Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Za Ufumu Wamtendere wa Mesiya
11 Padzatuluka mphukira pa tsinde la Yese
ndipo nthambi idzaphukira kuchokera ku mizu yake.
2 Mzimu wa Yehova udzakhala pa iye
Mzimu wanzeru ndi wa kumvetsa zinthu,
Mzimu wauphungu ndi wamphamvu,
Mzimu wachidziwitso ndi wakuopa Yehova.
3 Ndipo kuopa Yehova ndiye chidzakhale chinthu chomukondweretsa.
Iye sadzaweruza potsata zooneka pamaso,
kapena kugamula mlandu potsata zakumva;
4 koma amphawi adzawaweruza mwachilungamo,
adzaweruza mwachilungamo mlandu wa anthu osauka a dziko lapansi.
Iye adzakantha dziko lapansi ndi mawu ake;
atalamula Iyeyu anthu oyipa adzaphedwa.
5 Chilungamo chidzakhala ngati lamba wake
ndipo kukhulupirika kudzakhala ngati chomangira mʼchiwuno mwake.
6 Mʼmbulu udzakhala pamodzi ndi mwana wankhosa,
kambuku adzagona pansi pamodzi ndi mwana wambuzi,
mwana wangʼombe ndi mwana wa mkango adzadyera limodzi
ndipo mwana wamngʼono adzaziweta.
7 Ngʼombe yayikazi ndi chimbalangondo zidzadya pamodzi,
ana awo adzagona pamodzi,
ndipo mkango udzadya udzu ngati ngʼombe.
8 Mwana wakhanda adzasewera pa dzenje la mamba,
ndipo mwana wamngʼono adzapisa dzanja lake ku phanga la mphiri osalumidwa.
9 Sipadzakhala chilichonse chopweteka kapena chowononga
pa phiri lopatulika la Yehova,
pakuti anthu a dziko lapansi adzadzaza ndi nzeru yotha kudziwa Yehova
monga momwe nyanja imadzazira ndi madzi.
10 Tsiku limenelo mfumu yatsopano yochokera pa Muzu wa Yese idzakhala ngati chizindikiro kwa anthu a mitundu yonse. Mitundu ya anthu idzasonkhana kwa Iye, ndipo malo awo okhalapo adzakhala aulemerero.
Salimo la Solomoni.
72 Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo,
Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.
2 Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo,
anthu anu ozunzika mosakondera.
3 Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu,
timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.
4 Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu
ndi kupulumutsa ana a anthu osowa;
adzaphwanya ozunza anzawo.
5 Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse,
nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.
6 Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa
ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.
7 Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika;
chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.
18 Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli
amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.
19 Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya
dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake.
Ameni ndi Ameni.
4 Pakuti zilizonse zimene zinalembedwa kale zinalembedwa kuti zitiphunzitse ife. Malembawo amatilimbikitsa kupirira kuti tikhale ndi chiyembekezo.
5 Mulungu amene amapereka kupirira ndi chilimbikitso akupatseni maganizo amodzi pakati panu monga inu mukutsatira Khristu Yesu, 6 kotero kuti ndi mtima umodzi ndi movomerezana mulemekeze Mulungu ndi Atate a Ambuye athu Yesu Khristu.
7 Tsopano landiranani wina ndi mnzake, monganso Khristu anakulandirani inu, ndi cholinga choti Mulungu alemekezeke. 8 Chifukwa kunena zoona, Khristu wasanduka mtumiki wa Ayuda, kuonetsa kuti Mulungu ndi wokhulupirika pa malonjezo amene anachita kwa makolo awo 9 kuti a mitundu ina atamande Mulungu chifukwa cha chifundo chake. Monga kwalembedwa kuti,
“Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa a mitundu;
ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.”
10 Akutinso,
“Kondwerani inu anthu a mitundu ina pamodzi ndi anthu ake.”
11 Ndipo akutinso,
“Tamandani Ambuye, inu nonse a mitundu ina,
ndi kuyimba zotamanda Iye, inu anthu onse.”
12 Ndiponso Yesaya akuti,
“Muzu wa Yese udzaphuka,
wina amene adzauka kulamulira anthu a mitundu ina;
mwa Iye mudzakhala chiyembekezo cha a mitundu ina.”
13 Mulungu amene amatipatsa chiyembekezo adzaze mitima yanu ndi chimwemwe ndi mtendere pamene mukumudalira Iye, kuti chiyembekezo chanu chisefukire mwamphamvu ya Mzimu Woyera.
Yohane Mʼbatizi
3 Mʼmasiku amenewo, Yohane Mʼbatizi anadza nalalikira mʼchipululu cha Yudeya 2 kuti, “Tembenukani mtima chifukwa ufumu wakumwamba wayandikira.” 3 Uyu ndi amene mneneri Yesaya ananena za iye kuti,
“Mawu a wofuwula mʼchipululu,
‘Konzani njira ya Ambuye,
wongolani njira zake.’ ”
4 Zovala za Yohane zinali zopangidwa ndi ubweya wa ngamira, ndipo amamangira lamba wachikopa mʼchiwuno mwake. Chakudya chake chinali dzombe ndi uchi wa kuthengo. 5 Anthu ankapita kwa iye kuchokera ku Yerusalemu ndi ku Yudeya konse ndi ku madera onse a Yorodani. 6 Ndipo akavomereza machimo awo ankabatizidwa mu mtsinje wa Yorodani.
7 Koma iye ataona Afarisi ndi Asaduki ambiri akubwera kumene ankabatiza, anawawuza kuti, “Ana a njoka inu! Ndani anakuchenjezani kuthawa mkwiyo umene ukubwera? 8 Onetsani chipatso cha kutembenuka mtima. 9 Ndipo musaganize ndi kunena mwa inu nokha kuti, ‘Tili nawo abambo athu Abrahamu.’ Ndinena kwa inu kuti Mulungu akhoza kusandutsa miyala iyi kukhala ana a Abrahamu. 10 Tikukamba pano nkhwangwa yayikidwa kale pa mizu ya mitengo, ndipo mtengo umene subala chipatso chabwino udulidwa ndi kuponyedwa pa moto.
11 “Ine ndikubatizani ndi madzi kusonyeza kutembenuka mtima. Koma pambuyo panga akubwera wina amene ali ndi mphamvu kuposa ine, amene sindiyenera kunyamula nsapato zake. Iyeyu adzakubatizani ndi Mzimu Woyera ndi moto. 12 Mʼdzanja lake muli chopetera ndipo adzayeretsa popunthirapo pake nadzathira tirigu wake mʼnkhokwe ndi kutentha zotsalira zonse ndi moto wosazima.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.