Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 20

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

20 Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso;
    dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.
Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika;
    akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.
Iye akumbukire nsembe zako zonse
    ndipo alandire nsembe zako zopsereza.
            Sela
Akupatse chokhumba cha mtima wako
    ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.
Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana
    ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu,
Yehova ayankhe zopempha zako zonse.

Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake;
    Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika
    ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.
Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo
    koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.
Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa,
    koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.

Inu Yehova, pulumutsani mfumu!
    Tiyankheni pamene tikuyitanani!

Yeremiya 31:15-22

15 Yehova akuti,

“Kulira kukumveka ku Rama,
    kulira kwakukulu,
Rakele akulirira ana ake.
    Sakutonthozeka
    chifukwa ana akewo palibe.”

16 Yehova akuti,

“Leka kulira
    ndi kukhetsa misozi
pakuti udzalandira mphotho ya ntchito yako,”
            akutero Yehova.
    “Iwo adzabwerako ku dziko la adani.
17 Tsono chiyembekezo chilipo pa zamʼtsogolo,”
            akutero Yehova.
    “Ana ako adzabwerera ku dziko lawo.

18 “Ndithu ndamva Efereimu akubuwula kuti,
    ‘Ife tinali ngati ana angʼombe osamva.
    Koma inu mwatiphunzitsa kumvera.
Mutibweze kuti tithe kubwerera,
    chifukwa ndinu Yehova Mulungu wanga.
19 Popeza tatembenuka mtima,
    ndiye tikumva chisoni;
popeza tazindikira
    ndiye tikudziguguda pachifukwa.
Tachita manyazi ndipo tanyazitsidwa
    chifukwa tinachimwa paubwana wathu.’
20 Kodi Efereimu si mwana wanga wokondedwa,
    mwana amene Ine ndimakondwera naye?
Ngakhale nthawi zambiri ndimamudzudzula,
    ndimamukumbukirabe.
Kotero mtima wanga ukumufunabe;
    ndimamumvera chifundo chachikulu kwambiri,”
            akutero Yehova.

21 “Muyike zizindikiro za mu msewu;
    muyimike zikwangwani.
Yangʼanitsitsani msewuwo,
    njira imene mukuyendamo.
Bwerera, iwe namwali wa Israeli,
    bwerera ku mizinda yako ija.
22 Udzakhala jenkha mpaka liti,
    iwe mwana wa mkazi wosakhulupirika?
Yehova walenga chinthu chatsopano pa dziko lapansi; mkazi ndiye tsopano aziteteza mwamuna.”

Luka 19:41-44

41 Iye atayandikira ku Yerusalemu ndi kuona mzindawo, anawulirira 42 nati, “Iwe ukanadziwa lero lino zinthu zokubweretsera mtendere, koma tsopano zabisikira maso ako. 43 Pakuti masiku adzabwera pamene adani ako adzamanga mitumbira yankhondo nakuzungulira, nadzakutsekereza mbali zonse. 44 Iwo adzakugwetsera pansi, iwe, ana ako onse a mʼkati mwako. Iwo sadzasiya mwa iwe mwala wina pa unzake, chifukwa sunazindikire nthawi ya kubwera kwa Mulungu.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.