Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo.
67 Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa,
achititse kuti nkhope yake itiwalire.
2 Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi,
chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
3 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu;
mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
4 Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe,
pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo
ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
5 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu;
mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
6 Nthaka yabereka zokolola zake;
tidalitseni Mulungu wathu.
7 Mulungu atidalitse
kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.
Ubwino Wanzeru
2 Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga
ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
2 ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru
ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
3 ngati upempha kuti uzindikire zinthu
inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
4 ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva
ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
5 ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova;
ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
Paulo Asiyana ndi Barnaba
36 Patapita masiku ena Paulo anati kwa Barnaba, “Tiyeni tibwerere kuti tikaone abale ku mizinda yonse imene tinalalika Mawu a Ambuye ndipo tikaone mmene akuchitira.” 37 Barnaba anafuna kutenga Yohane, wotchedwanso Marko, kuti apite nawo. 38 Koma Paulo anaganiza kuti sichinali cha nzeru kumutenga Yohane chifukwa iye anawathawa ku Pamfiliya ndipo sanapitirire nawo pa ntchito. 39 Iwo anatsutsana kwambiri kotero kuti anapatukana. Barnaba anatenga Marko ndipo anakwera sitima ya pamadzi kupita ku Kupro. 40 Paulo anasankha Sila. Abale atawapempherera kwa Ambuye kuti alandire chisomo, ananyamuka. 41 Iye anadutsa ku Siriya ndi ku Kilikiya kupita akulimbikitsa mipingo.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.