndipo sadzaonanso nkhope ya Ambuye ndi ulemerero wamphamvu zake 10 pa tsiku limene iye adzabwera kudzalemekezedwa mwa oyera mtima ndi kuyamikidwa ndi onse amene anakhulupirira. Inu mudzakhala nawo mʼgulumo chifukwa munakhulupirira umboni wathu.
11 Nʼchifukwa chake timakupemphererani nthawi zonse, kuti Mulungu wathu akusandutseni oyenera mayitanidwe ake, ndi kuti mwa mphamvu zake akwaniritse cholinga chanu chilichonse chabwino ndi chilichonse chochitika mwachikhulupiriro. 12 Ife timapempherera zimenezi kuti dzina la Ambuye athu Yesu lilemekezedwe mwa inu, ndi inu mulemekezedwe mwa Iyeyo. Zonsezi zidzachitika chifukwa cha chisomo cha Mulungu wathu ndi Ambuye Yesu Khristu.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.