Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba popereka Nyumba ya Mulungu.
30 Ndidzakukwezani Yehova,
chifukwa mwanditulutsa kwakuya,
ndipo simunalole kuti adani anga akondwere pa ine.
2 Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo
ndipo Inu munandichiritsa.
3 Inu Yehova, munanditulutsa ku manda,
munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje.
4 Imbirani Yehova inu anthu ake okhulupirika;
tamandani dzina lake loyera.
5 Pakuti mkwiyo wake umakhala kwa kanthawi
koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse;
utha kuchezera kulira usiku wonse,
koma chimwemwe chimabwera mmawa.
6 Pamene ndinaona kuti ndili otetezedwa ndinati,
“Sindidzagwedezekanso.”
7 Inu Yehova, pamene munandikomera mtima,
munachititsa phiri langa kuyima chilili;
koma pamene munabisa nkhope yanu,
ndinataya mtima.
8 Kwa Inu Yehova ndinayitana;
kwa Ambuye ndinapempha chifundo;
9 “Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga
ngati nditsikira ku dzenje?
Kodi fumbi lidzakutamandani Inu?
Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu?
10 Imvani Yehova ndipo mundichitire chifundo;
Yehova mukhale thandizo langa.”
11 Inu munasandutsa kulira kwanga kukhala kuvina;
munachotsa chiguduli changa ndi kundiveka ndi chimwemwe,
12 kuti mtima wanga uthe kuyimbira Inu usakhale chete.
Yehova Mulungu wanga, ndidzapereka kwa Inu mayamiko kwamuyaya.
Alendo Atatu a Abrahamu
18 Yehova anadza kwa Abrahamu pafupi ndi mitengo ikuluikulu ya thundu ya ku Mamre. Abrahamu nʼkuti atakhala pansi pa khoma la tenti yake masana, dzuwa likutentha. 2 Tsono Abrahamu atakweza maso ake patali anangoona anthu atatu atayima cha potero. Atawaona, ananyamuka mofulumira kuti awachingamire. Atafika anaweramitsa mutu pansi mwa ulemu nati, 3 “Ngati mwandikomera mtima, mbuye wanga, musamulambalale mtumiki wanu. 4 Ndikupatseniko timadzi pangʼono kuti nonse musambitse mapazi anu ndi kupumula pansi pa mtengo uwu. 5 Tsono ndikutengereniko kachakudya kuti mudye kuti mwina nʼkupezako mphamvu zopitirizira ulendo wanu. Inu mwafika kumalo kwa mtumiki wanu.”
Ndipo iwo anamuyankha nati, “Zikomo kwambiri, chita monga wanenera.”
6 Choncho Abrahamu anafulumira kupita kwa Sara mʼtenti nati, “Tafulumira, tenga mabeseni atatu a ufa wosalala, ukande ndi kupanga buledi.”
7 Kenaka Abrahamu anakatenga mwana wangʼombe wonenepa ndi wofewa bwino ndi kupatsa wantchito wake amene anachita changu kukonza ndiwoyo. 8 Tsono Abrahamu anatenga chambiko, mkaka ndi mwana wangʼombe wokonzedwa uja nazipereka kwa anthu aja. Alendowo akudya, Abrahamu ankawayangʼana atayimirira pansi pa mtengo.
12 Kenaka Yesu anati kwa mwini malo uja, “Ukakonza chakudya chamasana kapena chamadzulo, usamayitane abwenzi ako, abale ako, anthu afuko lako kapena anzako achuma; ngati iwe utero, iwo adzakuyitananso, choncho udzalandiriratu mphotho yako. 13 Koma ukakonza phwando, itana anthu osauka, ofa ziwalo, olumala ndi osaona. 14 Pamenepo udzakhala wodala, chifukwa iwo sangakubwezere kanthu, koma Mulungu ndiye adzakubwezera pa chiukitso cha olungama.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.