Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Salimo. Nyimbo yothokoza.
100 Fuwulani kwa Yehova mwachimwemwe, inu dziko lonse lapansi.
2 Mulambireni Yehova mosangalala;
bwerani pamaso pake ndi nyimbo zachikondwerero.
3 Dziwani kuti Yehova ndi Mulungu.
Iye ndiye amene anatipanga ndipo ife ndife ake;
ndife anthu ake, nkhosa za pabusa pake.
4 Lowani ku zipata zake ndi chiyamiko
ndi ku mabwalo ake ndi matamando;
muyamikeni ndi kutamanda dzina lake.
5 Pakuti Yehova ndi wabwino ndipo chikondi chake ndi chamuyaya;
kukhulupirika kwake nʼkokhazikika pa mibado ndi mibado.
17 “Aisraeli ali ngati nkhosa zomwe zabalalika
pothamangitsidwa ndi mikango.
Mfumu ya ku Asiriya ndiye inayamba kuwapha Aisraeliwo.
Wotsiriza anali Nebukadinezara
mfumu ya ku Babuloni
amene anachita ngati kuphwanya mafupa ake.”
18 Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti,
“Ndidzalanga mfumu ya ku Babuloni pamodzi ndi dziko lake
monga momwe ndinalangira mfumu ya ku Asiriya.
19 Koma ndidzabwezera Israeli ku msipu wake
ndipo adzadya mʼminda ya ku Karimeli ndi Basani;
adzadya nakhuta ku mapiri
a ku Efereimu ndi Giliyadi.
20 Masiku amenewo, nthawi imeneyo,”
akutero Yehova,
“anthu adzafunafuna zolakwa za Israeli
koma sadzapeza nʼchimodzi chomwe,
ndipo adzafufuza machimo a Yuda,
koma sadzapeza ndi limodzi lomwe,
chifukwa otsala amene ndawasiya ndidzawakhululukira.
31 Ayuda anatolanso miyala kuti amugende Iye, 32 koma Yesu anawawuza kuti, “Ine ndakuonetsani zinthu zambiri zabwino zodabwitsa kuchokera kwa Atate. Nʼchifukwa chiti mwa izi chimene mukundigendera?”
33 Ayuda anayankha kuti, “Ife sitikukugenda chifukwa cha izi, koma popeza ukunyoza Mulungu, chifukwa iwe, munthu wamba, ukuti ndiwe Mulungu.”
34 Yesu anawayankha kuti, “Kodi sizinalembedwa mʼmalamulo anu kuti, ‘Ine ndanena kuti ndinu milungu?’ 35 Ngati anawatcha milungu anthu amene analandira mawu a Mulungu, pajatu Malemba sangasweke, 36 nanga bwanji uyu amene Atate anamuyika padera monga wake weniweni ndi kumutuma ku dziko lapansi? Nanga ndi chifukwa chiyani mukundinena Ine kuti ndikuchita chipongwe? Kodi nʼchifukwa choti ndanena kuti, ‘Ine ndine Mwana wa Mulungu?’ 37 Musandikhulupirire Ine ngati sindichita ntchito za Atate anga. 38 Koma ngati Ine ndikuchita zimenezi, ngakhale kuti simundikhulupirira, khulupirirani ntchito zodabwitsazo, ndipo mudziwe ndi kuzindikira kuti Atate ali mwa Ine, ndiponso Ine ndili mwa Atate.” 39 Iwo anafuna kumugwiranso koma anawapulumuka mʼmanja mwawo.
40 Kenaka Yesu anabwereranso kutsidya la mtsinje wa Yorodani kumalo kumene Yohane ankabatiza mʼmasiku akale. Iye anakhala kumeneko 41 ndipo anthu ambiri anabwera kwa Iye. Iwo anati, “Ngakhale kuti Yohane sanachite chizindikiro chodabwitsa, zonse zimene Yohane ananena za munthu uyu zinali zoona.” 42 Ndipo pamalo amenewo ambiri anakhulupirira Yesu.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.